< Yesaya 7 >

1 Pamene Ahazi mwana wa Yotamu, mdzukulu wa Uziya anali mfumu ya Yuda, Rezini mfumu ya Siriya ndi Peka mwana wa Remaliya, mfumu ya Israeli anabwera kudzathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu, koma sanathe kuwugonjetsa.
And it was don in the daies of Achas, the sone of Joathan, the sone of Osias, kyng of Juda, Rasyn, the kyng of Sirie, and Facee, the sone of Romelie, the kyng of Israel, stieden to Jerusalem, for to fiyte ayens it; and thei myyten not ouercome it.
2 Tsono nyumba ya Davide inawuzidwa kuti, “Dziko la Siriya lagwirizana ndi Efereimu.” Choncho mfumu Ahazi ndi anthu ake ananjenjemera, monga momwe mitengo ya mʼnkhalango imagwedezekera ndi mphepo.
And thei telden to the hous of Dauid, and seiden, Sirie hath restid on Effraym, and the herte of hym and of his puple was mouyd togidere, as the trees of wodis ben mouyd of the face of the wynd.
3 Pamenepo Yehova anawuza Yesaya kuti, “Tuluka, iwe ndi mwana wako Seariyasubu, mupite mukakumane ndi Ahazi kumapeto kwa ngalande yamadzi yochokera ku Dziwe Lakumtunda, pa msewu wopita ku Munda wa mmisiri wochapa nsalu.
And the Lord seide to Isaie, Go thou out, and Jasub, thi sone, which is left, in to the meetyng of Achas, at the laste ende of the water cundijt of the hiyere cisterne, in the weie of the feeld of the fullere.
4 Ukamuwuze kuti, ‘Chenjera, khala phee ndipo usaope. Usataye mtima chifukwa cha zitsa ziwiri zomwe zikufuka, chifukwa cha ukali woopsa wa Rezini ndi Siriya, ndiponso wa Peka mwana wa Remaliya.
And thou schalt seie to hym, Se thou, that thou be stille; nyle thou drede, and thin herte be not aferd of twei tailis of these brondis smokynge in the wraththe of woodnesse, of Rasyn, kynge of Sirie, and of the sone of Romelye.
5 Mfumu ya Siriya, Efereimu ndi mwana wa Remaliya apangana kuti akuchitire choyipa. Akunena kuti,
For Sirie, and Effraym, and the sone of Romelie, han bigunne yuel councel ayens thee, and seien, Stie we to Juda,
6 ‘Tiyeni tikalimbane ndi Yuda. Tiyeni tiliwononge ndi kuligawa; tiligawane pakati pathu, ndipo tilonge ufumu mwana wa Tabeeli kumeneko.’
and reise we hym, and drawe we hym out to vs; and sette we a kyng in the myddis therof, the sone of Tabeel.
7 Komabe zimene akunena Ambuye Yehova ndi izi: “‘Zimenezo sizidzatheka, sizidzachitika konse,
The Lord God seith these thingis, This schal not be, and it schal not stonde;
8 pakuti Siriya amadalira Damasiko, ndipo Damasiko amadalira mfumu Rezini basi. Zisanathe zaka 65 Efereimu adzawonongedwa kotheratu, sadzakhalanso mtundu wa anthu.
but Damask schal be the heed of Sirie, and Rasyn `schal be the heed of Damask; and yit sixti yeer and fiue, and Effraym schal faile to be a puple;
9 Dziko la Efereimu limadalira Samariya ndipo Samariya amadalira mwana wa Remaliya basi. Mukapanda kulimbika pa chikhulupiriro chanu, ndithu simudzalimba konse.’”
and Samarie shal faile to be the heed of Effraym, and the sone of Romelie `schal faile to be heed of Samarie. Forsothe if ye schulen not bileue, ye schulen not dwelle.
10 Yehova anayankhulanso ndi Ahazi,
And the Lord addide to speke to Achas,
11 “Pempha chizindikiro kwa Yehova Mulungu wako, chikhale chozama ngati manda kapena chachitali ngati mlengalenga.” (Sheol h7585)
and seide, Axe thou to thee a signe of thi Lord God, in to the depthe of helle, ethir in to heiythe aboue. (Sheol h7585)
12 Koma Ahazi anati, “Ine sindipempha; sindikufuna kuyesa Yehova.”
And Achas seide, Y schal not axe, and Y schal not tempte the Lord.
13 Apo Yesaya anati, “Imva tsopano, iwe nyumba ya Davide! Kodi sikokwanira kutopetsa anthu? Kodi mudzayeseranso kutopetsa Mulungu wanga?
And Ysaie seide, Therfor the hous of Dauid, here ye; whether it is litil to you to be diseseful to men, for ye ben diseseful also to my God?
14 Nʼchifukwa chake Ambuye mwini adzakupatsani chizindikiro: Onani, namwali adzakhala woyembekezera ndipo adzabala mwana wamwamuna, ndipo mwanayo adzamutcha Imanueli.
For this thing the Lord hym silf schal yyue a signe to you. Lo! a virgyn schal conseyue, and schal bere a sone; and his name schal be clepid Emanuel.
15 Azidzadya chambiko ndi uchi, mpaka atadziwa kukana choyipa ndi kusankha chabwino.
He schal ete botere and hony, that he kunne repreue yuel, and cheese good.
16 Koma nthawi yokana choyipa ndi kusankha chabwino kwa mwanayo isanafike, mayiko a mafumu awiri amene amakuopsaniwo adzakhala atasanduka bwinja.
For whi bifore that the child kunne repreue yuel, and chese good, the lond, which thou wlatist, schal be forsakun of the face of her twei kyngis.
17 Yehova adzabweretsa pa inu, pa anthu anu ndiponso pa nyumba ya bambo wanu masiku a mavuto woti sanakhalepo kuyambira tsiku limene Efereimu anapatukana ndi Yuda. Yehova adzabweretsa mfumu ya ku Asiriya.”
The Lord schal brynge on thee, and on thi puple, and on the hous of thi fadir, daies that camen not fro the daies of departyng of Effraym fro Juda, with the kyng of Assiriens.
18 Tsiku limenelo Yehova adzalizira likhweru ntchentche zochokera ku mitsinje yakutali ku Igupto, ndiponso njuchi zochokera ku dziko la Asiriya.
And it schal be, in that dai the Lord schal hisse to a flie, which is in the laste parte of the floodis of Egipt; and to a bee, which is in the lond of Assur;
19 Onsewo adzafika ndi kudzakhazikika mu zigwa zozama, mʼmingʼalu ya matanthwe ndi mʼzitsamba zonse zaminga ndiponso ponse pamene pali malo omwetsera ziweto.
and `alle so schulen come, and schulen reste in the strondis of valeis, and in caues of stoonis, and in alle places of buyschis, and in alle hoolis.
20 Tsiku limenelo Ambuye adzalemba ganyu ometa ochokera kutsidya kwa Mtsinje, ndiye mfumu ya ku Asiriya, kudzameta tsitsi lanu la ku mutu ndi la mʼmiyendo ndi ndevu zomwe.
And in that dai the Lord schal schaue with a scharp rasour in these men, that ben biyendis the flood, in the kyng of Assiriens, the heed, and heeris of the feet, and al the beerd.
21 Tsiku limenelo adzangosunga ngʼombe yayikazi yayingʼono ndi mbuzi ziwiri.
And it schal be, in that day a man schal nurische a cow of oxis, and twei scheep,
22 Ndipo chifukwa cha kuchuluka kwa mkaka umene ziwetozi zidzapereka, munthuyo azidzadya chambiko. Aliyense amene adzatsalire mʼdzikomo azidzadya chambiko ndi uchi.
and for the plentee of mylk he schal ete botere; for whi ech man that schal be left in the myddis of the lond, schal ete boter and hony.
23 Tsiku limenelo, paliponse pamene panali mitengo ya mpesa 1,000 ndipo mtengo wake ndi wokwana masekeli asiliva 1,000, padzamera mkandankhuku ndi minga.
And it schal be, in that dai ech place where a thousand vyneris schulen be worth a thousynde platis of siluer, and schulen be in to thornes and breeris,
24 Anthu adzapita kumeneko kukachita uzimba ali ndi uta ndi mivi, popeza kuti mʼdziko monsemo mudzakhala mkandankhuku ndi minga.
men schulen entre thidur with bouwis and arowis; for whi breris and thornes schulen be in al the lond.
25 Ndipo mʼmapiri monse mʼmene kale munkalimidwa ndi khasu, simudzapitamo kuopa mkandankhuku ndi minga; malowo adzasanduka odyetserako ngʼombe ndi nkhosa.
And alle hillis that schulen be purgid with a sarpe, the drede of thornes and of breris schal not come thidir; and it schal be in to lesewe of oxen, and in to treding of scheep.

< Yesaya 7 >