< Yesaya 8 >
1 Yehova anati kwa ine, “Tenga cholembapo chachikulu ndipo ulembepo malemba odziwika bwino: Kusakaza-Kwamsanga Kufunkha-Kofulumira.
Og Herren sa til mig: Ta dig en stor tavle og skriv på den med almindelig skrift: Snart bytte, rov i hast!
2 Ndipo ndidzayitana wansembe Uriya ndi Zekariya mwana wa Yeberekiya kuti akhale mboni zanga zodalirika.”
Og jeg vil ta mig sikre vidner, presten Uria og Sakarias, Jeberekjas sønn.
3 Ndipo ine ndinapita kwa mneneri wamkazi, ndipo anakhala woyembekezera nabala mwana wamwamuna. Ndipo Yehova anati kwa ine, “Umutche dzina lakuti, ‘Kusakaza-Kwamsanga Kufunkha-Kofulumira.’
Og jeg gikk inn til profetinnen, og hun blev fruktsommelig og fødte en sønn; og Herren sa til mig: Kall ham Maher-Sjalal Hasj-Bas!
4 Mwanayo asanayambe kudziwa kuyitana kuti, ‘Ababa’ kapena ‘Amama’ chuma cha Damasiko ndi zofunkha za Samariya zidzatengedwa ndi mfumu ya ku Asiriya.”
For før gutten skjønner å rope far og mor, skal de bære rikdommene i Damaskus og byttet fra Samaria frem for Assurs konge.
5 Yehova anayankhulanso ndi Ine;
Og Herren blev fremdeles ved å tale til mig og sa:
6 “Popeza anthu a dziko ili akana madzi anga oyenda mwachifatse a ku Siloamu, ndipo akukondwerera Rezini ndi mwana wa Remaliya,
Fordi dette folk forakter Siloahs vann, de som rinner så stilt, og gleder sig med Resin og Remaljas sønn,
7 nʼchifukwa chake Ambuye ali pafupi kubweretsa madzi amkokomo a mtsinje wa Yufurate kudzalimbana nawo; mfumu ya ku Asiriya ndi gulu lake lonse lankhondo. Madziwo adzasefukira mʼngalande zake zonse ndi mʼmagombe ake onse.
se, derfor fører Herren over dem elvens vann, de mektige og store - Assurs konge og all hans herlighet - og den stiger over alle sine løp og går over alle sine bredder,
8 Ndipo adzalowa mwamphamvu mʼdziko la Yuda, adzasefukira, adzapitirira mpaka kumuyesa mʼkhosi. Mapiko ake otambasuka adzaphimba dziko lako lonse, iwe Imanueli!”
og den trenger inn i Juda, skyller over og velter frem og når folk like til halsen, og dens utspente vinger fyller ditt land, så vidt som det er, Immanuel!
9 Chitani phokoso lankhondo, inu mitundu ya anthu, ndipo munjenjemere! Tamverani, inu mayiko onse akutali. Konzekerani nkhondo ndipo munjenjemere! Konzekerani nkhondo ndipo munjenjemere!
Larm, I folkeslag! I skal dog bli forferdet. Og hør, alle I jordens land langt borte! Rust eder! I skal dog forferdes.
10 Konzani kachitidwe kanu kankhondo, koma simudzaphula kanthu, kambiranani zochita, koma zidzalephereka, pakuti Mulungu ali nafe.
Legg op råd! De skal dog gjøres til intet. Tal et ord! Det skal dog ikke skje. For med oss er Gud.
11 Yehova anandiyankhula ine mwamphamvu, ndipo anandichenjeza kuti ndisamayende mʼnjira za anthuwa. Iye anati:
For så sa Herren til mig da hans hånd grep mig med makt, og han advarte mig mot å vandre på dette folks vei:
12 “Usamanene kuti ndi chiwembu, chilichonse chimene anthuwa amati ndi chiwembu usamaope zimene anthuwa amaziopa, ndipo usamachite nazo mantha.
I skal ikke kalle alt det sammensvergelse som dette folk kaller sammensvergelse, og hvad det frykter, skal I ikke frykte og ikke reddes for.
13 Yehova Wamphamvuzonse ndiye amene uyenera kumuona kuti ndi woyera, ndiye amene uyenera kumuopa, ndiye amene uyenera kuchita naye mantha,
Herren, hærskarenes Gud, ham skal I holde hellig, og han skal være eders frykt, han skal være eders redsel.
14 ndipo ndiye amene adzakhala malo opatulika; koma kwa anthu a ku Yuda ndi kwa anthu a ku Israeli adzakhala mwala wopunthwitsa, mwala umene umapunthwitsa anthu, thanthwe limene limagwetsa anthu. Ndipo kwa anthu a mu Yerusalemu adzakhala ngati msampha ndi khwekhwe.
Og han skal bli til en helligdom og til en snublesten og en anstøtsklippe for begge Israels hus, til en snare og et rep for Jerusalems innbyggere.
15 Anthu ambiri adzapunthwapo adzagwa ndi kuthyokathyoka, adzakodwa ndi kugwidwa.”
Og mange blandt dem skal snuble, og de skal falle og skamslå sig, og de skal snares og fanges.
16 Manga umboniwu ndipo umate malamulowa pamaso pa ophunzira anga.
Bind vidnesbyrdet inn, forsegl ordet i mine disipler!
17 Ndidzayembekezera Yehova, amene akubisira nkhope yake nyumba ya Yakobo. Ine ndidzakhulupirira Iyeyo.
Jeg vil bie efter Herren, som nu skjuler sitt åsyn for Jakobs hus; jeg vil vente på ham.
18 Onani, ine ndili pano pamodzi ndi ana amene Yehova wandipatsa, ndife zizindikiro ndi zodabwitsa kwa Aisraeli zochokera kwa Yehova Wamphamvuzonse, amene amakhala pa Phiri la Ziyoni.
Se, jeg og de barn Herren har gitt mig, er til tegn og forbilleder i Israel fra Herren, hærskarenes Gud, som bor på Sions berg.
19 Anthu akakuwuza kuti kafunsire kwa oyankhula ndi mizimu, amene amayankhula monongʼona ndi mongʼungʼudza, kodi anthu sayenera kukafunsira kwa Mulungu wawo? Chifukwa chiyani amafunsira kwa anthu akufa mʼmalo mwa kwa anthu amoyo,
Og når de sier til eder: Søk til dødningemanerne og sannsigerne, som hvisker og mumler, da skal I svare: Skal ikke et folk søke til sin Gud? Skal en søke til de døde for de levende?
20 kuti akalandireko mawu enieni ndi malangizo? Ngati anthuwo sayankhula monga mwa mawu awa, mwa iwo mulibe kuwala.
Til ordet og til vidnesbyrdet! - Dersom de ikke sier så, det folk som ingen morgenrøde har,
21 Anthu adzayendayenda mʼdziko movutika kwambiri ali ndi njala; pamene afowokeratu ndi njala, iwo adzakwiya kwambiri ndipo adzayangʼana kumwamba ndi kutemberera mfumu yawo ndi Mulungu wawo.
da skal de dra gjennem landet hårdt plaget og hungrige, og når de hungrer, så blir de harme og forbanner sin konge og sin Gud. De skal vende sine øine mot det høie,
22 Ndipo akadzayangʼana pa dziko lapansi adzangoona mavuto okhaokha ndi mdima woopsa ndi wodetsa nkhawa, ndipo adzaponyedwa mu mdima wandiweyani.
og de skal se ned mot jorden, men se, det er trengsel og mørke, angstfullt mørke; de er støtt ut i natten.