< Yesaya 7 >

1 Pamene Ahazi mwana wa Yotamu, mdzukulu wa Uziya anali mfumu ya Yuda, Rezini mfumu ya Siriya ndi Peka mwana wa Remaliya, mfumu ya Israeli anabwera kudzathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu, koma sanathe kuwugonjetsa.
Det begaf sig uti Ahas, Jothams sons, Ussia sons, Juda Konungs, tid, drog Rezin, Konungen i Syrien, och Pekah, Remalia son, Israels Konung, upp till Jerusalem, till att örliga deremot; men de kunde intet öfvervinna det.
2 Tsono nyumba ya Davide inawuzidwa kuti, “Dziko la Siriya lagwirizana ndi Efereimu.” Choncho mfumu Ahazi ndi anthu ake ananjenjemera, monga momwe mitengo ya mʼnkhalango imagwedezekera ndi mphepo.
Då vardt Davids huse sagdt: De Syror förlåta sig uppå Ephraim. Då bäfvade honom hjertat, och hans folks hjerta, lika som trän i skogenom bäfva för vädret.
3 Pamenepo Yehova anawuza Yesaya kuti, “Tuluka, iwe ndi mwana wako Seariyasubu, mupite mukakumane ndi Ahazi kumapeto kwa ngalande yamadzi yochokera ku Dziwe Lakumtunda, pa msewu wopita ku Munda wa mmisiri wochapa nsalu.
Men Herren talade till Esaia: Gack ut emot Ahas, du och din son SearJasub, till ändan af vatturännone vid öfra dammen, på den vägen vid färgarens åker;
4 Ukamuwuze kuti, ‘Chenjera, khala phee ndipo usaope. Usataye mtima chifukwa cha zitsa ziwiri zomwe zikufuka, chifukwa cha ukali woopsa wa Rezini ndi Siriya, ndiponso wa Peka mwana wa Remaliya.
Och säg till honom: Vara dig, och blir stilla, frukta dig intet, och ditt hjerta vare oförskräckt för dessa två rykande släckebrandar; nämliga för Rezins och de Syrers, och Remalia sons vrede;
5 Mfumu ya Siriya, Efereimu ndi mwana wa Remaliya apangana kuti akuchitire choyipa. Akunena kuti,
Att de Syror hafva gjort ett ondt rådslag emot dig, samt med Ephraim och Remalia son, och säga:
6 ‘Tiyeni tikalimbane ndi Yuda. Tiyeni tiliwononge ndi kuligawa; tiligawane pakati pathu, ndipo tilonge ufumu mwana wa Tabeeli kumeneko.’
Vi vilje upp till Juda, och förskräcka honom, och skifta oss emellan, och göra Tabeels son till Konung derinne.
7 Komabe zimene akunena Ambuye Yehova ndi izi: “‘Zimenezo sizidzatheka, sizidzachitika konse,
Ty så säger Herren, Herren: Det skall intet så bestå eller så ske;
8 pakuti Siriya amadalira Damasiko, ndipo Damasiko amadalira mfumu Rezini basi. Zisanathe zaka 65 Efereimu adzawonongedwa kotheratu, sadzakhalanso mtundu wa anthu.
Utan lika som Damascus är hufvudet i Syrien, så skall Rezin vara hufvudet i Damasco. Och efter fem och sextio år skall det vara ute med Ephraim, att de icke mer skola vara något folk.
9 Dziko la Efereimu limadalira Samariya ndipo Samariya amadalira mwana wa Remaliya basi. Mukapanda kulimbika pa chikhulupiriro chanu, ndithu simudzalimba konse.’”
Och lika som Samarien är hufvudet i Ephraim, så skall Remalia son vara hufvudet i Samarien. Tron I icke, så felar det med eder.
10 Yehova anayankhulanso ndi Ahazi,
Och Herren talade åter till Ahas, och sade:
11 “Pempha chizindikiro kwa Yehova Mulungu wako, chikhale chozama ngati manda kapena chachitali ngati mlengalenga.” (Sheol h7585)
Äska dig ett tecken af Herranom, dinom Gud, antingen nedre i helvetet, eller ofvantill i höjdene. (Sheol h7585)
12 Koma Ahazi anati, “Ine sindipempha; sindikufuna kuyesa Yehova.”
Men Ahas sade: Jag äskar intet, att jag icke skall försöka Herran.
13 Apo Yesaya anati, “Imva tsopano, iwe nyumba ya Davide! Kodi sikokwanira kutopetsa anthu? Kodi mudzayeseranso kutopetsa Mulungu wanga?
Då sade han: Nu väl, så hörer I af Davids hus; är det eder litet, att I gören menniskom emot, utan att I ock gören min Gud emot?
14 Nʼchifukwa chake Ambuye mwini adzakupatsani chizindikiro: Onani, namwali adzakhala woyembekezera ndipo adzabala mwana wamwamuna, ndipo mwanayo adzamutcha Imanueli.
Derföre skall Herren sjelf gifva eder ett tecken; si, en Jungfru är hafvandes, och skall föda en son, den skall hon kalla ImmanuEl.
15 Azidzadya chambiko ndi uchi, mpaka atadziwa kukana choyipa ndi kusankha chabwino.
Smör och hannog skall han äta, att han skall veta förkasta det onda, och utvälja det goda.
16 Koma nthawi yokana choyipa ndi kusankha chabwino kwa mwanayo isanafike, mayiko a mafumu awiri amene amakuopsaniwo adzakhala atasanduka bwinja.
Ty förr än pilten lärer förkasta det ondt är, och utvälja det godt är, skall det land, der du grufvar dig före, öfvergifvet varda af sina två Konungar.
17 Yehova adzabweretsa pa inu, pa anthu anu ndiponso pa nyumba ya bambo wanu masiku a mavuto woti sanakhalepo kuyambira tsiku limene Efereimu anapatukana ndi Yuda. Yehova adzabweretsa mfumu ya ku Asiriya.”
Men öfver dig, öfver ditt folk och öfver dins faders hus, skall Herren, genom Konungen af Assyrien, komma låta dagar, de icke komne äro, sedan Ephraim ifrå Juda skiljdes.
18 Tsiku limenelo Yehova adzalizira likhweru ntchentche zochokera ku mitsinje yakutali ku Igupto, ndiponso njuchi zochokera ku dziko la Asiriya.
Ty på den tiden skall Herren hvissla till flugorna vid ändan på Egypti älfver, och till bin i Assurs land;
19 Onsewo adzafika ndi kudzakhazikika mu zigwa zozama, mʼmingʼalu ya matanthwe ndi mʼzitsamba zonse zaminga ndiponso ponse pamene pali malo omwetsera ziweto.
Att de skola komma, och allesammans lägga sig vid bäcker och stenklyftor, och all hål trä, och uti all hål.
20 Tsiku limenelo Ambuye adzalemba ganyu ometa ochokera kutsidya kwa Mtsinje, ndiye mfumu ya ku Asiriya, kudzameta tsitsi lanu la ku mutu ndi la mʼmiyendo ndi ndevu zomwe.
På den samma tiden skall Herren raka hufvudet, och håret af fötterna, och taga bort skägget genom en lejd rakoknif; nämliga genom dem som på hinsidon älfvena äro, det är, genom Konungen af Assyrien.
21 Tsiku limenelo adzangosunga ngʼombe yayikazi yayingʼono ndi mbuzi ziwiri.
På den samma tiden skall en man föda en hop kor, och två hjordar;
22 Ndipo chifukwa cha kuchuluka kwa mkaka umene ziwetozi zidzapereka, munthuyo azidzadya chambiko. Aliyense amene adzatsalire mʼdzikomo azidzadya chambiko ndi uchi.
Och skall hafva så mycket till att molka, att han smör äta skall; ty den som i landens igenlefves, han skall äta smör och hannog.
23 Tsiku limenelo, paliponse pamene panali mitengo ya mpesa 1,000 ndipo mtengo wake ndi wokwana masekeli asiliva 1,000, padzamera mkandankhuku ndi minga.
Ty det skall ske på den tiden, att der nu tusende vinträd stå, tusende silfpenningar värd, der skall vara törne och tistel;
24 Anthu adzapita kumeneko kukachita uzimba ali ndi uta ndi mivi, popeza kuti mʼdziko monsemo mudzakhala mkandankhuku ndi minga.
Så att man måste gå dit med pil och båga; ty uti hela landet skall törne och tistel vara;
25 Ndipo mʼmapiri monse mʼmene kale munkalimidwa ndi khasu, simudzapitamo kuopa mkandankhuku ndi minga; malowo adzasanduka odyetserako ngʼombe ndi nkhosa.
Så att man icke komma kan till alla de berg, som man plägar uppgrafva med hacko, för tistlars och törnes styggelses skull; utan man skall låta oxar gå deruppå och får deröfver trampa.

< Yesaya 7 >