< Yesaya 8 >
1 Yehova anati kwa ine, “Tenga cholembapo chachikulu ndipo ulembepo malemba odziwika bwino: Kusakaza-Kwamsanga Kufunkha-Kofulumira.
Ja Herra sanoi minulle: "Ota iso taulu ja kirjoita siihen selkeällä kirjoituksella: Maher-Saalal Haas-Bas.
2 Ndipo ndidzayitana wansembe Uriya ndi Zekariya mwana wa Yeberekiya kuti akhale mboni zanga zodalirika.”
Ja minä otan itselleni luotettavat todistajat, pappi Uurian ja Sakarjan, Jeberekjan pojan."
3 Ndipo ine ndinapita kwa mneneri wamkazi, ndipo anakhala woyembekezera nabala mwana wamwamuna. Ndipo Yehova anati kwa ine, “Umutche dzina lakuti, ‘Kusakaza-Kwamsanga Kufunkha-Kofulumira.’
Sitten minä lähestyin profeetta-vaimoani, ja hän tuli raskaaksi ja synnytti pojan. Niin Herra sanoi minulle: "Pane hänelle nimeksi Maher-Saalal Haas-Bas.
4 Mwanayo asanayambe kudziwa kuyitana kuti, ‘Ababa’ kapena ‘Amama’ chuma cha Damasiko ndi zofunkha za Samariya zidzatengedwa ndi mfumu ya ku Asiriya.”
Sillä ennenkuin poika oppii sanomaan: 'isä' ja 'äiti', viedään Damaskoon tavarat ja Samarian saalis Assurin kuninkaan eteen."
5 Yehova anayankhulanso ndi Ine;
Ja Herra puhui jälleen minulle ja sanoi:
6 “Popeza anthu a dziko ili akana madzi anga oyenda mwachifatse a ku Siloamu, ndipo akukondwerera Rezini ndi mwana wa Remaliya,
"Koska tämä kansa halveksii Siiloan hiljaa virtaavia vesiä ja iloitsee Resinin ja Remaljan pojan kanssa,
7 nʼchifukwa chake Ambuye ali pafupi kubweretsa madzi amkokomo a mtsinje wa Yufurate kudzalimbana nawo; mfumu ya ku Asiriya ndi gulu lake lonse lankhondo. Madziwo adzasefukira mʼngalande zake zonse ndi mʼmagombe ake onse.
niin katso, sentähden Herra antaa tulla heidän ylitsensä virran vedet, valtavat ja suuret: Assurin kuninkaan ja kaiken hänen kunniansa; se nousee kaikkien uomiensa yli ja menee kaikkien äyräittensä yli,
8 Ndipo adzalowa mwamphamvu mʼdziko la Yuda, adzasefukira, adzapitirira mpaka kumuyesa mʼkhosi. Mapiko ake otambasuka adzaphimba dziko lako lonse, iwe Imanueli!”
ja se tunkeutuu Juudaan, paisuu ja tulvii ja ulottuu kaulaan saakka. Ja levittäen siipensä se täyttää yliyltään sinun maasi, Immanuel."
9 Chitani phokoso lankhondo, inu mitundu ya anthu, ndipo munjenjemere! Tamverani, inu mayiko onse akutali. Konzekerani nkhondo ndipo munjenjemere! Konzekerani nkhondo ndipo munjenjemere!
Riehukaa, kansat, kuitenkin kukistutte; kuulkaa, kaikki kaukaiset maat: sonnustautukaa, kuitenkin kukistutte; sonnustautukaa, kuitenkin kukistutte.
10 Konzani kachitidwe kanu kankhondo, koma simudzaphula kanthu, kambiranani zochita, koma zidzalephereka, pakuti Mulungu ali nafe.
Pitäkää neuvoa: se raukeaa; sopikaa sopimus: ei se pysy. Sillä Jumala on meidän kanssamme.
11 Yehova anandiyankhula ine mwamphamvu, ndipo anandichenjeza kuti ndisamayende mʼnjira za anthuwa. Iye anati:
Sillä näin sanoi minulle Herra, kun hänen kätensä valtasi minut ja hän varoitti minua vaeltamasta tämän kansan tietä:
12 “Usamanene kuti ndi chiwembu, chilichonse chimene anthuwa amati ndi chiwembu usamaope zimene anthuwa amaziopa, ndipo usamachite nazo mantha.
"Älkää sanoko salaliitoksi kaikkea, mitä tämä kansa salaliitoksi sanoo; älkää peljätkö, mitä se pelkää, älkääkä kauhistuko.
13 Yehova Wamphamvuzonse ndiye amene uyenera kumuona kuti ndi woyera, ndiye amene uyenera kumuopa, ndiye amene uyenera kuchita naye mantha,
Herra Sebaot pitäkää pyhänä, häntä te peljätkää ja kauhistukaa.
14 ndipo ndiye amene adzakhala malo opatulika; koma kwa anthu a ku Yuda ndi kwa anthu a ku Israeli adzakhala mwala wopunthwitsa, mwala umene umapunthwitsa anthu, thanthwe limene limagwetsa anthu. Ndipo kwa anthu a mu Yerusalemu adzakhala ngati msampha ndi khwekhwe.
Ja hän on oleva pyhäkkö, hän loukkauskivi ja kompastuksen kallio molemmille Israelin huonekunnille, paula ja ansa Jerusalemin asukkaille.
15 Anthu ambiri adzapunthwapo adzagwa ndi kuthyokathyoka, adzakodwa ndi kugwidwa.”
Monet heistä kompastuvat ja kaatuvat ja ruhjoutuvat, monet kiedotaan ja vangitaan.
16 Manga umboniwu ndipo umate malamulowa pamaso pa ophunzira anga.
Sido todistus talteen, lukitse laki sinetillä minun opetuslapsiini."
17 Ndidzayembekezera Yehova, amene akubisira nkhope yake nyumba ya Yakobo. Ine ndidzakhulupirira Iyeyo.
Niin minä odotan Herraa, joka kätkee kasvonsa Jaakobin heimolta, ja panen toivoni häneen.
18 Onani, ine ndili pano pamodzi ndi ana amene Yehova wandipatsa, ndife zizindikiro ndi zodabwitsa kwa Aisraeli zochokera kwa Yehova Wamphamvuzonse, amene amakhala pa Phiri la Ziyoni.
Katso, minä ja lapset, jotka Herra on minulle antanut, me olemme Herran Sebaotin merkkeinä ja ihmeinä Israelissa, hänen, joka asuu Siionin vuorella.
19 Anthu akakuwuza kuti kafunsire kwa oyankhula ndi mizimu, amene amayankhula monongʼona ndi mongʼungʼudza, kodi anthu sayenera kukafunsira kwa Mulungu wawo? Chifukwa chiyani amafunsira kwa anthu akufa mʼmalo mwa kwa anthu amoyo,
Ja kun he sanovat teille: "Kysykää vainaja-ja tietäjähengiltä, jotka supisevat ja mumisevat", niin eikö kansa kysyisi Jumalaltansa? Kuolleiltako elävien puolesta?
20 kuti akalandireko mawu enieni ndi malangizo? Ngati anthuwo sayankhula monga mwa mawu awa, mwa iwo mulibe kuwala.
"Pysykää laissa ja todistuksessa!" Elleivät he näin sano, ei heillä aamunkoittoa ole.
21 Anthu adzayendayenda mʼdziko movutika kwambiri ali ndi njala; pamene afowokeratu ndi njala, iwo adzakwiya kwambiri ndipo adzayangʼana kumwamba ndi kutemberera mfumu yawo ndi Mulungu wawo.
Ja siellä he kuljeskelevat vaivattuina ja nälkäisinä, ja nälissään he vimmastuvat ja kiroavat kuninkaansa ja Jumalansa. He luovat silmänsä korkeuteen,
22 Ndipo akadzayangʼana pa dziko lapansi adzangoona mavuto okhaokha ndi mdima woopsa ndi wodetsa nkhawa, ndipo adzaponyedwa mu mdima wandiweyani.
he katsahtavat maan puoleen, mutta katso: ainoastaan ahdistusta ja pimeyttä; he ovat syöstyt tuskan synkeyteen ja pimeyteen.