< Yesaya 7 >
1 Pamene Ahazi mwana wa Yotamu, mdzukulu wa Uziya anali mfumu ya Yuda, Rezini mfumu ya Siriya ndi Peka mwana wa Remaliya, mfumu ya Israeli anabwera kudzathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu, koma sanathe kuwugonjetsa.
Nos dias de Acaz, filho de Jotão, filho de Uzias, rei de Judá, Rezim, rei da Síria, e Peca, filho de Remalias, rei de Israel, subiram a Jerusalém para fazer guerra contra ela, mas não puderam prevalecer contra ela.
2 Tsono nyumba ya Davide inawuzidwa kuti, “Dziko la Siriya lagwirizana ndi Efereimu.” Choncho mfumu Ahazi ndi anthu ake ananjenjemera, monga momwe mitengo ya mʼnkhalango imagwedezekera ndi mphepo.
Foi dito à casa de Davi: “A Síria é aliada de Efraim”. Seu coração tremia, e o coração de seu povo, enquanto as árvores da floresta tremiam com o vento.
3 Pamenepo Yehova anawuza Yesaya kuti, “Tuluka, iwe ndi mwana wako Seariyasubu, mupite mukakumane ndi Ahazi kumapeto kwa ngalande yamadzi yochokera ku Dziwe Lakumtunda, pa msewu wopita ku Munda wa mmisiri wochapa nsalu.
Então Yahweh disse a Isaías: “Saia agora para encontrar Ahaz, você, e Shearjashub seu filho, no final do conduíte da piscina superior, na rodovia do campo do fuller.
4 Ukamuwuze kuti, ‘Chenjera, khala phee ndipo usaope. Usataye mtima chifukwa cha zitsa ziwiri zomwe zikufuka, chifukwa cha ukali woopsa wa Rezini ndi Siriya, ndiponso wa Peka mwana wa Remaliya.
Diga-lhe: 'Tenha cuidado e mantenha a calma. Não tenha medo, nem deixe seu coração desmaiar por causa dessas duas caudas de tochas fumegantes, pela raiva feroz de Rezin e da Síria, e do filho de Remaliah.
5 Mfumu ya Siriya, Efereimu ndi mwana wa Remaliya apangana kuti akuchitire choyipa. Akunena kuti,
Porque a Síria, Efraim, e o filho de Remalias, conspiraram contra você, dizendo:
6 ‘Tiyeni tikalimbane ndi Yuda. Tiyeni tiliwononge ndi kuligawa; tiligawane pakati pathu, ndipo tilonge ufumu mwana wa Tabeeli kumeneko.’
“Vamos contra Judá, e rasguemo-lo, e dividamo-lo entre nós, e constituamos um rei dentro dele, até mesmo o filho de Tabeel”.
7 Komabe zimene akunena Ambuye Yehova ndi izi: “‘Zimenezo sizidzatheka, sizidzachitika konse,
Isto é o que o Senhor Javé diz: “Não subsistirá, nem acontecerá”.
8 pakuti Siriya amadalira Damasiko, ndipo Damasiko amadalira mfumu Rezini basi. Zisanathe zaka 65 Efereimu adzawonongedwa kotheratu, sadzakhalanso mtundu wa anthu.
Pois o chefe da Síria é Damasco, e o chefe de Damasco é Rezin. Dentro de sessenta e cinco anos Efraim será quebrado em pedaços, para que não seja um povo.
9 Dziko la Efereimu limadalira Samariya ndipo Samariya amadalira mwana wa Remaliya basi. Mukapanda kulimbika pa chikhulupiriro chanu, ndithu simudzalimba konse.’”
A cabeça de Efraim é Samaria, e a cabeça de Samaria é o filho de Remaliah. Se você não acreditar, certamente não será estabelecido””.
10 Yehova anayankhulanso ndi Ahazi,
Yahweh falou novamente com Ahaz, dizendo,
11 “Pempha chizindikiro kwa Yehova Mulungu wako, chikhale chozama ngati manda kapena chachitali ngati mlengalenga.” (Sheol )
“Peça um sinal de Yahweh seu Deus; peça-o ou na profundidade, ou na altura acima”. (Sheol )
12 Koma Ahazi anati, “Ine sindipempha; sindikufuna kuyesa Yehova.”
Mas Ahaz disse: “Eu não vou perguntar. Eu não vou tentar Yahweh”.
13 Apo Yesaya anati, “Imva tsopano, iwe nyumba ya Davide! Kodi sikokwanira kutopetsa anthu? Kodi mudzayeseranso kutopetsa Mulungu wanga?
Ele disse: “Escute agora, casa de David. Não é suficiente que você experimente a paciência dos homens, que você também experimente a paciência do meu Deus?
14 Nʼchifukwa chake Ambuye mwini adzakupatsani chizindikiro: Onani, namwali adzakhala woyembekezera ndipo adzabala mwana wamwamuna, ndipo mwanayo adzamutcha Imanueli.
Portanto, o próprio Senhor lhe dará um sinal. Eis que a virgem conceberá, e dará à luz um filho, e chamará seu nome Emanuel.
15 Azidzadya chambiko ndi uchi, mpaka atadziwa kukana choyipa ndi kusankha chabwino.
Ele comerá manteiga e mel quando souber recusar o mal e escolher o bem.
16 Koma nthawi yokana choyipa ndi kusankha chabwino kwa mwanayo isanafike, mayiko a mafumu awiri amene amakuopsaniwo adzakhala atasanduka bwinja.
Pois antes que a criança saiba recusar o mal e escolher o bem, a terra cujos dois reis você abomina será abandonada.
17 Yehova adzabweretsa pa inu, pa anthu anu ndiponso pa nyumba ya bambo wanu masiku a mavuto woti sanakhalepo kuyambira tsiku limene Efereimu anapatukana ndi Yuda. Yehova adzabweretsa mfumu ya ku Asiriya.”
Yahweh trará sobre você, sobre seu povo e sobre a casa de seu pai dias que não vieram, desde o dia em que Efraim partiu de Judá, até mesmo o rei da Assíria.
18 Tsiku limenelo Yehova adzalizira likhweru ntchentche zochokera ku mitsinje yakutali ku Igupto, ndiponso njuchi zochokera ku dziko la Asiriya.
Acontecerá nesse dia que Javé assobiará pela mosca que está na parte mais alta dos rios do Egito, e pela abelha que está na terra da Assíria.
19 Onsewo adzafika ndi kudzakhazikika mu zigwa zozama, mʼmingʼalu ya matanthwe ndi mʼzitsamba zonse zaminga ndiponso ponse pamene pali malo omwetsera ziweto.
Elas virão, e todas descansarão nos vales desolados, nas fendas das rochas, em todas as sebes de espinhos, e em todos os pastos.
20 Tsiku limenelo Ambuye adzalemba ganyu ometa ochokera kutsidya kwa Mtsinje, ndiye mfumu ya ku Asiriya, kudzameta tsitsi lanu la ku mutu ndi la mʼmiyendo ndi ndevu zomwe.
Naquele dia o Senhor fará a barba com uma lâmina de barbear que é alugada nas partes além do rio, mesmo com o rei da Assíria, a cabeça e os cabelos dos pés; e também consumirá a barba.
21 Tsiku limenelo adzangosunga ngʼombe yayikazi yayingʼono ndi mbuzi ziwiri.
Acontecerá naquele dia que um homem manterá viva uma vaca jovem, e duas ovelhas.
22 Ndipo chifukwa cha kuchuluka kwa mkaka umene ziwetozi zidzapereka, munthuyo azidzadya chambiko. Aliyense amene adzatsalire mʼdzikomo azidzadya chambiko ndi uchi.
Acontecerá que, por causa da abundância de leite que eles darão, ele comerá manteiga, pois todos comerão a manteiga e o mel que restar dentro da terra.
23 Tsiku limenelo, paliponse pamene panali mitengo ya mpesa 1,000 ndipo mtengo wake ndi wokwana masekeli asiliva 1,000, padzamera mkandankhuku ndi minga.
Acontecerá naquele dia que cada lugar onde houvesse mil videiras no valor de mil siclos de prata, será para sarças e espinhos.
24 Anthu adzapita kumeneko kukachita uzimba ali ndi uta ndi mivi, popeza kuti mʼdziko monsemo mudzakhala mkandankhuku ndi minga.
As pessoas irão lá com flechas e com arco, porque toda a terra será para sarças e espinhos.
25 Ndipo mʼmapiri monse mʼmene kale munkalimidwa ndi khasu, simudzapitamo kuopa mkandankhuku ndi minga; malowo adzasanduka odyetserako ngʼombe ndi nkhosa.
Todas as colinas que foram cultivadas com a enxada, não virão para lá por medo de sarças e espinhos; mas será para o envio de bois, e para que as ovelhas pisem”.