< Yesaya 8 >

1 Yehova anati kwa ine, “Tenga cholembapo chachikulu ndipo ulembepo malemba odziwika bwino: Kusakaza-Kwamsanga Kufunkha-Kofulumira.
And Jehovah said to me, Take thee a great tablet, and write upon it with the pen of a man, For Maher-shalal-hash-baz.
2 Ndipo ndidzayitana wansembe Uriya ndi Zekariya mwana wa Yeberekiya kuti akhale mboni zanga zodalirika.”
And I will take to me faithful witnesses to record, Uriah the priest, and Zechariah the son of Jeberechiah.
3 Ndipo ine ndinapita kwa mneneri wamkazi, ndipo anakhala woyembekezera nabala mwana wamwamuna. Ndipo Yehova anati kwa ine, “Umutche dzina lakuti, ‘Kusakaza-Kwamsanga Kufunkha-Kofulumira.’
And I went to the prophetess, and she conceived, and bore a son. Then Jehovah said to me, Call his name Maher-shalal-hash-baz.
4 Mwanayo asanayambe kudziwa kuyitana kuti, ‘Ababa’ kapena ‘Amama’ chuma cha Damasiko ndi zofunkha za Samariya zidzatengedwa ndi mfumu ya ku Asiriya.”
For before the child shall have knowledge to cry, My father, and, My mother, the riches of Damascus and the spoil of Samaria shall be carried away before the king of Assyria.
5 Yehova anayankhulanso ndi Ine;
And Jehovah spoke to me yet again, saying,
6 “Popeza anthu a dziko ili akana madzi anga oyenda mwachifatse a ku Siloamu, ndipo akukondwerera Rezini ndi mwana wa Remaliya,
Inasmuch as this people have refused the waters of Shiloah that go softly, and rejoice in Rezin and Remaliah's son,
7 nʼchifukwa chake Ambuye ali pafupi kubweretsa madzi amkokomo a mtsinje wa Yufurate kudzalimbana nawo; mfumu ya ku Asiriya ndi gulu lake lonse lankhondo. Madziwo adzasefukira mʼngalande zake zonse ndi mʼmagombe ake onse.
now therefore, behold, the Lord brings up upon them the waters of the River, strong and many, even the king of Assyria and all his glory. And it shall come up over all its channels, and go over all its banks,
8 Ndipo adzalowa mwamphamvu mʼdziko la Yuda, adzasefukira, adzapitirira mpaka kumuyesa mʼkhosi. Mapiko ake otambasuka adzaphimba dziko lako lonse, iwe Imanueli!”
and it shall sweep onward into Judah. It shall overflow and pass through; it shall reach even to the neck. And the stretching out of its wings shall fill the breadth of thy land, O Immanuel.
9 Chitani phokoso lankhondo, inu mitundu ya anthu, ndipo munjenjemere! Tamverani, inu mayiko onse akutali. Konzekerani nkhondo ndipo munjenjemere! Konzekerani nkhondo ndipo munjenjemere!
Make an uproar, O ye peoples, and be broken in pieces. And give ear, all ye of far countries. Gird yourselves, and be broken in pieces. Gird yourselves, and be broken in pieces.
10 Konzani kachitidwe kanu kankhondo, koma simudzaphula kanthu, kambiranani zochita, koma zidzalephereka, pakuti Mulungu ali nafe.
Take counsel together, and it shall be brought to nothing. Speak the word, and it shall not stand, for God is with us.
11 Yehova anandiyankhula ine mwamphamvu, ndipo anandichenjeza kuti ndisamayende mʼnjira za anthuwa. Iye anati:
For Jehovah spoke thus to me with a strong hand, and instructed me not to walk in the way of this people, saying,
12 “Usamanene kuti ndi chiwembu, chilichonse chimene anthuwa amati ndi chiwembu usamaope zimene anthuwa amaziopa, ndipo usamachite nazo mantha.
Say ye not, A conspiracy, concerning all of which this people shall say, A conspiracy, nor fear ye their fear, nor be in dread of it.
13 Yehova Wamphamvuzonse ndiye amene uyenera kumuona kuti ndi woyera, ndiye amene uyenera kumuopa, ndiye amene uyenera kuchita naye mantha,
Jehovah of hosts, him ye shall sanctify, and let him be your fear, and let him be your dread.
14 ndipo ndiye amene adzakhala malo opatulika; koma kwa anthu a ku Yuda ndi kwa anthu a ku Israeli adzakhala mwala wopunthwitsa, mwala umene umapunthwitsa anthu, thanthwe limene limagwetsa anthu. Ndipo kwa anthu a mu Yerusalemu adzakhala ngati msampha ndi khwekhwe.
And he shall be for a sanctuary, but for a stone of stumbling and for a rock of offense to both the houses of Israel, for a net and for a snare to the inhabitants of Jerusalem.
15 Anthu ambiri adzapunthwapo adzagwa ndi kuthyokathyoka, adzakodwa ndi kugwidwa.”
And many shall stumble on it, and fall, and be broken, and be snared, and be taken.
16 Manga umboniwu ndipo umate malamulowa pamaso pa ophunzira anga.
Bind thou up the testimony. Seal the law among my disciples.
17 Ndidzayembekezera Yehova, amene akubisira nkhope yake nyumba ya Yakobo. Ine ndidzakhulupirira Iyeyo.
And I will wait for Jehovah, who hides his face from the house of Jacob, and I will be a man who has trusted in him.
18 Onani, ine ndili pano pamodzi ndi ana amene Yehova wandipatsa, ndife zizindikiro ndi zodabwitsa kwa Aisraeli zochokera kwa Yehova Wamphamvuzonse, amene amakhala pa Phiri la Ziyoni.
Behold, I and the children whom Jehovah has given me are for signs and for wonders in Israel from Jehovah of hosts, who dwells in mount Zion.
19 Anthu akakuwuza kuti kafunsire kwa oyankhula ndi mizimu, amene amayankhula monongʼona ndi mongʼungʼudza, kodi anthu sayenera kukafunsira kwa Mulungu wawo? Chifukwa chiyani amafunsira kwa anthu akufa mʼmalo mwa kwa anthu amoyo,
And when they shall say to you, Seek for those who have familiar spirits and for the wizards, who chirp and who mutter, should not a people seek for their God? On behalf of the living seek to the dead?
20 kuti akalandireko mawu enieni ndi malangizo? Ngati anthuwo sayankhula monga mwa mawu awa, mwa iwo mulibe kuwala.
Seek to the law and to the testimony! If they speak not according to this word, surely there is no morning for them.
21 Anthu adzayendayenda mʼdziko movutika kwambiri ali ndi njala; pamene afowokeratu ndi njala, iwo adzakwiya kwambiri ndipo adzayangʼana kumwamba ndi kutemberera mfumu yawo ndi Mulungu wawo.
And they shall pass through it, greatly distressed and hungry. And it shall come to pass that, when they shall be hungry, they shall fret themselves, and curse by their king and by their God, and turn their faces upward.
22 Ndipo akadzayangʼana pa dziko lapansi adzangoona mavuto okhaokha ndi mdima woopsa ndi wodetsa nkhawa, ndipo adzaponyedwa mu mdima wandiweyani.
And they shall look to the earth, and, behold, distress and darkness, the gloom of anguish, and into thick darkness to be driven away.

< Yesaya 8 >