< Yesaya 7 >

1 Pamene Ahazi mwana wa Yotamu, mdzukulu wa Uziya anali mfumu ya Yuda, Rezini mfumu ya Siriya ndi Peka mwana wa Remaliya, mfumu ya Israeli anabwera kudzathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu, koma sanathe kuwugonjetsa.
Kwathi u-Ahazi indodana kaJothamu, indodana ka-Uziya, eyinkosi yakoJuda, uRezini inkosi yase-Aramu loPhekha indodana kaRemaliya inkosi yako-Israyeli basuka bayahlasela iJerusalema, kodwa kabalinqobanga.
2 Tsono nyumba ya Davide inawuzidwa kuti, “Dziko la Siriya lagwirizana ndi Efereimu.” Choncho mfumu Ahazi ndi anthu ake ananjenjemera, monga momwe mitengo ya mʼnkhalango imagwedezekera ndi mphepo.
Indlu kaDavida yatshelwa kwathiwa, “I-Aramu isimanyene lo-Efrayimi,” inhliziyo ka-Ahazi lezabantu bakhe zanyikinyeka njengezihlahla zegusu zinyikinywa ngumoya.
3 Pamenepo Yehova anawuza Yesaya kuti, “Tuluka, iwe ndi mwana wako Seariyasubu, mupite mukakumane ndi Ahazi kumapeto kwa ngalande yamadzi yochokera ku Dziwe Lakumtunda, pa msewu wopita ku Munda wa mmisiri wochapa nsalu.
UThixo wasesithi ku-Isaya, “Hamba wena lendodana yakho uSheyari-Jashubi ukuba lihlangabeze u-Ahazi ekucineni komgelo wamanzi oweChibi Elingaphezulu, emgwaqweni oya Ensimini Yomgezisi.
4 Ukamuwuze kuti, ‘Chenjera, khala phee ndipo usaope. Usataye mtima chifukwa cha zitsa ziwiri zomwe zikufuka, chifukwa cha ukali woopsa wa Rezini ndi Siriya, ndiponso wa Peka mwana wa Remaliya.
Lithi kuye, ‘Nanzelela, hlala ngokuthula, njalo ungesabi. Inhliziyo yakho kayingadeli ngenxa yolaka olwesabekayo lukaRezini lo-Aramu lolwendodana kaRemaliya.’”
5 Mfumu ya Siriya, Efereimu ndi mwana wa Remaliya apangana kuti akuchitire choyipa. Akunena kuti,
U-Aramu lo-Efrayimi lendodana kaRemaliya sebecebe ukukutshabalalisa besithi,
6 ‘Tiyeni tikalimbane ndi Yuda. Tiyeni tiliwononge ndi kuligawa; tiligawane pakati pathu, ndipo tilonge ufumu mwana wa Tabeeli kumeneko.’
“Kasihlaseleni ilizwe lakoJuda; kasilidabuleni phakathi silabelane, senze indodana kaThabheli ibe yinkosi yalo.”
7 Komabe zimene akunena Ambuye Yehova ndi izi: “‘Zimenezo sizidzatheka, sizidzachitika konse,
Kodwa-ke lokhu yikho okutshiwo nguThixo Wobukhosi ukuthi: “‘Akuyikuphumelela, akuyikwenzakala,
8 pakuti Siriya amadalira Damasiko, ndipo Damasiko amadalira mfumu Rezini basi. Zisanathe zaka 65 Efereimu adzawonongedwa kotheratu, sadzakhalanso mtundu wa anthu.
ngoba inhloko ye-Aramu yiDamaseko, inhloko yeDamaseko nguRezini kuphela. Phakathi kweminyaka engamatshumi ayisithupha lanhlanu u-Efrayimi uzakuba esetshabalele engaseyiso sizwe.
9 Dziko la Efereimu limadalira Samariya ndipo Samariya amadalira mwana wa Remaliya basi. Mukapanda kulimbika pa chikhulupiriro chanu, ndithu simudzalimba konse.’”
Inhloko ka-Efrayimi yiSamariya, inhloko yeSamariya yindodana kaRemaliya kuphela. Nxa lingami liqine okholweni lwenu alisoze livele lime.’”
10 Yehova anayankhulanso ndi Ahazi,
UThixo wakhuluma njalo ku-Ahazi wathi,
11 “Pempha chizindikiro kwa Yehova Mulungu wako, chikhale chozama ngati manda kapena chachitali ngati mlengalenga.” (Sheol h7585)
“Cela isibonakaliso kuThixo uNkulunkulu wakho, ingabe ekujuleni kwezulu loba phezulu engqongweni.” (Sheol h7585)
12 Koma Ahazi anati, “Ine sindipempha; sindikufuna kuyesa Yehova.”
Kodwa u-Ahazi wathi, “Angiyikucela. Angiyikulinga uThixo.”
13 Apo Yesaya anati, “Imva tsopano, iwe nyumba ya Davide! Kodi sikokwanira kutopetsa anthu? Kodi mudzayeseranso kutopetsa Mulungu wanga?
U-Isaya wasesithi, “Khathesi-ke zwana wena lendlu kaDavida. Akwenelanga na ukulinga ukubekezela kwabantu? Uzalinga lokubekezela kukaNkulunkulu wami njalo na?
14 Nʼchifukwa chake Ambuye mwini adzakupatsani chizindikiro: Onani, namwali adzakhala woyembekezera ndipo adzabala mwana wamwamuna, ndipo mwanayo adzamutcha Imanueli.
Ngakho-ke iNkosi ngokwayo izanika isibonakaliso: Intombi egcweleyo izakhulelwa izale indodana bayibize ngokuthi ngu-Emanuweli.
15 Azidzadya chambiko ndi uchi, mpaka atadziwa kukana choyipa ndi kusankha chabwino.
Uzakudla amasi loluju lapho eselolwazi olwaneleyo ukuba ale okubi akhethe okulungileyo.
16 Koma nthawi yokana choyipa ndi kusankha chabwino kwa mwanayo isanafike, mayiko a mafumu awiri amene amakuopsaniwo adzakhala atasanduka bwinja.
Kodwa-ke umfana engakazi okwaneleyo ukuba ale okubi akhethe okulungileyo, ilizwe lamakhosi amabili owesabayo lizachithwa.
17 Yehova adzabweretsa pa inu, pa anthu anu ndiponso pa nyumba ya bambo wanu masiku a mavuto woti sanakhalepo kuyambira tsiku limene Efereimu anapatukana ndi Yuda. Yehova adzabweretsa mfumu ya ku Asiriya.”
UThixo uzakwehlisela phezu kwakho laphezu kwabantu bakho, laphezu kwendlu kayihlo, isikhathi esingafani lesinye kusukela u-Efrayimi ebhazuka kuJuda, uzaletha inkosi yase-Asiriya.”
18 Tsiku limenelo Yehova adzalizira likhweru ntchentche zochokera ku mitsinje yakutali ku Igupto, ndiponso njuchi zochokera ku dziko la Asiriya.
Ngalelolanga uThixo uzatshaya ikhwelo ebiza impukane ezisekudabukeni kwezifula zaseGibhithe lezinyosi eziselizweni lase-Asiriya.
19 Onsewo adzafika ndi kudzakhazikika mu zigwa zozama, mʼmingʼalu ya matanthwe ndi mʼzitsamba zonse zaminga ndiponso ponse pamene pali malo omwetsera ziweto.
Zizakuza zonke zihlale ezingoxweni ezingamawa, ezimbalwini zamadwala, ezihlahleni zonke zameva kuwo wonke amagodi amanzi.
20 Tsiku limenelo Ambuye adzalemba ganyu ometa ochokera kutsidya kwa Mtsinje, ndiye mfumu ya ku Asiriya, kudzameta tsitsi lanu la ku mutu ndi la mʼmiyendo ndi ndevu zomwe.
Ngalolosuku iNkosi izasebenzisa impuco ebolekwe enkosini yase-Asiriya ngaphetsheya koMfula iYufrathe ukuphuca ikhanda lakho loboya obusembaleni yakho, lokugunda indevu zakho lazo.
21 Tsiku limenelo adzangosunga ngʼombe yayikazi yayingʼono ndi mbuzi ziwiri.
Ngalolosuku umuntu uzafuya ithokazi elilodwa lembuzi ezimbili.
22 Ndipo chifukwa cha kuchuluka kwa mkaka umene ziwetozi zidzapereka, munthuyo azidzadya chambiko. Aliyense amene adzatsalire mʼdzikomo azidzadya chambiko ndi uchi.
Ngenxa yobunengi bochago oluzavela kuzo, uzakuba lamasi azawadla. Bonke abazasala elizweni bazakudla amasi loluju.
23 Tsiku limenelo, paliponse pamene panali mitengo ya mpesa 1,000 ndipo mtengo wake ndi wokwana masekeli asiliva 1,000, padzamera mkandankhuku ndi minga.
Ngalolosuku, ezindaweni zonke lapho okwakulamavini ayinkulungwane alingana amashekeli esiliva ayinkulungwane, kuzakuba lokhula lameva kuphela.
24 Anthu adzapita kumeneko kukachita uzimba ali ndi uta ndi mivi, popeza kuti mʼdziko monsemo mudzakhala mkandankhuku ndi minga.
Abantu bazakuya khona belamadandili lemitshoko ngoba ilizwe lizakuba seligcwele ukhula lameva.
25 Ndipo mʼmapiri monse mʼmene kale munkalimidwa ndi khasu, simudzapitamo kuopa mkandankhuku ndi minga; malowo adzasanduka odyetserako ngʼombe ndi nkhosa.
Emaqaqeni wonke ake alinywa ngekhuba kawusayikuya khona ngenxa yokwesaba ukhula lameva, azakuba yindawo yokwelusela inkomo lamadlelo ezimvu.

< Yesaya 7 >