< Yesaya 9 >
1 Anthu amene anali ndi nkhawa, sadzakhalanso otaya mtima. Masiku amakedzana Mulungu ananyozetsa dziko la Zebuloni ndi dziko la Nafutali, koma kutsogolo kuno dera lonse la Galileya, limene lili dziko la anthu a mitundu ina, kuyambira ku nyanja yayikulu, mʼmbali mwa Yorodani, adzalisandutsa laulemu.
Mutta ei jää pimeään se, mikä nyt on vaivan alla. Entiseen aikaan hän saattoi halveksituksi Sebulonin maan ja Naftalin maan, mutta tulevaisuudessa hän saattaa kunniaan merentien, Jordanin tuonpuoleisen maan, pakanain alueen.
2 Anthu oyenda mu mdima awona kuwala kwakukulu; kwa iwo okhala mʼdziko la mdima wandiweyani kuwunika kwawafikira.
Kansa, joka pimeydessä vaeltaa, näkee suuren valkeuden; jotka asuvat kuoleman varjon maassa, niille loistaa valkeus.
3 Inu mwauchulukitsa mtundu wanu ndipo mwawonjezera chimwemwe chawo. Iwo akukondwa pamaso panu, ngati mmene anthu amakondwera nthawi yokolola, ngatinso mmene anthu amakondwera pamene akugawana zolanda ku nkhondo.
Sinä lisäät kansan, annat sille suuren ilon; he iloitsevat sinun edessäsi, niinkuin elonaikana iloitaan, niinkuin saaliinjaossa riemuitaan.
4 Monga munachitira pogonjetsa Amidiyani, inu mwathyola goli limene limawalemera, ndodo zimene amamenyera mapewa awo, ndiponso mikwapulo ya anthu owazunza.
Sillä heidän kuormansa ikeen, heidän olkainsa vitsan ja heidän käskijänsä sauvan sinä särjet niinkuin Midianin päivänä;
5 Nsapato iliyonse ya munthu wankhondo, ndiponso chovala chilichonse chodonthekera magazi zidzatenthedwa pa moto ngati nkhuni.
ja kaikki taistelun pauhussa tallatut sotakengät ja verellä tahratut vaipat poltetaan ja tulella kulutetaan.
6 Chifukwa mwana watibadwira, mwana wamwamuna wapatsidwa kwa ife, ndipo ulamuliro udzakhala pa phewa lake. Ndipo adzamutcha dzina lake lakuti Phungu Wodabwitsa, Mulungu Wamphamvu, Atate Amuyaya, ndi Mfumu ya Mtendere.
Sillä lapsi on meille syntynyt, poika on meille annettu, jonka hartioilla on herraus, ja hänen nimensä on: Ihmeellinen neuvonantaja, Väkevä Jumala, Iankaikkinen isä, Rauhanruhtinas.
7 Ulamuliro ndi mtendere wake zidzakhala zopanda malire. Iye adzalamulira ufumu wake ali pa mpando waufumu wa Davide, ndipo adzawukhazikitsa ndi kuwuchirikiza mwa chiweruzo cholungama ndi pochita zachilungamo kuyambira nthawi imeneyo mpaka muyaya. Ndi mtima wake wonse, Yehova Wamphamvuzonse watsimikiza kuchita zimenezi.
Herraus on oleva suuri ja rauha loppumaton Daavidin valtaistuimella ja hänen valtakunnallansa; se perustetaan ja vahvistetaan tuomiolla ja vanhurskaudella nyt ja iankaikkisesti. Herran Sebaotin kiivaus on sen tekevä.
8 Ambuye atumiza mawu otsutsa Yakobo; ndipo mawuwo agwera pa Israeli.
Herra lähetti sanan Jaakobia vastaan, ja se iski Israeliin,
9 Anthu onse okhala mu Efereimu ndi okhala mu Samariya, adzadziwa zimenezi. Iwo amayankhula modzikuza kuti,
ja sen sai tuntea koko kansa, Efraim ja Samarian asukkaat, mutta he sanoivat ylpeydessään ja sydämensä kopeudessa:
10 “Ngakhale njerwa zagumuka, koma ife tidzamanga ndi miyala yosema. Mitanda ya mkuyu yagwetsedwa, koma ife tidzayika mitanda ya mkungudza mʼmalo mwake.”
"Tiilikivet sortuivat maahan, mutta me rakennamme hakatuista kivistä; metsäviikunapuut lyötiin poikki, mutta me panemme setripuita sijaan".
11 Koma Yehova wadzutsa adani kuti alimbane nawo ndipo wawafulumiza adani awo kuti amenyane nawo.
Silloin Herra nostatti sitä vastaan Resinin ahdistajat ja kiihoitti sen viholliset,
12 Asiriya ochokera kummawa ndi Afilisti ochokera kumadzulo ndipo ayasama pakamwa kuti adye a Israeli. Komabe, mkwiyo wake sunawachokere, mkono wake uli chitambasulire.
aramilaiset edestä ja filistealaiset takaa, ja he söivät Israelia suun täydeltä. Kaikesta tästä ei hänen vihansa ole asettunut, ja vielä on hänen kätensä ojennettu.
13 Koma anthu sanabwerere kwa amene anawakantha uja, ngakhale kufunafuna Yehova Wamphamvuzonse.
Mutta kansa ei palannut kurittajansa tykö, eivätkä he etsineet Herraa Sebaotia.
14 Choncho Yehova adzadula mutu wa Israeli pamodzi ndi mchira womwe, nthambi ya kanjedza ndi bango lomwe tsiku limodzi;
Sentähden Herra katkaisi Israelilta pään ja hännän, palmunlehvän ja kaislan, yhtenä päivänä.
15 mutuwo ndiye akuluakulu ndi olemekezeka, mchira ndiye aneneri ophunzitsa zabodza.
Vanhin ja arvomies on pää, mutta profeetta, joka valhetta opettaa, on häntä.
16 Amene amatsogolera anthuwa ndiwo amawasocheretsa, ndipo otsogoleredwa amatayika.
Ja tämän kansan johtajat tulivat eksyttäjiksi, ja johdettavat joutuivat hämminkiin.
17 Nʼchifukwa chake Ambuye adzakondwera nawo achinyamata, ngakhale kuwachitira chifundo ana amasiye ndi akazi amasiye, pakuti aliyense ndi wosapembedza Mulungu ndiponso ndi wochimwa ndipo aliyense amayankhula zopusa. Komabe, mkwiyo wake sunawachokere, mkono wake uli chitambasulire.
Sentähden Herra ei iloitse sen nuorista miehistä eikä armahda sen orpoja ja leskiä, sillä he ovat kaikki jumalattomia ja pahantekijöitä, ja jokainen suu puhuu hulluutta. Kaikesta tästä ei hänen vihansa ole asettunut, ja vielä on hänen kätensä ojennettu.
18 Ndithu kuyipa kwa anthuwo kumayaka ngati moto; moto wake umanyeketsa mkandankhuku ndi minga, umayatsa nkhalango yowirira, ndipo utsi wake umachita kuti toloo ngati mtambo.
Sillä jumalattomuus palaa tulena, kuluttaa orjantappurat ja ohdakkeet ja sytyttää sankan metsän, niin että se savuna tupruaa ilmaan.
19 Dziko lidzatenthedwa ndi ukali wa Yehova Wamphamvuzonse, dziko lidzatenthedwa ndipo anthu adzakhala ngati nkhuni zosonkhera moto; palibe munthu amene adzachitire chifundo mʼbale wake.
Herran Sebaotin vihasta maa syttyy palamaan, ja kansa on kuin tulen syötävänä; toinen ei sääli toistansa.
20 Kudzanja lamanja adzapeza chakudya nʼkudya, koma adzakhalabe ndi njala; kudzanja lamanzere adzapeza chakudya nʼkudya, koma sadzakhuta. Aliyense azidzadya ana ake omwe.
Ahmivat oikealta, mutta on yhä nälkä, syövät vasemmalta, mutta eivät saa kylläänsä; jokainen syö oman käsivartensa lihaa:
21 Manase adzadya Efereimu ndipo Efereimu adzadya Manase; onsewa pamodzi adzadya Yuda. Komabe pa zonsezi, mkwiyo wake sunawachokere, mkono wake uli chitambasulire.
Manasse Efraimia ja Efraim Manassea, molemmat yhdessä käyvät Juudan kimppuun. Kaikesta tästä ei hänen vihansa ole asettunut, ja vielä on hänen kätensä ojennettu.