< Yesaya 66 >

1 Yehova akuti, “Kumwamba ndi mpando wanga waufumu ndipo dziko lapansi ndilo chopondapo mapazi anga. Tsono nyumba ili kuti yomwe mundimangire, ndipo malo ali kuti amene inu mungandikonzere kuti ndizipumuliramo?
Аша ворбеште Домнул: „Черул есте скаунул Меу де домние ши пэмынтул есте аштернутул пичоарелор Меле! Че касэ аць путя вой сэ-Мь зидиць ши че лок Мь-аць путя вой да ка локуинцэ?
2 Kodi si manja anga amene anapanga zinthu zonsezi, motero zonsezi ndi zanga?” Akutero Yehova. “Koma munthu amene ndimakondwera naye ndi uyu: amene ali wodzichepetsa ndi wosweka mtima, ndipo amamvera mawu anga.
Тоате ачесте лукрурь доар мына Мя ле-а фэкут ши тоате шь-ау кэпэтат астфел фиинца”, зиче Домнул. „Ятэ спре чине Ымь вой ындрепта привириле: спре чел че суферэ ши аре духул мыхнит, спре чел че се теме де Кувынтул Меу.
3 Koma aliyense amene amapereka nsembe ngʼombe yayimuna amaphanso munthu, ndipo aliyense amene amapereka mwana wankhosa, amaphanso galu. Aliyense amene amapereka nsembe chopereka cha chakudya amaperekanso magazi a nkhumba. Ndipo amene amafukiza lubani pa guwa lansembe la chikumbutso amapembedzanso fano. Popeza iwo asankha njira zawozawo, ndiponso kusangalatsidwa ndi zonyansa zawo.
Чине ынжунгие ун боу ка жертфэ ну есте май бун декыт чел че учиде ун ом; чине жертфеште ун мел есте ка чел че ар рупе гытул унуй кыне, чине адуче ун дар де мынкаре есте ка чел че ар вэрса сынӂе де порк, чине арде тэмые есте ка чел че с-ар ынкина ла идоль; тоць ачештя ышь алег кэиле лор, ши суфлетул лор гэсеште плэчере ын урычуниле лор.
4 Inenso ndawasankhira chilango chowawa ndipo ndidzabweretsa pa iwo zimene amaziopa zija. Pakuti pamene ndinawayitana palibe amene anayankha, pamene ndinayankhula palibe amene anatchera khutu. Anachita zoyipa pamaso panga ndi kusankha kuchita zimene zimandinyansa zija.”
Де ачея ши Еу вой алеӂе че есте спре неферичиря лор ши вой адуче песте ей лукруриле де каре се тем, кэч, кынд ам кемат Еу, н-ау рэспунс ши, кынд ам ворбит Еу, н-ау аскултат, чи ау фэкут че есте рэу ынаинтя Мя ши ау алес че ну-Мь плаче!”
5 Imvani mawu a Yehova, inu amene mumanjenjemera ndi mawu ake: “Abale anu amene amakudani, ndi kukuchotsani pakati pawo chifukwa cha dzina langa, amanena kuti, ‘Yehova alemekezeke kuti ife tione chimwemwe chanu!’ Koma ndi iwowo amene adzachite manyazi.
Аскултаць Кувынтул Домнулуй, вой, каре вэ темець де Кувынтул Луй: „Ятэ че зик фраций воштри, каре вэ урэск ши вэ изгонеск дин причина Нумелуй Меу: ‘Сэ-Шь арате Домнул слава, ка сэ вэ ведем букурия!’ Дар ей вор рэмыне де рушине!
6 Imvani mfuwu mu mzinda, imvani phokoso mʼNyumba ya Mulungu! Limenelo ndi liwu la Yehova, kulanga adani ake onse.
Ун глас рэсунэтор есе дин четате! Ун глас есе дин Темплу! Есте гласул Домнулуй, каре дэ врэжмашилор Луй плата кувенитэ!
7 “Mzinda uli ngati amayi apakati amene asanayambe kumva zowawa wachira kale; asanayambe kumva ululu, wabala kale mwana wamwamuna.
Ынаинте ка сэ симтэ дурерь, а нэскут ши, ынаинте ка сэ-й винэ суферинцеле, а дат наштере унуй фиу.
8 Ndani anamvapo zinthu zoterezi? Ndani anazionapo zinthu zoterezi? Kodi dziko nʼkupangika tsiku limodzi, kapena mtundu wa anthu nʼkubadwa tsiku limodzi? Komatu Ziyoni atangoyamba kumva zowawa nthawi yomweyo anabereka ana ake.
Чине а аузит вреодатэ аша чева? Чине а вэзут вреодатэ аша чева? Се поате наште оаре о царэ ынтр-о зи? Се наште ун ням аша динтр-одатэ? Абя ау апукат-о мунчиле, ши фийка Сионулуй шь-а ши нэскут фиий!
9 Kodi Ine ndingangofikitsa amayi apakati mpaka nthawi yake yochira, koma osalola kuti abaledi mwana?” akutero Yehova. “Kodi ndingatseke mimba pa nthawi yoti abeleke?” akutero Mulungu wako.
Аш путя сэ дескид пынтечеле мамей ши сэ ну о лас сэ наскэ?”, зиче Домнул. „Еу, каре фак сэ наскэ, аш путя сэ ымпедик оаре наштеря?”, зиче Думнезеул тэу.
10 “Kondwera nayeni Yerusalemu ndipo musangalale chifukwa cha Iye, inu nonse amene mumakonda Yerusalemu, kondwera nayeni kwambiri, nonse amene mumamulira.
Букураци-вэ ымпреунэ ку Иерусалимул ши веселици-вэ ку ел, тоць чей че-л юбиць; ымпэрциць ши букурия ку ел, акум, тоць чей че л-аць плынс,
11 Pakuti mudzagawana naye ulemerero wake ngati kuyamwa ndi kukhuta mkaka wambiri wa mʼmawere a chitonthozo chake.”
ка сэ фиць сэтураць бынд лаптеле мынгыерилор луй, ка сэ вэ десфэтаць ын тотул де плинэтатя славей луй.
12 Yehova akuti, “Ndidzamupatsa mtendere ngati mtsinje wa madzi, ndiponso chuma cha anthu a mitundu ina ngati mtsinje wosefukira. Mudzakhala ngati mwana woyamwa amene amayi ake amunyamulira pambalipa, kapena kumufungata pa miyendo yake.
Кэч аша ворбеште Домнул: „Ятэ, вой ындрепта спре ел пачя ка ун рыу ши слава нямурилор ка ун пырыу ешит дин маткэ ши вець фи алэптаць; вець фи пуртаць ын браце ши дезмердаць пе ӂенункь.
13 Monga momwe amayi amasangalatsira mwana wawo, moteronso Ine ndidzakusangalatsani; ndipo mudzasangalala chifukwa cha Yerusalemu.”
Кум мынгые пе чинева мама са, аша вэ вой мынгыя Еу; да, вець фи мынгыяць ын Иерусалим!
14 Mukadzaona zimenezi mitima yanu idzakondwera. Mudzabiriwira ngati udzu. Zimenezi zidzakulimbikitsani ndi kukupatsani moyo wamphamvu. Mudzadziwa kuti ndimathandiza amene amanditumikira ndi kuti ndimakwiyira adani anga.
Ши кынд вець ведя ачесте лукрурь, инима ви се ва букура ши оаселе воастре вор принде путере ка ярба.” Домнул Ышь ва арэта астфел путеря фацэ де робий Сэй, дар ва фаче пе врэжмаший Луй сэ-Й симтэ мыния.
15 Taonani, Yehova akubwera ngati moto, ndipo magaleta ake ali ngati kamvuluvulu; Iye adzaonetsa mkwiyo wake nadzalanga adani ake ndi malawi amoto.
Кэч ятэ, Домнул вине ынтр-ун фок ши кареле Луй сунт ка ун выртеж; Ышь префаче мыния ынтр-ун жэратик ши аменинцэриле, ын флэкэрь де фок.
16 Pakuti Yehova adzalanga anthu onse ndi moto ndi lupanga, Yehova adzapha anthu ambiri.
Кэч ку фок Ышь адуче Домнул ла ындеплинире жудекэциле ши ку сабия Луй педепсеште пе орьчине, ши чей учишь де Домнул вор фи мулць ла нумэр.
17 Yehova akuti, “Amene amadzipatula ndi kudziyeretsa okha kuti apite ku minda, ali ndi mtsogoleri awo, nʼkumadya nyama ya nkhumba, mbewa ndi zinthu zina zonyansa, onsewa adzafera limodzi.”
„Чей че се сфинцеск ши се курэцеск ын грэдинь, мергынд унул кыте унул ын мижлокул челор че мэнынкэ ши карне де порк, ши шоаречь, ши алте лукрурь урычоасе, тоць ачея вор пери”, зиче Домнул.
18 “Ndipo Ine, chifukwa cha zochita zawo ndi maganizo awo, ndili pafupi kubwera kudzasonkhanitsa mitundu yonse ya anthu ndi ziyankhulo zonse. Iwo adzabwera ndi kuona ulemerero wanga.
„Еу педепсеск фаптеле ши гындуриле лор! Дар вине время кынд вой стрынӂе тоате нямуриле ши тоате лимбиле; еле вор вени ши вор ведя слава Мя.
19 “Ndidzayika chizindikiro pakati pawo, ndipo ndidzatumiza ena mwa iwowa amene anapulumuka kuti apite kwa anthu a mitundu ina inu ku Tarisisi, ku Libiya ndi ku Ludi (akatswiri a mauta) ku Tubala ndi Grisi, ndi ku mayiko akutali a mbali mwa nyanja amene sanamvepo za mbiri yanga kapena kuona ulemerero wanga. Iwo adzalalika za ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina.
Ши вой пуне ун семн ынтре еле ши вой тримите ла нямурь пе чей че вор скэпа дин Исраел, ла Тарсис, ла Пул ши ла Луд, каре траг ку аркул, ла Тубал ши ла Иаван, ын остроавеле депэртате, каре н-ау аузит ворбинду-се ничодатэ де Мине ши н-ау вэзут слава Мя; ей вор вести слава Мя принтре нямурь.
20 Ndipo adzabwera nawo abale anu onse ngati mphatso yopereka kwa Yehova kuchokera kwa anthu a mitundu yonse. Iwo adzakwera nawo kupita ku Yerusalemu, phiri langa loyera ku Yerusalemu monga nsembe kwa Yehova, atakwera akavalo, magaleta ndi ngolo, ndi pa abulu ndi ngamira,” akutero Yehova. “Adzabwera nawo ngati momwe Aisraeli amabwerera ndi zopereka zachakudya ku Nyumba ya Yehova mu ziwiya zoyeretsedwa monga mwa mwambo.
Вор адуче пе тоць фраций воштри дин мижлокул тутурор нямурилор, ка дар Домнулуй, пе кай, ын каре ши пе тэрӂь, пе катырь ши пе дромадерь, ла мунтеле Меу чел сфынт, ла Иерусалим”, зиче Домнул, „кум ышь адук копиий луй Исраел даруриле де мынкаре, ынтр-ун вас курат, ла Каса Домнулуй.
21 Ndipo ndidzasankha ena mwa iwonso kukhala ansembe ndi Alevi,” akutero Yehova.
Ши вой луа ши динтре ей пе уний ка преоць ши левиць”, зиче Домнул.
22 “Monga momwe mlengalenga mwatsopano ndi dziko lapansi latsopano zimene ndidzapanga zidzakhala mpaka muyaya pamaso panga, ndi chonchonso dzina lanu ndi zidzukulu zanu zidzakhalire.” Akutero Yehova.
„Кэч дупэ кум черуриле челе ной ши пэмынтул чел ноу пе каре ле вой фаче вор дэйнуи ынаинтя Мя”, зиче Домнул, „аша вор дэйнуи ши сэмынца воастрэ ши нумеле востру.
23 “Anthu a mitundu yonse adzabwera kudzandipembedza ku Yerusalemu, pa chikondwerero chilichonse cha pokhala pa mwezi watsopano ndi tsiku la Sabata lililonse,” akutero Yehova.
Ын фиекаре лунэ ноуэ ши ын фиекаре Сабат, ва вени орьче фэптурэ сэ се ынкине ынаинтя Мя”, зиче Домнул.
24 “Akamachoka adzaona mitembo ya anthu amene anandiwukira Ine. Mphutsi zawo sizidzafa, kapena moto wawo sudzazimitsidwa. Anthu a mitundu ina yonse powaona adzanyansidwa nawo.”
„Ши, кынд вор еши, вор ведя трупуриле моарте але оаменилор каре с-ау рэзврэтит ымпотрива Мя, кэч вермеле лор ну ва мури ши фокул лор ну се ва стинӂе ши вор фи о причинэ де гроазэ пентру орьче фэптурэ.”

< Yesaya 66 >