< Yesaya 66 >

1 Yehova akuti, “Kumwamba ndi mpando wanga waufumu ndipo dziko lapansi ndilo chopondapo mapazi anga. Tsono nyumba ili kuti yomwe mundimangire, ndipo malo ali kuti amene inu mungandikonzere kuti ndizipumuliramo?
Also spricht Jehovah: Die Himmel sind Mein Thron, und die Erde Meiner Füße Schemel. Was für ein Haus wollt ihr Mir denn bauen, und welchen Ort zu Meiner Ruhe?
2 Kodi si manja anga amene anapanga zinthu zonsezi, motero zonsezi ndi zanga?” Akutero Yehova. “Koma munthu amene ndimakondwera naye ndi uyu: amene ali wodzichepetsa ndi wosweka mtima, ndipo amamvera mawu anga.
Und alles dies hat Meine Hand gemacht, so daß das alles geworden ist, spricht Jehovah. Und Ich blicke auf diesen, auf den Elenden, und auf den, der zerschlagenen Geistes ist, und der erzittert ob Meinem Wort.
3 Koma aliyense amene amapereka nsembe ngʼombe yayimuna amaphanso munthu, ndipo aliyense amene amapereka mwana wankhosa, amaphanso galu. Aliyense amene amapereka nsembe chopereka cha chakudya amaperekanso magazi a nkhumba. Ndipo amene amafukiza lubani pa guwa lansembe la chikumbutso amapembedzanso fano. Popeza iwo asankha njira zawozawo, ndiponso kusangalatsidwa ndi zonyansa zawo.
Wer einen Ochsen schlachtet, ist, als erschlüge er einen Mann; wer ein Schaf opfert, als bräche er einem Hunde das Genick, wer ein Speiseopfer als einer, der Blut der Schweine darbringt, wer Weihrauch anzündet, wie wer das Unrecht segnet; wie ihre eigenen Wege sie erwählten, und an ihren Abscheulichkeiten ihre Seele Lust hat,
4 Inenso ndawasankhira chilango chowawa ndipo ndidzabweretsa pa iwo zimene amaziopa zija. Pakuti pamene ndinawayitana palibe amene anayankha, pamene ndinayankhula palibe amene anatchera khutu. Anachita zoyipa pamaso panga ndi kusankha kuchita zimene zimandinyansa zija.”
So wähle auch Ich Mir ihre Mißhandlung aus, und laß ihr Bangen kommen über sie; weil Ich rief und niemand antwortete, Ich redete und niemand hörte, und sie taten, was böse war in Meinen Augen, und wählten zu tun, woran Ich keine Lust hatte.
5 Imvani mawu a Yehova, inu amene mumanjenjemera ndi mawu ake: “Abale anu amene amakudani, ndi kukuchotsani pakati pawo chifukwa cha dzina langa, amanena kuti, ‘Yehova alemekezeke kuti ife tione chimwemwe chanu!’ Koma ndi iwowo amene adzachite manyazi.
Höret Jehovahs Wort, ihr, die ihr erzittert vor Seinem Wort: Es sprachen eure Brüder, die euch hassen, euch ob Meines Namens ausscheiden: Jehovah verherrliche Sich, daß wir eure Fröhlichkeit sehen; aber sie sollen beschämt werden.
6 Imvani mfuwu mu mzinda, imvani phokoso mʼNyumba ya Mulungu! Limenelo ndi liwu la Yehova, kulanga adani ake onse.
Man hört die Stimme des Tosens aus der Stadt, vom Tempel eine Stimme, Jehovahs Stimme, Der Vergeltung erweist Seinen Feinden.
7 “Mzinda uli ngati amayi apakati amene asanayambe kumva zowawa wachira kale; asanayambe kumva ululu, wabala kale mwana wamwamuna.
Ehe sie kreißt, gebiert sie; ehe sie in Geburtsnöten kommt, ist sie eines Männlichen entbunden.
8 Ndani anamvapo zinthu zoterezi? Ndani anazionapo zinthu zoterezi? Kodi dziko nʼkupangika tsiku limodzi, kapena mtundu wa anthu nʼkubadwa tsiku limodzi? Komatu Ziyoni atangoyamba kumva zowawa nthawi yomweyo anabereka ana ake.
Wer hat solches gehört; wer solches gesehen? Hat ein Land an einem Tag gekreißt eine Völkerschaft, geboren mit einem Mal, wie Zijon mit seinen Söhnen gekreißt und sie geboren hat?
9 Kodi Ine ndingangofikitsa amayi apakati mpaka nthawi yake yochira, koma osalola kuti abaledi mwana?” akutero Yehova. “Kodi ndingatseke mimba pa nthawi yoti abeleke?” akutero Mulungu wako.
Und sollte Ich brechen und nicht gebären lassen, spricht Jehovah, und sollte Ich, Der gebären ließ, verschließen? spricht dein Gott.
10 “Kondwera nayeni Yerusalemu ndipo musangalale chifukwa cha Iye, inu nonse amene mumakonda Yerusalemu, kondwera nayeni kwambiri, nonse amene mumamulira.
Seid fröhlich mit Jerusalem, und frohlokket in ihr, ihr alle, die ihr es liebt. Freuet euch mit Freude mit ihr, die ihr über sie getrauert.
11 Pakuti mudzagawana naye ulemerero wake ngati kuyamwa ndi kukhuta mkaka wambiri wa mʼmawere a chitonthozo chake.”
Denn ihr sollt saugen und euch sättigen aus der Brust ihrer Tröstungen, denn ihr sollt ausdrücken und euch erlaben an der Pracht ihrer Herrlichkeit.
12 Yehova akuti, “Ndidzamupatsa mtendere ngati mtsinje wa madzi, ndiponso chuma cha anthu a mitundu ina ngati mtsinje wosefukira. Mudzakhala ngati mwana woyamwa amene amayi ake amunyamulira pambalipa, kapena kumufungata pa miyendo yake.
Denn also spricht Jehovah: Siehe, Ich breite Frieden wie einen Strom aus auf sie, und wie einen überflutenden Bach die Herrlichkeit der Völkerschaften, daß ihr sauget. Auf der Seite wird man euch tragen und werdet euch ergötzen auf den Knien.
13 Monga momwe amayi amasangalatsira mwana wawo, moteronso Ine ndidzakusangalatsani; ndipo mudzasangalala chifukwa cha Yerusalemu.”
Wie einen seine Mutter tröstet, so will Ich euch trösten, und ihr sollt getröstet werden in Jerusalem.
14 Mukadzaona zimenezi mitima yanu idzakondwera. Mudzabiriwira ngati udzu. Zimenezi zidzakulimbikitsani ndi kukupatsani moyo wamphamvu. Mudzadziwa kuti ndimathandiza amene amanditumikira ndi kuti ndimakwiyira adani anga.
Und ihr werdet es sehen, und euer Herz wird sich freuen, und sprossen werden eure Gebeine wie junges Kraut; und kund wird Jehovahs Hand an Seinen Knechten, und wider Seine Feinde ist Er unwillig.
15 Taonani, Yehova akubwera ngati moto, ndipo magaleta ake ali ngati kamvuluvulu; Iye adzaonetsa mkwiyo wake nadzalanga adani ake ndi malawi amoto.
Denn siehe, Jehovah kommt im Feuer und wie der Sturmwind Seine Streitwagen, zu vergelten in Seines Zornes Grimm und Sein Drohen in den Flammen des Feuers.
16 Pakuti Yehova adzalanga anthu onse ndi moto ndi lupanga, Yehova adzapha anthu ambiri.
Denn mit dem Feuer wird Jehovah richten, und mit Seinem Schwerte alles Fleisch, und viel wird werden der Erschlagenen Jehovahs.
17 Yehova akuti, “Amene amadzipatula ndi kudziyeretsa okha kuti apite ku minda, ali ndi mtsogoleri awo, nʼkumadya nyama ya nkhumba, mbewa ndi zinthu zina zonyansa, onsewa adzafera limodzi.”
Die, so sich heiligen und reinigen für die Gärten hinter einem her inmitten ihrer, die da essen des Schweines Fleisch und des Abscheulichen und der Mäuse, sie werden weggerafft allzumal! spricht Jehovah.
18 “Ndipo Ine, chifukwa cha zochita zawo ndi maganizo awo, ndili pafupi kubwera kudzasonkhanitsa mitundu yonse ya anthu ndi ziyankhulo zonse. Iwo adzabwera ndi kuona ulemerero wanga.
Ich aber kenne ihre Werke und Gedanken. Es kommt, daß man zusammenbringt alle Völkerschaften und Zungen und sie kommen und sehen Meine Herrlichkeit.
19 “Ndidzayika chizindikiro pakati pawo, ndipo ndidzatumiza ena mwa iwowa amene anapulumuka kuti apite kwa anthu a mitundu ina inu ku Tarisisi, ku Libiya ndi ku Ludi (akatswiri a mauta) ku Tubala ndi Grisi, ndi ku mayiko akutali a mbali mwa nyanja amene sanamvepo za mbiri yanga kapena kuona ulemerero wanga. Iwo adzalalika za ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina.
Und setzen werde Ich unter sie ein Zeichen und senden aus ihnen Entkommene zu den Völkerschaften Tharschisch, Pul und Lud, die den Bogen spannen, Thubal und Javan und zu den fernen Inseln, die nicht Mein Gerücht gehört und nicht gesehen Meine Herrlichkeit. Und sie werden Meine Herrlichkeit verkünden unter den Völkerschaften.
20 Ndipo adzabwera nawo abale anu onse ngati mphatso yopereka kwa Yehova kuchokera kwa anthu a mitundu yonse. Iwo adzakwera nawo kupita ku Yerusalemu, phiri langa loyera ku Yerusalemu monga nsembe kwa Yehova, atakwera akavalo, magaleta ndi ngolo, ndi pa abulu ndi ngamira,” akutero Yehova. “Adzabwera nawo ngati momwe Aisraeli amabwerera ndi zopereka zachakudya ku Nyumba ya Yehova mu ziwiya zoyeretsedwa monga mwa mwambo.
Und werden alle eure Brüder aus allen Völkerschaften herbeibringen als Speiseopfer dem Jehovah auf Rossen und auf Streitwagen und auf Sänften und auf Maultieren und Dromedaren, auf den Berg Meiner Heiligkeit, gen Jerusalem, spricht Jehovah, wie die Söhne Israels in reinem Gefäß das Speiseopfer bringen in das Haus Jehovahs.
21 Ndipo ndidzasankha ena mwa iwonso kukhala ansembe ndi Alevi,” akutero Yehova.
Und Ich will auch aus denselben nehmen zu Priestern und zu Leviten, spricht Jehovah.
22 “Monga momwe mlengalenga mwatsopano ndi dziko lapansi latsopano zimene ndidzapanga zidzakhala mpaka muyaya pamaso panga, ndi chonchonso dzina lanu ndi zidzukulu zanu zidzakhalire.” Akutero Yehova.
Denn wie die neuen Himmel und die neue Erde, so Ich mache, vor Mir stehen, spricht Jehovah, so soll auch euer Same und euer Name stehen.
23 “Anthu a mitundu yonse adzabwera kudzandipembedza ku Yerusalemu, pa chikondwerero chilichonse cha pokhala pa mwezi watsopano ndi tsiku la Sabata lililonse,” akutero Yehova.
Und es wird geschehen, daß von Monat zu Monat und von Sabbath zu Sabbath alles Fleisch kommen wird, vor Mir anzubeten, spricht Jehovah.
24 “Akamachoka adzaona mitembo ya anthu amene anandiwukira Ine. Mphutsi zawo sizidzafa, kapena moto wawo sudzazimitsidwa. Anthu a mitundu ina yonse powaona adzanyansidwa nawo.”
Und sie werden hinausgehen und sehen die Leichen der Männer, die von Mir abgefallen sind; denn ihr Wurm wird nicht sterben und ihr Feuer nicht erlöschen, und sie sind zum Widerwillen allem Fleisch.

< Yesaya 66 >