< Yesaya 7 >
1 Pamene Ahazi mwana wa Yotamu, mdzukulu wa Uziya anali mfumu ya Yuda, Rezini mfumu ya Siriya ndi Peka mwana wa Remaliya, mfumu ya Israeli anabwera kudzathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu, koma sanathe kuwugonjetsa.
Du temps d'Achaz, fils de Jotham, fils d'Ozias, roi de Juda, Retsin, roi de Syrie, et Pékah, fils de Remalia, roi d'Israël, montèrent à Jérusalem pour lui faire la guerre, mais ils ne purent l'emporter.
2 Tsono nyumba ya Davide inawuzidwa kuti, “Dziko la Siriya lagwirizana ndi Efereimu.” Choncho mfumu Ahazi ndi anthu ake ananjenjemera, monga momwe mitengo ya mʼnkhalango imagwedezekera ndi mphepo.
On dit à la maison de David: « La Syrie est alliée à Ephraïm. » Son cœur trembla, et le cœur de son peuple, comme les arbres de la forêt tremblent sous l'effet du vent.
3 Pamenepo Yehova anawuza Yesaya kuti, “Tuluka, iwe ndi mwana wako Seariyasubu, mupite mukakumane ndi Ahazi kumapeto kwa ngalande yamadzi yochokera ku Dziwe Lakumtunda, pa msewu wopita ku Munda wa mmisiri wochapa nsalu.
Et Yahvé dit à Ésaïe: « Va à la rencontre d'Achaz, toi et Shearjashub, ton fils, à l'extrémité du conduit de l'étang supérieur, sur la route du champ du foulon.
4 Ukamuwuze kuti, ‘Chenjera, khala phee ndipo usaope. Usataye mtima chifukwa cha zitsa ziwiri zomwe zikufuka, chifukwa cha ukali woopsa wa Rezini ndi Siriya, ndiponso wa Peka mwana wa Remaliya.
Tu lui diras: « Prends garde et reste calme. N'aie pas peur, et que ton cœur ne s'affaiblisse pas à cause de ces deux queues de torches fumantes, à cause de la colère ardente de Retsin et de la Syrie, et du fils de Remalia.
5 Mfumu ya Siriya, Efereimu ndi mwana wa Remaliya apangana kuti akuchitire choyipa. Akunena kuti,
Car la Syrie, Éphraïm et le fils de Remalia ont comploté contre toi, en disant:
6 ‘Tiyeni tikalimbane ndi Yuda. Tiyeni tiliwononge ndi kuligawa; tiligawane pakati pathu, ndipo tilonge ufumu mwana wa Tabeeli kumeneko.’
« Montons contre Juda, et déchirons-le, et partageons-le entre nous, et établissons-y un roi, le fils de Tabeel. »
7 Komabe zimene akunena Ambuye Yehova ndi izi: “‘Zimenezo sizidzatheka, sizidzachitika konse,
Voici ce que dit le Seigneur Yahvé: « Cela ne tiendra pas, cela n'arrivera pas. »
8 pakuti Siriya amadalira Damasiko, ndipo Damasiko amadalira mfumu Rezini basi. Zisanathe zaka 65 Efereimu adzawonongedwa kotheratu, sadzakhalanso mtundu wa anthu.
Car le chef de la Syrie est Damas, et le chef de Damas est Rezin. Dans l'espace de soixante-cinq ans, Éphraïm sera brisé en morceaux, de sorte qu'il ne sera plus un peuple.
9 Dziko la Efereimu limadalira Samariya ndipo Samariya amadalira mwana wa Remaliya basi. Mukapanda kulimbika pa chikhulupiriro chanu, ndithu simudzalimba konse.’”
Le chef d'Éphraïm, c'est Samarie, et le chef de Samarie, c'est le fils de Remalia. Si vous ne voulez pas croire, vous ne serez pas établis.'"
10 Yehova anayankhulanso ndi Ahazi,
Yahvé parla de nouveau à Achaz et dit:
11 “Pempha chizindikiro kwa Yehova Mulungu wako, chikhale chozama ngati manda kapena chachitali ngati mlengalenga.” (Sheol )
« Demande un signe à Yahvé ton Dieu; demande-le soit dans la profondeur, soit dans la hauteur. » (Sheol )
12 Koma Ahazi anati, “Ine sindipempha; sindikufuna kuyesa Yehova.”
Mais Achaz dit: « Je ne demanderai rien. Je ne tenterai pas Yahvé. »
13 Apo Yesaya anati, “Imva tsopano, iwe nyumba ya Davide! Kodi sikokwanira kutopetsa anthu? Kodi mudzayeseranso kutopetsa Mulungu wanga?
Il dit: « Écoutez maintenant, maison de David. N'est-ce pas assez pour vous d'éprouver la patience des hommes, que vous éprouviez aussi la patience de mon Dieu?
14 Nʼchifukwa chake Ambuye mwini adzakupatsani chizindikiro: Onani, namwali adzakhala woyembekezera ndipo adzabala mwana wamwamuna, ndipo mwanayo adzamutcha Imanueli.
C'est pourquoi le Seigneur lui-même vous donnera un signe. Voici que la vierge concevra et enfantera un fils, et elle lui donnera le nom d'Emmanuel.
15 Azidzadya chambiko ndi uchi, mpaka atadziwa kukana choyipa ndi kusankha chabwino.
Il mangera du beurre et du miel, quand il saura refuser le mal et choisir le bien.
16 Koma nthawi yokana choyipa ndi kusankha chabwino kwa mwanayo isanafike, mayiko a mafumu awiri amene amakuopsaniwo adzakhala atasanduka bwinja.
Car avant que l'enfant sache refuser le mal et choisir le bien, le pays dont vous avez les deux rois en horreur sera abandonné.
17 Yehova adzabweretsa pa inu, pa anthu anu ndiponso pa nyumba ya bambo wanu masiku a mavuto woti sanakhalepo kuyambira tsiku limene Efereimu anapatukana ndi Yuda. Yehova adzabweretsa mfumu ya ku Asiriya.”
Yahvé fera venir sur toi, sur ton peuple et sur la maison de ton père des jours qui ne sont pas venus, depuis le jour où Éphraïm s'est séparé de Juda, jusqu'au roi d'Assyrie.
18 Tsiku limenelo Yehova adzalizira likhweru ntchentche zochokera ku mitsinje yakutali ku Igupto, ndiponso njuchi zochokera ku dziko la Asiriya.
En ce jour-là, l'Éternel sifflera pour la mouche qui est à l'extrémité des fleuves d'Égypte, et pour l'abeille qui est au pays d'Assyrie.
19 Onsewo adzafika ndi kudzakhazikika mu zigwa zozama, mʼmingʼalu ya matanthwe ndi mʼzitsamba zonse zaminga ndiponso ponse pamene pali malo omwetsera ziweto.
Elles viendront et se reposeront toutes dans les vallées désolées, dans les fentes des rochers, sur toutes les haies d'épines et sur tous les pâturages.
20 Tsiku limenelo Ambuye adzalemba ganyu ometa ochokera kutsidya kwa Mtsinje, ndiye mfumu ya ku Asiriya, kudzameta tsitsi lanu la ku mutu ndi la mʼmiyendo ndi ndevu zomwe.
En ce jour-là, l'Éternel rasera avec un rasoir loué dans les régions situées au-delà du fleuve, avec le roi d'Assyrie, la tête et le poil des pieds, et il consumera aussi la barbe.
21 Tsiku limenelo adzangosunga ngʼombe yayikazi yayingʼono ndi mbuzi ziwiri.
Il arrivera en ce jour-là qu'un homme gardera en vie une jeune vache et deux brebis.
22 Ndipo chifukwa cha kuchuluka kwa mkaka umene ziwetozi zidzapereka, munthuyo azidzadya chambiko. Aliyense amene adzatsalire mʼdzikomo azidzadya chambiko ndi uchi.
Il arrivera qu'à cause de l'abondance du lait qu'elles donneront, il mangera du beurre, car tout le monde mangera du beurre et du miel qui restera dans le pays.
23 Tsiku limenelo, paliponse pamene panali mitengo ya mpesa 1,000 ndipo mtengo wake ndi wokwana masekeli asiliva 1,000, padzamera mkandankhuku ndi minga.
Il arrivera en ce jour-là que tout endroit où il y avait mille vignes valant mille sicles d'argent, sera pour des ronces et des épines.
24 Anthu adzapita kumeneko kukachita uzimba ali ndi uta ndi mivi, popeza kuti mʼdziko monsemo mudzakhala mkandankhuku ndi minga.
On s'y rendra avec des flèches et avec l'arc, car tout le pays ne sera que ronces et épines.
25 Ndipo mʼmapiri monse mʼmene kale munkalimidwa ndi khasu, simudzapitamo kuopa mkandankhuku ndi minga; malowo adzasanduka odyetserako ngʼombe ndi nkhosa.
Toutes les collines qui ont été cultivées à la houe, vous n'y viendrez pas par crainte des ronces et des épines; mais on y enverra des bœufs et on y piétinera des moutons. »