< Yesaya 9 >
1 Anthu amene anali ndi nkhawa, sadzakhalanso otaya mtima. Masiku amakedzana Mulungu ananyozetsa dziko la Zebuloni ndi dziko la Nafutali, koma kutsogolo kuno dera lonse la Galileya, limene lili dziko la anthu a mitundu ina, kuyambira ku nyanja yayikulu, mʼmbali mwa Yorodani, adzalisandutsa laulemu.
The gloom will be dispelled from her who was in anguish. In an earlier time he humiliated the land of Zebulun and the land of Naphtali, but in the later time he will make it glorious, the way to the sea, beyond the Jordan, Galilee of the nations.
2 Anthu oyenda mu mdima awona kuwala kwakukulu; kwa iwo okhala mʼdziko la mdima wandiweyani kuwunika kwawafikira.
The people who walked in darkness have seen a great light; those who have lived in the land of the shadow of death, the light has shone on them.
3 Inu mwauchulukitsa mtundu wanu ndipo mwawonjezera chimwemwe chawo. Iwo akukondwa pamaso panu, ngati mmene anthu amakondwera nthawi yokolola, ngatinso mmene anthu amakondwera pamene akugawana zolanda ku nkhondo.
You have multiplied the nation; you have increased their joy. They rejoice before you like the joy at harvest time, as men rejoice when they divide the plunder.
4 Monga munachitira pogonjetsa Amidiyani, inu mwathyola goli limene limawalemera, ndodo zimene amamenyera mapewa awo, ndiponso mikwapulo ya anthu owazunza.
For the yoke of his burden, the beam across his shoulder, the rod of his oppressor, you have shattered as on the day of Midian.
5 Nsapato iliyonse ya munthu wankhondo, ndiponso chovala chilichonse chodonthekera magazi zidzatenthedwa pa moto ngati nkhuni.
For every boot treading in the tumult and the garments rolled in blood will be burned, fuel for the fire.
6 Chifukwa mwana watibadwira, mwana wamwamuna wapatsidwa kwa ife, ndipo ulamuliro udzakhala pa phewa lake. Ndipo adzamutcha dzina lake lakuti Phungu Wodabwitsa, Mulungu Wamphamvu, Atate Amuyaya, ndi Mfumu ya Mtendere.
For to us a child has been born, to us a son has been given; and the rule will be on his shoulder; and his name will be called Wonderful Counselor, Mighty God, Everlasting Father, Prince of Peace.
7 Ulamuliro ndi mtendere wake zidzakhala zopanda malire. Iye adzalamulira ufumu wake ali pa mpando waufumu wa Davide, ndipo adzawukhazikitsa ndi kuwuchirikiza mwa chiweruzo cholungama ndi pochita zachilungamo kuyambira nthawi imeneyo mpaka muyaya. Ndi mtima wake wonse, Yehova Wamphamvuzonse watsimikiza kuchita zimenezi.
Of the increase of his government and of peace there will be no end, as he rules on the throne of David, and over his kingdom, to establish it and sustain it with justice and with righteousness from this time onward and for evermore. The zeal of Yahweh of hosts will do this.
8 Ambuye atumiza mawu otsutsa Yakobo; ndipo mawuwo agwera pa Israeli.
The Lord sent a word against Jacob, and it fell on Israel.
9 Anthu onse okhala mu Efereimu ndi okhala mu Samariya, adzadziwa zimenezi. Iwo amayankhula modzikuza kuti,
All the people will know, even Ephraim and the inhabitants of Samaria, who say in pride and with an arrogant heart,
10 “Ngakhale njerwa zagumuka, koma ife tidzamanga ndi miyala yosema. Mitanda ya mkuyu yagwetsedwa, koma ife tidzayika mitanda ya mkungudza mʼmalo mwake.”
“The bricks have fallen, but we will rebuild with chiseled stone; the sycamores have been cut down, but we will put cedars in their place.”
11 Koma Yehova wadzutsa adani kuti alimbane nawo ndipo wawafulumiza adani awo kuti amenyane nawo.
Therefore Yahweh will raise up against him Rezin, his adversary, and will stir up his enemies,
12 Asiriya ochokera kummawa ndi Afilisti ochokera kumadzulo ndipo ayasama pakamwa kuti adye a Israeli. Komabe, mkwiyo wake sunawachokere, mkono wake uli chitambasulire.
the Arameans on the east, and the Philistines on the west. They will devour Israel with open mouth. In all these things, his anger does not subside; instead, his hand is still stretched out.
13 Koma anthu sanabwerere kwa amene anawakantha uja, ngakhale kufunafuna Yehova Wamphamvuzonse.
Yet the people will not turn to him who struck them, nor will they seek Yahweh of hosts.
14 Choncho Yehova adzadula mutu wa Israeli pamodzi ndi mchira womwe, nthambi ya kanjedza ndi bango lomwe tsiku limodzi;
Therefore Yahweh will cut off from Israel head and tail, palm branch and reed, in one day.
15 mutuwo ndiye akuluakulu ndi olemekezeka, mchira ndiye aneneri ophunzitsa zabodza.
The leader and the noble man are the head; and the prophet that teaches lies is the tail.
16 Amene amatsogolera anthuwa ndiwo amawasocheretsa, ndipo otsogoleredwa amatayika.
Those who lead this people lead them astray, and those who are led by them are swallowed up.
17 Nʼchifukwa chake Ambuye adzakondwera nawo achinyamata, ngakhale kuwachitira chifundo ana amasiye ndi akazi amasiye, pakuti aliyense ndi wosapembedza Mulungu ndiponso ndi wochimwa ndipo aliyense amayankhula zopusa. Komabe, mkwiyo wake sunawachokere, mkono wake uli chitambasulire.
Therefore the Lord will not rejoice over their young men nor will he have compassion on their fatherless and widows, since every one is godless and an evildoer, and every mouth speaks foolish things. In all these things, his anger does not subside; instead, his hand is still stretched out.
18 Ndithu kuyipa kwa anthuwo kumayaka ngati moto; moto wake umanyeketsa mkandankhuku ndi minga, umayatsa nkhalango yowirira, ndipo utsi wake umachita kuti toloo ngati mtambo.
Wickedness burns like a fire; it devours the briers and thorns; it even burns the thickets of the forest, which rise in a column of smoke.
19 Dziko lidzatenthedwa ndi ukali wa Yehova Wamphamvuzonse, dziko lidzatenthedwa ndipo anthu adzakhala ngati nkhuni zosonkhera moto; palibe munthu amene adzachitire chifundo mʼbale wake.
Through the fury of Yahweh of hosts the land is scorched, and the people are like fuel for the fire. No man spares his brother.
20 Kudzanja lamanja adzapeza chakudya nʼkudya, koma adzakhalabe ndi njala; kudzanja lamanzere adzapeza chakudya nʼkudya, koma sadzakhuta. Aliyense azidzadya ana ake omwe.
They will grab food on the right hand but still be hungry; they will eat food on the left hand but will not be satisfied. Each will even eat the flesh of his own arm.
21 Manase adzadya Efereimu ndipo Efereimu adzadya Manase; onsewa pamodzi adzadya Yuda. Komabe pa zonsezi, mkwiyo wake sunawachokere, mkono wake uli chitambasulire.
Manasseh will devour Ephraim, and Ephraim, Manasseh; and they together will attack Judah. In all these things, his anger does not subside; instead, his hand is still stretched out.