< Yesaya 8 >
1 Yehova anati kwa ine, “Tenga cholembapo chachikulu ndipo ulembepo malemba odziwika bwino: Kusakaza-Kwamsanga Kufunkha-Kofulumira.
And the LORD said unto me: 'Take thee a great tablet, and write upon it in common script: The spoil speedeth, the prey hasteth;
2 Ndipo ndidzayitana wansembe Uriya ndi Zekariya mwana wa Yeberekiya kuti akhale mboni zanga zodalirika.”
and I will take unto Me faithful witnesses to record, Uriah the priest, and Zechariah the son of Jeberechiah.'
3 Ndipo ine ndinapita kwa mneneri wamkazi, ndipo anakhala woyembekezera nabala mwana wamwamuna. Ndipo Yehova anati kwa ine, “Umutche dzina lakuti, ‘Kusakaza-Kwamsanga Kufunkha-Kofulumira.’
And I went unto the prophetess; and she conceived, and bore a son. Then said the LORD unto me: 'Call his name Maher-shalal-hashbaz.
4 Mwanayo asanayambe kudziwa kuyitana kuti, ‘Ababa’ kapena ‘Amama’ chuma cha Damasiko ndi zofunkha za Samariya zidzatengedwa ndi mfumu ya ku Asiriya.”
For before the child shall have knowledge to cry: My father, and: My mother, the riches of Damascus and the spoil of Samaria shall be carried away before the king of Assyria.'
5 Yehova anayankhulanso ndi Ine;
And the LORD spoke unto me yet again, saying:
6 “Popeza anthu a dziko ili akana madzi anga oyenda mwachifatse a ku Siloamu, ndipo akukondwerera Rezini ndi mwana wa Remaliya,
Forasmuch as this people hath refused the waters of Shiloah that go softly, and rejoiceth with Rezin and Remaliah's son;
7 nʼchifukwa chake Ambuye ali pafupi kubweretsa madzi amkokomo a mtsinje wa Yufurate kudzalimbana nawo; mfumu ya ku Asiriya ndi gulu lake lonse lankhondo. Madziwo adzasefukira mʼngalande zake zonse ndi mʼmagombe ake onse.
Now therefore, behold, the Lord bringeth up upon them the waters of the River, mighty and many, even the king of Assyria and all his glory; and he shall come up over all his channels, and go over all his banks;
8 Ndipo adzalowa mwamphamvu mʼdziko la Yuda, adzasefukira, adzapitirira mpaka kumuyesa mʼkhosi. Mapiko ake otambasuka adzaphimba dziko lako lonse, iwe Imanueli!”
And he shall sweep through Judah overflowing as he passeth through he shall reach even to the neck; and the stretching out of his wings shall fill the breadth of thy land, O Immanuel.
9 Chitani phokoso lankhondo, inu mitundu ya anthu, ndipo munjenjemere! Tamverani, inu mayiko onse akutali. Konzekerani nkhondo ndipo munjenjemere! Konzekerani nkhondo ndipo munjenjemere!
Make an uproar, O ye peoples, and ye shall be broken in pieces; and give ear, all ye of far countries; gird yourselves, and ye shall be broken in pieces; gird yourselves, and ye shall be broken in pieces.
10 Konzani kachitidwe kanu kankhondo, koma simudzaphula kanthu, kambiranani zochita, koma zidzalephereka, pakuti Mulungu ali nafe.
Take counsel together, and it shall be brought to nought; speak the word, and it shall not stand; for God is with us.
11 Yehova anandiyankhula ine mwamphamvu, ndipo anandichenjeza kuti ndisamayende mʼnjira za anthuwa. Iye anati:
For the LORD spoke thus to me with a strong hand, admonishing me that I should not walk in the way of this people, saying:
12 “Usamanene kuti ndi chiwembu, chilichonse chimene anthuwa amati ndi chiwembu usamaope zimene anthuwa amaziopa, ndipo usamachite nazo mantha.
'Say ye not: A conspiracy, concerning all whereof this people do say: A conspiracy; neither fear ye their fear, nor account it dreadful.
13 Yehova Wamphamvuzonse ndiye amene uyenera kumuona kuti ndi woyera, ndiye amene uyenera kumuopa, ndiye amene uyenera kuchita naye mantha,
The LORD of hosts, Him shall ye sanctify; and let Him be your fear, and let Him be your dread.
14 ndipo ndiye amene adzakhala malo opatulika; koma kwa anthu a ku Yuda ndi kwa anthu a ku Israeli adzakhala mwala wopunthwitsa, mwala umene umapunthwitsa anthu, thanthwe limene limagwetsa anthu. Ndipo kwa anthu a mu Yerusalemu adzakhala ngati msampha ndi khwekhwe.
And He shall be for a sanctuary; but for a stone of stumbling and for a rock of offence to both the houses of Israel, for a gin and for a snare to the inhabitants of Jerusalem.
15 Anthu ambiri adzapunthwapo adzagwa ndi kuthyokathyoka, adzakodwa ndi kugwidwa.”
And many among them shall stumble, and fall, and be broken, and be snared, and be taken.'
16 Manga umboniwu ndipo umate malamulowa pamaso pa ophunzira anga.
'Bind up the testimony, seal the instruction among My disciples.'
17 Ndidzayembekezera Yehova, amene akubisira nkhope yake nyumba ya Yakobo. Ine ndidzakhulupirira Iyeyo.
And I will wait for the LORD, that hideth His face from the house of Jacob, and I will look for Him.
18 Onani, ine ndili pano pamodzi ndi ana amene Yehova wandipatsa, ndife zizindikiro ndi zodabwitsa kwa Aisraeli zochokera kwa Yehova Wamphamvuzonse, amene amakhala pa Phiri la Ziyoni.
Behold, I and the children whom the LORD hath given me shall be for signs and for wonders in Israel from the LORD of hosts, who dwelleth in mount Zion.
19 Anthu akakuwuza kuti kafunsire kwa oyankhula ndi mizimu, amene amayankhula monongʼona ndi mongʼungʼudza, kodi anthu sayenera kukafunsira kwa Mulungu wawo? Chifukwa chiyani amafunsira kwa anthu akufa mʼmalo mwa kwa anthu amoyo,
And when they shall say unto you: 'Seek unto the ghosts and the familiar spirits, that chirp and that mutter; should not a people seek unto their God? on behalf of the living unto the dead
20 kuti akalandireko mawu enieni ndi malangizo? Ngati anthuwo sayankhula monga mwa mawu awa, mwa iwo mulibe kuwala.
for instruction and for testimony?' — Surely they will speak according to this word, wherein there is no light. —
21 Anthu adzayendayenda mʼdziko movutika kwambiri ali ndi njala; pamene afowokeratu ndi njala, iwo adzakwiya kwambiri ndipo adzayangʼana kumwamba ndi kutemberera mfumu yawo ndi Mulungu wawo.
And they shall pass this way that are sore bestead and hungry; and it shall come to pass that, when they shall be hungry, they shall fret themselves, and curse by their king and by their God, and, whether they turn their faces upward,
22 Ndipo akadzayangʼana pa dziko lapansi adzangoona mavuto okhaokha ndi mdima woopsa ndi wodetsa nkhawa, ndipo adzaponyedwa mu mdima wandiweyani.
or look unto the earth, behold distress and darkness, the gloom of anguish, and outspread thick darkness.