< Yesaya 7 >

1 Pamene Ahazi mwana wa Yotamu, mdzukulu wa Uziya anali mfumu ya Yuda, Rezini mfumu ya Siriya ndi Peka mwana wa Remaliya, mfumu ya Israeli anabwera kudzathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu, koma sanathe kuwugonjetsa.
I KE kau ia Ahaza, ke keiki a Iotama, ke keiki a Uzia, ke alii o ka Iuda, hele mai o Rezina, ke alii o Suria, a me Peka, ke keiki a Remalia, ke alii o ka Iseraela, e ku e ia Ierusalema, kaua mai, aole nae i hiki ia lakou ke lanakila maluna o ia wahi.
2 Tsono nyumba ya Davide inawuzidwa kuti, “Dziko la Siriya lagwirizana ndi Efereimu.” Choncho mfumu Ahazi ndi anthu ake ananjenjemera, monga momwe mitengo ya mʼnkhalango imagwedezekera ndi mphepo.
A haiia mai la i ko ka hale o Davida, i ka i ana mai, Ke hoomoana nei ko Suria maloko o ko Eperaima. Alaila, haalulu ka naau o ke alii, a me ka naau o kona poo kanaka, o like me ka haalulu ana o na laau o ka ululaau imua o ka makani.
3 Pamenepo Yehova anawuza Yesaya kuti, “Tuluka, iwe ndi mwana wako Seariyasubu, mupite mukakumane ndi Ahazi kumapeto kwa ngalande yamadzi yochokera ku Dziwe Lakumtunda, pa msewu wopita ku Munda wa mmisiri wochapa nsalu.
I mai la o Iehova ia Isaia, O hele, ano, e halawai me Ahaza, o oe, a me Seariasuba, kau keiki, ma ka welau o ka auwai o ka waipuna luna, ma ke ala e hiki aku ai ke kula holoi lole;
4 Ukamuwuze kuti, ‘Chenjera, khala phee ndipo usaope. Usataye mtima chifukwa cha zitsa ziwiri zomwe zikufuka, chifukwa cha ukali woopsa wa Rezini ndi Siriya, ndiponso wa Peka mwana wa Remaliya.
A e i aku oe ia ia, E ao oe, e noho malie; Mai makau hoi, mai maule kou naau, No na welowelo alua o keia mau momoku ahi, O ka huhu o Rezina, a me ko Suria, a me ko keiki a Remalia.
5 Mfumu ya Siriya, Efereimu ndi mwana wa Remaliya apangana kuti akuchitire choyipa. Akunena kuti,
No ka imi hala o ko Suria ia oe, A me Eperaima, a me ke keiki a Remalia, i ka i ana ae,
6 ‘Tiyeni tikalimbane ndi Yuda. Tiyeni tiliwononge ndi kuligawa; tiligawane pakati pathu, ndipo tilonge ufumu mwana wa Tabeeli kumeneko.’
E pii ku e kakou i ka Iuda, e hoopilikia aku hoi, A e mahele ia wahi no kakou, A e hoonoho i ke keiki a Tabeala, i alii maloko ona.
7 Komabe zimene akunena Ambuye Yehova ndi izi: “‘Zimenezo sizidzatheka, sizidzachitika konse,
Ke i mai nei ka Haku, o Iehova penei, Aole e ku keia, aole ia e hanaia.
8 pakuti Siriya amadalira Damasiko, ndipo Damasiko amadalira mfumu Rezini basi. Zisanathe zaka 65 Efereimu adzawonongedwa kotheratu, sadzakhalanso mtundu wa anthu.
O ke poo o Suria, o Damaseko ia, A o ke poo o Damaseko, o Rezina no; He kanaonokumamalima makahiki i koe, Alaila, kahuli o Eperaima, a lilo i aupuni ole.
9 Dziko la Efereimu limadalira Samariya ndipo Samariya amadalira mwana wa Remaliya basi. Mukapanda kulimbika pa chikhulupiriro chanu, ndithu simudzalimba konse.’”
O Samaria no ke poo o Eperaima, A o ke poo hoi o Samaria, oia ke keiki a Remalia. I ole oukou e manaoio i keia, aole oukou e malu.
10 Yehova anayankhulanso ndi Ahazi,
Olelo hou mai o Iehova ia Ahaza, i mai la,
11 “Pempha chizindikiro kwa Yehova Mulungu wako, chikhale chozama ngati manda kapena chachitali ngati mlengalenga.” (Sheol h7585)
E nonoi oe i hoailona nou, mai Iehova, mai kou Akua mai; E nonoi ma ka hohonu, a ma kahi kiekie paha. (Sheol h7585)
12 Koma Ahazi anati, “Ine sindipempha; sindikufuna kuyesa Yehova.”
I aku la o Ahaza, Aole au e nonoi, Aole hoi au e aa aku ia Iehova.
13 Apo Yesaya anati, “Imva tsopano, iwe nyumba ya Davide! Kodi sikokwanira kutopetsa anthu? Kodi mudzayeseranso kutopetsa Mulungu wanga?
Alaila, i mai la ia, E hoolohe oukou, e ka ohana a Davida, He mea uuku anei ia oukou ke hoopaupauaho i kanaka? E hoopaupauaho pu anei oukou i ko'u Akua?
14 Nʼchifukwa chake Ambuye mwini adzakupatsani chizindikiro: Onani, namwali adzakhala woyembekezera ndipo adzabala mwana wamwamuna, ndipo mwanayo adzamutcha Imanueli.
Nolaila, na ka Haku ponoi no e haawi mai ia oukou i hoailona; Aia hoi! e hapai ana no kekahi wahine puupaa, A e hanau mai hoi ia i keiki, A e kapa aku no oia i kona inoa, o IMANUELA.
15 Azidzadya chambiko ndi uchi, mpaka atadziwa kukana choyipa ndi kusankha chabwino.
O ka waiu paa a me ka mele kana e ai ai, A ike oia i ka hoole i ka hewa, a e koho hoi i ka pono.
16 Koma nthawi yokana choyipa ndi kusankha chabwino kwa mwanayo isanafike, mayiko a mafumu awiri amene amakuopsaniwo adzakhala atasanduka bwinja.
No ka mea, mamua o ka ike ana o ke keiki e hoole i ka hewa, A e koho hoi i ka pono, E neoneo e no ka aina o ua mau alii la elua au e makau nei.
17 Yehova adzabweretsa pa inu, pa anthu anu ndiponso pa nyumba ya bambo wanu masiku a mavuto woti sanakhalepo kuyambira tsiku limene Efereimu anapatukana ndi Yuda. Yehova adzabweretsa mfumu ya ku Asiriya.”
Na Iehova no e hoopuka mai maluna ou, A maluna hoi o kou poe kanaka, A maluna o ka hale o kou makuakane, I na la i hiki ole mai ai mamua, Mai ka wa mai o ko Eperaima haalele ana i ka Iuda; I ke alii no Asuria.
18 Tsiku limenelo Yehova adzalizira likhweru ntchentche zochokera ku mitsinje yakutali ku Igupto, ndiponso njuchi zochokera ku dziko la Asiriya.
A hiki aku i kela la, Na Iehova no e pio aku i ka nalo, E noho ana ma na welau o na muliwai o Aigupita, A i ka nalo-hope-eha, ma ka aina o Asuria;
19 Onsewo adzafika ndi kudzakhazikika mu zigwa zozama, mʼmingʼalu ya matanthwe ndi mʼzitsamba zonse zaminga ndiponso ponse pamene pali malo omwetsera ziweto.
A e hele mai hoi lakou, a e kau mai lakou a pau, Ma na kahawai olohelohe, a ma na lua o na pohaku, A ma ka nahele ooi a pau, A ma na kula holoholona a pau.
20 Tsiku limenelo Ambuye adzalemba ganyu ometa ochokera kutsidya kwa Mtsinje, ndiye mfumu ya ku Asiriya, kudzameta tsitsi lanu la ku mutu ndi la mʼmiyendo ndi ndevu zomwe.
Ia la la, na ka Haku no e kahi, me ka pahi-kahi i hoolimalimaia, ma kela aoao o ka muliwai, Me ke alii hoi o Asuria, I ke poo, a me ke oho o na kapuwai; A e kahiia no hoi ka umiumi.
21 Tsiku limenelo adzangosunga ngʼombe yayikazi yayingʼono ndi mbuzi ziwiri.
A hiki aku i kela la, E hanai no ke kanaka i ka bipi ohi, a me na hipa elua;
22 Ndipo chifukwa cha kuchuluka kwa mkaka umene ziwetozi zidzapereka, munthuyo azidzadya chambiko. Aliyense amene adzatsalire mʼdzikomo azidzadya chambiko ndi uchi.
A no ka nui loa mai o ka waiu, E ai no ia i ka waiupaa; E ai io no i ka waiupaa a me ka meli, O ka poe a pau i koe ma ka aina.
23 Tsiku limenelo, paliponse pamene panali mitengo ya mpesa 1,000 ndipo mtengo wake ndi wokwana masekeli asiliva 1,000, padzamera mkandankhuku ndi minga.
A hiki aku i kela la, O kahi a pau i ulu ai na kumuwaina, he tausani, I kuaiia no na hapalua he tausani, E paapu ia wahi i ka nahele ooi, a me ka laau kalakala.
24 Anthu adzapita kumeneko kukachita uzimba ali ndi uta ndi mivi, popeza kuti mʼdziko monsemo mudzakhala mkandankhuku ndi minga.
Me na pua a me na kakaka lakou e hele ai ilaila, No ka mea, e nahelehele ana no ka aina a pau, I ka laau kalakala a me ka nahele ooi.
25 Ndipo mʼmapiri monse mʼmene kale munkalimidwa ndi khasu, simudzapitamo kuopa mkandankhuku ndi minga; malowo adzasanduka odyetserako ngʼombe ndi nkhosa.
Ma na mauna a pau i olaolaoia i ka oo, Aohe mea hele ilaila, No ka makau i ka laau kalakala, a me ka nahele ooi: He wahi ia e hoouna aku ai i ka bipi, He wahi hoi e hahi ai na hipa.

< Yesaya 7 >