< Yesaya 66 >
1 Yehova akuti, “Kumwamba ndi mpando wanga waufumu ndipo dziko lapansi ndilo chopondapo mapazi anga. Tsono nyumba ili kuti yomwe mundimangire, ndipo malo ali kuti amene inu mungandikonzere kuti ndizipumuliramo?
RAB diyor ki, “Gökler tahtım, Yeryüzü ayaklarımın taburesidir. Nerede benim için yapacağınız ev, Neresi dinleneceğim yer?
2 Kodi si manja anga amene anapanga zinthu zonsezi, motero zonsezi ndi zanga?” Akutero Yehova. “Koma munthu amene ndimakondwera naye ndi uyu: amene ali wodzichepetsa ndi wosweka mtima, ndipo amamvera mawu anga.
Çünkü bütün bunları ellerim yaptı, Hepsi böylece var oldu” diyor RAB. “Ancak ben alçakgönüllüye, ruhu ezik olana, Sözümden titreyen kişiye değer veririm.
3 Koma aliyense amene amapereka nsembe ngʼombe yayimuna amaphanso munthu, ndipo aliyense amene amapereka mwana wankhosa, amaphanso galu. Aliyense amene amapereka nsembe chopereka cha chakudya amaperekanso magazi a nkhumba. Ndipo amene amafukiza lubani pa guwa lansembe la chikumbutso amapembedzanso fano. Popeza iwo asankha njira zawozawo, ndiponso kusangalatsidwa ndi zonyansa zawo.
Sığır boğazlayan, adam öldüren gibidir, Davar kurban eden, köpek boynu kıran, Tahıl sunusu getiren, domuz kanı sunan, Anma sunusu olarak günnük yakan, putperest gibidir. Evet, bunlar kendi yollarını seçtiler, Yaptıkları iğrençliklerden hoşlanıyorlar.
4 Inenso ndawasankhira chilango chowawa ndipo ndidzabweretsa pa iwo zimene amaziopa zija. Pakuti pamene ndinawayitana palibe amene anayankha, pamene ndinayankhula palibe amene anatchera khutu. Anachita zoyipa pamaso panga ndi kusankha kuchita zimene zimandinyansa zija.”
Ben de onlar için yıkımı seçecek, Korktuklarını başlarına getireceğim. Çünkü çağırdığımda yanıt veren olmadı, Konuştuğumda dinlemediler, Gözümde kötü olanı yaptılar, Hoşlanmadığımı seçtiler.”
5 Imvani mawu a Yehova, inu amene mumanjenjemera ndi mawu ake: “Abale anu amene amakudani, ndi kukuchotsani pakati pawo chifukwa cha dzina langa, amanena kuti, ‘Yehova alemekezeke kuti ife tione chimwemwe chanu!’ Koma ndi iwowo amene adzachite manyazi.
RAB'bin sözünden titreyenler, Kulak verin O'nun söylediklerine: “Sizden nefret eden, Adımdan ötürü sizi dışlayan kardeşleriniz, ‘RAB yüceltilsin de sevincinizi görelim!’ diyorlar. Utandırılacak olan onlardır.
6 Imvani mfuwu mu mzinda, imvani phokoso mʼNyumba ya Mulungu! Limenelo ndi liwu la Yehova, kulanga adani ake onse.
Kentten gürültülü sesler, Tapınaktan bir ses yükseliyor! Düşmanlarına hak ettikleri karşılığı veren RAB'bin sesidir bu.
7 “Mzinda uli ngati amayi apakati amene asanayambe kumva zowawa wachira kale; asanayambe kumva ululu, wabala kale mwana wamwamuna.
“Doğum sancısı çekmeden doğurdu, Sancısı tutmadan bir erkek çocuk doğurdu.
8 Ndani anamvapo zinthu zoterezi? Ndani anazionapo zinthu zoterezi? Kodi dziko nʼkupangika tsiku limodzi, kapena mtundu wa anthu nʼkubadwa tsiku limodzi? Komatu Ziyoni atangoyamba kumva zowawa nthawi yomweyo anabereka ana ake.
Kim böyle bir şey duydu? Kim böyle şeyler gördü? Bir ülke bir günde doğar mı, Bir anda doğar mı bir ulus? Ama Siyon, ağrısı tutar tutmaz çocuklarını doğurdu.
9 Kodi Ine ndingangofikitsa amayi apakati mpaka nthawi yake yochira, koma osalola kuti abaledi mwana?” akutero Yehova. “Kodi ndingatseke mimba pa nthawi yoti abeleke?” akutero Mulungu wako.
Doğum anına dek getiririm de Doğuracak gücü vermez miyim?” diyor RAB. “Doğuracak güç veren ben, rahmi kapatır mıyım?” diyor Tanrın.
10 “Kondwera nayeni Yerusalemu ndipo musangalale chifukwa cha Iye, inu nonse amene mumakonda Yerusalemu, kondwera nayeni kwambiri, nonse amene mumamulira.
“Yeruşalim'le birlikte sevinin, Onu sevenler, hepiniz onun için coşun, Yeruşalim için yas tutanlar, onunla sevinçle coşun.
11 Pakuti mudzagawana naye ulemerero wake ngati kuyamwa ndi kukhuta mkaka wambiri wa mʼmawere a chitonthozo chake.”
Öyle ki, onun avutucu memelerini emip doyasınız, Kana kana içip Onun yüce bolluğundan zevk alasınız.”
12 Yehova akuti, “Ndidzamupatsa mtendere ngati mtsinje wa madzi, ndiponso chuma cha anthu a mitundu ina ngati mtsinje wosefukira. Mudzakhala ngati mwana woyamwa amene amayi ake amunyamulira pambalipa, kapena kumufungata pa miyendo yake.
Çünkü RAB diyor ki, “Bakın, esenliği bir ırmak gibi, Ulusların servetini taşkın bir ırmak gibi ona akıtacağım. Ondan beslenecek, kucakta taşınacak, Dizleri üzerinde sallanacaksınız.
13 Monga momwe amayi amasangalatsira mwana wawo, moteronso Ine ndidzakusangalatsani; ndipo mudzasangalala chifukwa cha Yerusalemu.”
Çocuğunu avutan bir anne gibi avutacağım sizi, Yeruşalim'de avuntu bulacaksınız.
14 Mukadzaona zimenezi mitima yanu idzakondwera. Mudzabiriwira ngati udzu. Zimenezi zidzakulimbikitsani ndi kukupatsani moyo wamphamvu. Mudzadziwa kuti ndimathandiza amene amanditumikira ndi kuti ndimakwiyira adani anga.
Bunları gördüğünüzde yüreğiniz sevinecek, Bedenleriniz körpe ot gibi tazelenecek. Herkes bilecek ki, RAB'bin koruyucu eli kullarının, Gazabı ise düşmanlarının üzerindedir.”
15 Taonani, Yehova akubwera ngati moto, ndipo magaleta ake ali ngati kamvuluvulu; Iye adzaonetsa mkwiyo wake nadzalanga adani ake ndi malawi amoto.
Bakın, RAB ateşle geliyor, Savaş arabaları kasırga gibi. Şiddetli öfkesini, Azarını alev alev dökmek üzere.
16 Pakuti Yehova adzalanga anthu onse ndi moto ndi lupanga, Yehova adzapha anthu ambiri.
Çünkü O bütün insanlığı ateş ve kılıçla yargılayacak, Pek çok kişiyi öldürecek.
17 Yehova akuti, “Amene amadzipatula ndi kudziyeretsa okha kuti apite ku minda, ali ndi mtsogoleri awo, nʼkumadya nyama ya nkhumba, mbewa ndi zinthu zina zonyansa, onsewa adzafera limodzi.”
“Bahçelere girmek için kendilerini arıtıp kutsayanlar, domuz, fare ve öteki iğrenç hayvanların etini yiyenlerin ortasında duranı izleyenler hep birlikte yok olacaklar” diyor RAB,
18 “Ndipo Ine, chifukwa cha zochita zawo ndi maganizo awo, ndili pafupi kubwera kudzasonkhanitsa mitundu yonse ya anthu ndi ziyankhulo zonse. Iwo adzabwera ndi kuona ulemerero wanga.
“Çünkü ben onların eylemlerini de düşüncelerini de bilirim. Bütün ulusları ve dilleri bir araya toplayacağım an geliyor; gelip yüceliğimi görecekler.
19 “Ndidzayika chizindikiro pakati pawo, ndipo ndidzatumiza ena mwa iwowa amene anapulumuka kuti apite kwa anthu a mitundu ina inu ku Tarisisi, ku Libiya ndi ku Ludi (akatswiri a mauta) ku Tubala ndi Grisi, ndi ku mayiko akutali a mbali mwa nyanja amene sanamvepo za mbiri yanga kapena kuona ulemerero wanga. Iwo adzalalika za ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina.
“Aralarına bir belirti koyacağım. Onlardan kaçıp kurtulanları uluslara, Tarşiş'e, Pûl'a, Lud'a –yay gerenlere– Tuval'a, Yâvan'a, ünümü duymamış, yüceliğimi görmemiş uzak kıyı halklarına göndereceğim. Uluslar arasında yüceliğimi ilan edecekler.
20 Ndipo adzabwera nawo abale anu onse ngati mphatso yopereka kwa Yehova kuchokera kwa anthu a mitundu yonse. Iwo adzakwera nawo kupita ku Yerusalemu, phiri langa loyera ku Yerusalemu monga nsembe kwa Yehova, atakwera akavalo, magaleta ndi ngolo, ndi pa abulu ndi ngamira,” akutero Yehova. “Adzabwera nawo ngati momwe Aisraeli amabwerera ndi zopereka zachakudya ku Nyumba ya Yehova mu ziwiya zoyeretsedwa monga mwa mwambo.
İsrailoğulları tahıl sunularını pak kaplar içinde RAB'bin Tapınağı'na nasıl getiriyorsa, onlar da bütün kardeşlerinizi uluslardan atlarla, savaş arabalarıyla, at arabalarıyla, katırlarla, develerle kutsal dağıma, Yeruşalim'e, RAB'be sunu olarak getirecekler.” Böyle diyor RAB.
21 Ndipo ndidzasankha ena mwa iwonso kukhala ansembe ndi Alevi,” akutero Yehova.
“Onların arasından kimilerini kâhin ve Levili olarak seçeceğim” diyor RAB.
22 “Monga momwe mlengalenga mwatsopano ndi dziko lapansi latsopano zimene ndidzapanga zidzakhala mpaka muyaya pamaso panga, ndi chonchonso dzina lanu ndi zidzukulu zanu zidzakhalire.” Akutero Yehova.
“Çünkü yaratacağım yeni yer ve gök önümde nasıl duracaksa, soyunuz ve adınız da öyle duracak” diyor RAB.
23 “Anthu a mitundu yonse adzabwera kudzandipembedza ku Yerusalemu, pa chikondwerero chilichonse cha pokhala pa mwezi watsopano ndi tsiku la Sabata lililonse,” akutero Yehova.
“Yeni Ay'dan Yeni Ay'a, Şabat Günü'nden Şabat Günü'ne bütün insanlar önüme gelip bana tapınacaklar” diyor RAB.
24 “Akamachoka adzaona mitembo ya anthu amene anandiwukira Ine. Mphutsi zawo sizidzafa, kapena moto wawo sudzazimitsidwa. Anthu a mitundu ina yonse powaona adzanyansidwa nawo.”
“Dışarı çıktıklarında bana başkaldırmış olanların cesetlerini görecekler. Öylelerini kemiren kurt ölmez, yakan ateş sönmez. Bütün insanlar onlardan iğrenecek.”