< Yesaya 8 >

1 Yehova anati kwa ine, “Tenga cholembapo chachikulu ndipo ulembepo malemba odziwika bwino: Kusakaza-Kwamsanga Kufunkha-Kofulumira.
Ja Herra sanoi minulle: ota suuri kirja etees, ja kirjoita siihen ihmisen kirjoituksella: ryöstä nopiasti, riennä saaliille.
2 Ndipo ndidzayitana wansembe Uriya ndi Zekariya mwana wa Yeberekiya kuti akhale mboni zanga zodalirika.”
Ja minä otin tyköni uskolliset todistajat: papin Urijan, ja Sakarian Jeberekjan pojan,
3 Ndipo ine ndinapita kwa mneneri wamkazi, ndipo anakhala woyembekezera nabala mwana wamwamuna. Ndipo Yehova anati kwa ine, “Umutche dzina lakuti, ‘Kusakaza-Kwamsanga Kufunkha-Kofulumira.’
Ja menin prophetissan tykö, se tuli raskaaksi ja synnytti pojan; ja Herra sanoi minulle: nimitä se: ryöstä pian, ja riennä jakoon.
4 Mwanayo asanayambe kudziwa kuyitana kuti, ‘Ababa’ kapena ‘Amama’ chuma cha Damasiko ndi zofunkha za Samariya zidzatengedwa ndi mfumu ya ku Asiriya.”
Sillä ennenkuin poikainen taitaa sanoa: isäni, äitini, viedään Damaskun tavarat ja Samarian saalis pois Assyrian kuninkaan edellä.
5 Yehova anayankhulanso ndi Ine;
Ja Herra puhui vielä minun kanssani ja sanoi:
6 “Popeza anthu a dziko ili akana madzi anga oyenda mwachifatse a ku Siloamu, ndipo akukondwerera Rezini ndi mwana wa Remaliya,
Että tämä kansa hylkää Siloan veden, joka hiljaksensa juoksee, ja turvaa Retsiniin ja Remalian poikaan;
7 nʼchifukwa chake Ambuye ali pafupi kubweretsa madzi amkokomo a mtsinje wa Yufurate kudzalimbana nawo; mfumu ya ku Asiriya ndi gulu lake lonse lankhondo. Madziwo adzasefukira mʼngalande zake zonse ndi mʼmagombe ake onse.
Katso, niin Herra antaa tulla hänen päällensä paljon ja väkevän virtaveden, Assyrian kuninkaan, ja kaiken hänen kunniansa, että se nousee kaikkein parrastensa yli, ja käypi kaikkein rantainsa yli;
8 Ndipo adzalowa mwamphamvu mʼdziko la Yuda, adzasefukira, adzapitirira mpaka kumuyesa mʼkhosi. Mapiko ake otambasuka adzaphimba dziko lako lonse, iwe Imanueli!”
Ja käypi Juudan lävitse, tulvaa ja nousee, siihenasti kuin se ulottuu kaulaan asti; ja levittää siipensä, niin että ne täyttävät sinun maas, o Immanuel, niin leviä kuin se on.
9 Chitani phokoso lankhondo, inu mitundu ya anthu, ndipo munjenjemere! Tamverani, inu mayiko onse akutali. Konzekerani nkhondo ndipo munjenjemere! Konzekerani nkhondo ndipo munjenjemere!
Kokoontukaat kansat, ja paetkaat kuitenkin; kuulkaat kaikki, jotka olette kaukaisissa maakunnissa: hankkikaat sotaan ja paetkaat kuitenkin, hankkikaat ja paetkaat kuitenkin.
10 Konzani kachitidwe kanu kankhondo, koma simudzaphula kanthu, kambiranani zochita, koma zidzalephereka, pakuti Mulungu ali nafe.
Päättäkäät neuvo, ja ei se miksikään tule; puhukaat keskenänne, ja ei sekään seiso, sillä tässä on Immanuel.
11 Yehova anandiyankhula ine mwamphamvu, ndipo anandichenjeza kuti ndisamayende mʼnjira za anthuwa. Iye anati:
Sillä näin sanoi Herra minulle, kuin hän käteeeni rupesi, ja neuvoi minua, etten minä vaeltaisi tämän kansan tiellä, ja sanoi:
12 “Usamanene kuti ndi chiwembu, chilichonse chimene anthuwa amati ndi chiwembu usamaope zimene anthuwa amaziopa, ndipo usamachite nazo mantha.
Älkäät sanoko liitoksi, mitä tämä kansa liitoksi sanoo: älkäät te peljätkö, niinkuin he tekevät, älkäät myös vapisko.
13 Yehova Wamphamvuzonse ndiye amene uyenera kumuona kuti ndi woyera, ndiye amene uyenera kumuopa, ndiye amene uyenera kuchita naye mantha,
Vaan pyhittäkäät Herra Zebaot; ja hän olkoon teidän pelkonne, hän olkoon teidän vapistuksenne;
14 ndipo ndiye amene adzakhala malo opatulika; koma kwa anthu a ku Yuda ndi kwa anthu a ku Israeli adzakhala mwala wopunthwitsa, mwala umene umapunthwitsa anthu, thanthwe limene limagwetsa anthu. Ndipo kwa anthu a mu Yerusalemu adzakhala ngati msampha ndi khwekhwe.
Niin hän on pyhitys; mutta loukkauskivi ja kompastuskallio kahdelle Israelin huoneelle, paulaksi ja ansaksi Jerusalemin asuville,
15 Anthu ambiri adzapunthwapo adzagwa ndi kuthyokathyoka, adzakodwa ndi kugwidwa.”
Niin että moni heistä loukkaa itsensä, ja lankeevat, särjetään, kiedotaan ja vangitaan.
16 Manga umboniwu ndipo umate malamulowa pamaso pa ophunzira anga.
Sido todistus kiinni, lukitse laki minun opetuslapsissani.
17 Ndidzayembekezera Yehova, amene akubisira nkhope yake nyumba ya Yakobo. Ine ndidzakhulupirira Iyeyo.
Sillä minä toivon Herraan, joka kasvonsa Jakobin huoneelta kätkenyt on; mutta minä odotan häntä.
18 Onani, ine ndili pano pamodzi ndi ana amene Yehova wandipatsa, ndife zizindikiro ndi zodabwitsa kwa Aisraeli zochokera kwa Yehova Wamphamvuzonse, amene amakhala pa Phiri la Ziyoni.
Katso, tässä minä olen, ja ne lapset, jotka Herra minulle antanut on merkiksi ja ihmeeksi Israelissa Herralta Zebaotilta, joka Zionin vuorella asuu.
19 Anthu akakuwuza kuti kafunsire kwa oyankhula ndi mizimu, amene amayankhula monongʼona ndi mongʼungʼudza, kodi anthu sayenera kukafunsira kwa Mulungu wawo? Chifukwa chiyani amafunsira kwa anthu akufa mʼmalo mwa kwa anthu amoyo,
Kuin siin he teille sanovat: kysykäät noidilta ja tietäjiltä, jotka kuiskuttelevat ja tutkivat, (niin sanokaat: ) eikö kansan pidä Jumalaltansa kysymän? (eikö ole parempi kysyä) eläviltä kuin kuolleilta?
20 kuti akalandireko mawu enieni ndi malangizo? Ngati anthuwo sayankhula monga mwa mawu awa, mwa iwo mulibe kuwala.
(Ja pikemmin) lain jälkeen ja todistuksen? Ellei he tämän sanan jälkeen sano, niin ei heidän pidä aamuruskoa saaman.
21 Anthu adzayendayenda mʼdziko movutika kwambiri ali ndi njala; pamene afowokeratu ndi njala, iwo adzakwiya kwambiri ndipo adzayangʼana kumwamba ndi kutemberera mfumu yawo ndi Mulungu wawo.
Vaan heidän pitää kävelemän maakunnassa vaivattuina ja nälkäisinä; mutta kuin he nälkää kärsivät, niin he vihastuvat ja kiroilevat kuningastansa ja Jumalaansa, ja katsovat ylöspäin,
22 Ndipo akadzayangʼana pa dziko lapansi adzangoona mavuto okhaokha ndi mdima woopsa ndi wodetsa nkhawa, ndipo adzaponyedwa mu mdima wandiweyani.
Ja katselevat maata, vaan ei muuta mitään löydä, kuin murheet ja pimeydet; sillä he ovat pimitetyt ahdistuksessa, ja eksyvät pimeydessä.

< Yesaya 8 >