< Yesaya 66 >
1 Yehova akuti, “Kumwamba ndi mpando wanga waufumu ndipo dziko lapansi ndilo chopondapo mapazi anga. Tsono nyumba ili kuti yomwe mundimangire, ndipo malo ali kuti amene inu mungandikonzere kuti ndizipumuliramo?
Voici ce que dit le Seigneur: Le ciel est mon trône, et la terre l'escabeau de mes pieds. Quelle maison me bâtirez-vous? Et quel sera le lieu où je résiderai?
2 Kodi si manja anga amene anapanga zinthu zonsezi, motero zonsezi ndi zanga?” Akutero Yehova. “Koma munthu amene ndimakondwera naye ndi uyu: amene ali wodzichepetsa ndi wosweka mtima, ndipo amamvera mawu anga.
Car ma main a tout fait, et tout est à moi, dit le Seigneur. Et sur qui jetterai-je mes regards, sinon sur l'humble et le doux, sur l'homme qui tremble à ma parole?
3 Koma aliyense amene amapereka nsembe ngʼombe yayimuna amaphanso munthu, ndipo aliyense amene amapereka mwana wankhosa, amaphanso galu. Aliyense amene amapereka nsembe chopereka cha chakudya amaperekanso magazi a nkhumba. Ndipo amene amafukiza lubani pa guwa lansembe la chikumbutso amapembedzanso fano. Popeza iwo asankha njira zawozawo, ndiponso kusangalatsidwa ndi zonyansa zawo.
L'injuste me sacrifie un bœuf, c'est comme s'il tuait un chien; un autre m'offre de la fleur de farine, c'est pour moi comme du sang de pourceau; un autre brûle de l'encens pour mémorial, c'est comme s'il blasphémait; ils ont choisi leurs voies, leur âme s'est complu en leurs abominations.
4 Inenso ndawasankhira chilango chowawa ndipo ndidzabweretsa pa iwo zimene amaziopa zija. Pakuti pamene ndinawayitana palibe amene anayankha, pamene ndinayankhula palibe amene anatchera khutu. Anachita zoyipa pamaso panga ndi kusankha kuchita zimene zimandinyansa zija.”
Et moi, je leur ferai payer leurs moqueries, et je punirai leurs péchés; car je les ai appelés, et ils ne m'ont pas obéi; j'ai parlé, et ils n'ont pas entendu; et devant moi ils ont fait le mal, et ce que je ne voulais pas, ils l'ont voulu.
5 Imvani mawu a Yehova, inu amene mumanjenjemera ndi mawu ake: “Abale anu amene amakudani, ndi kukuchotsani pakati pawo chifukwa cha dzina langa, amanena kuti, ‘Yehova alemekezeke kuti ife tione chimwemwe chanu!’ Koma ndi iwowo amene adzachite manyazi.
Écoutez ce que dit le Seigneur, vous qui tremblez à sa parole; vous avez dit: Nos frères, à ceux que vous avez en haine et en abomination; que le nom du Seigneur soit glorifié en eux, et se manifeste en leur joie; mais ils seront confondus.
6 Imvani mfuwu mu mzinda, imvani phokoso mʼNyumba ya Mulungu! Limenelo ndi liwu la Yehova, kulanga adani ake onse.
On entendra la voix de la ville, la voix du temple, la voix du Seigneur qui punira ses ennemis.
7 “Mzinda uli ngati amayi apakati amene asanayambe kumva zowawa wachira kale; asanayambe kumva ululu, wabala kale mwana wamwamuna.
Avant d'avoir été en mal d'enfant, avant que le moment des douleurs fût arrivé, elle a été délivrée, et elle a donné le jour à un fils.
8 Ndani anamvapo zinthu zoterezi? Ndani anazionapo zinthu zoterezi? Kodi dziko nʼkupangika tsiku limodzi, kapena mtundu wa anthu nʼkubadwa tsiku limodzi? Komatu Ziyoni atangoyamba kumva zowawa nthawi yomweyo anabereka ana ake.
Qui a jamais ouï pareille chose? qui a vu rien de semblable? La terre n'a-t-elle été en travail d'enfant qu'un seul jour? une nation est-elle née tout d'une fois, pour que Sion ait été en travail et ait mis au jour ses enfants?
9 Kodi Ine ndingangofikitsa amayi apakati mpaka nthawi yake yochira, koma osalola kuti abaledi mwana?” akutero Yehova. “Kodi ndingatseke mimba pa nthawi yoti abeleke?” akutero Mulungu wako.
Mais c'est moi qui ai fait naître cette attente, et tu ne t'es point souvenue de moi, dit le Seigneur. N'est-ce point moi qui rends une femme féconde ou stérile? dit ton Dieu.
10 “Kondwera nayeni Yerusalemu ndipo musangalale chifukwa cha Iye, inu nonse amene mumakonda Yerusalemu, kondwera nayeni kwambiri, nonse amene mumamulira.
Jérusalem, réjouis-toi; rassemblez-vous dans ses murs, vous tous qui l'aimez; réjouissez-vous de sa joie, vous qui vous êtes affligés sur elle:
11 Pakuti mudzagawana naye ulemerero wake ngati kuyamwa ndi kukhuta mkaka wambiri wa mʼmawere a chitonthozo chake.”
Afin que vous vous allaitiez et que vous puisiez la plénitude à la mamelle de sa consolation; afin qu'après vous être allaités, vous trouviez des délices dans le retour de sa gloire.
12 Yehova akuti, “Ndidzamupatsa mtendere ngati mtsinje wa madzi, ndiponso chuma cha anthu a mitundu ina ngati mtsinje wosefukira. Mudzakhala ngati mwana woyamwa amene amayi ake amunyamulira pambalipa, kapena kumufungata pa miyendo yake.
Car ainsi dit le Seigneur: Voilà que je détourne vers eux comme une flamme de paix, comme un torrent qui leur apportera dans ses flots la gloire des Gentils. Les enfants de mon peuple seront portés à bras; on les prendra sur les genoux pour les consoler.
13 Monga momwe amayi amasangalatsira mwana wawo, moteronso Ine ndidzakusangalatsani; ndipo mudzasangalala chifukwa cha Yerusalemu.”
Telle une mère console son enfant, et je vous consolerai, et c'est en Jérusalem que vous serez consolés.
14 Mukadzaona zimenezi mitima yanu idzakondwera. Mudzabiriwira ngati udzu. Zimenezi zidzakulimbikitsani ndi kukupatsani moyo wamphamvu. Mudzadziwa kuti ndimathandiza amene amanditumikira ndi kuti ndimakwiyira adani anga.
Et vous le verrez, et votre cœur sera réjoui, et vos os fleuriront comme l'herbe. Et la main du Seigneur sera connue de ceux qui le craignent, et elle menacera les rebelles.
15 Taonani, Yehova akubwera ngati moto, ndipo magaleta ake ali ngati kamvuluvulu; Iye adzaonetsa mkwiyo wake nadzalanga adani ake ndi malawi amoto.
Car voilà que le Seigneur viendra comme une flamme; les roues de son char seront comme un vent impétueux, apportant sa colère, sa vengeance et sa menace, dans une flamme de feu.
16 Pakuti Yehova adzalanga anthu onse ndi moto ndi lupanga, Yehova adzapha anthu ambiri.
Car toute la terre sera jugée par le feu du Seigneur, et toute chair par son glaive; une multitude d'hommes seront blessés par le Seigneur.
17 Yehova akuti, “Amene amadzipatula ndi kudziyeretsa okha kuti apite ku minda, ali ndi mtsogoleri awo, nʼkumadya nyama ya nkhumba, mbewa ndi zinthu zina zonyansa, onsewa adzafera limodzi.”
Ceux qui se sanctifient et se purifient dans les jardins, qui mangent sous leurs portiques de la chair de porc, des souris, et d'autres mets abominables, seront tous ensemble consumés par le Seigneur.
18 “Ndipo Ine, chifukwa cha zochita zawo ndi maganizo awo, ndili pafupi kubwera kudzasonkhanitsa mitundu yonse ya anthu ndi ziyankhulo zonse. Iwo adzabwera ndi kuona ulemerero wanga.
Et moi qui connais leurs œuvres et leurs pensées, je vais réunir tous les peuples et toutes les langues, et ils viendront, et ils verront ma gloire.
19 “Ndidzayika chizindikiro pakati pawo, ndipo ndidzatumiza ena mwa iwowa amene anapulumuka kuti apite kwa anthu a mitundu ina inu ku Tarisisi, ku Libiya ndi ku Ludi (akatswiri a mauta) ku Tubala ndi Grisi, ndi ku mayiko akutali a mbali mwa nyanja amene sanamvepo za mbiri yanga kapena kuona ulemerero wanga. Iwo adzalalika za ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina.
Et je laisserai sur eux un signe, et j'enverrai ceux d'entre eux qui auront été sauvés chez les Gentils à Tharsis, à Phud, à Lud, à Mosoch, à Thobel, en Grèce, et aux îles lointaines, où mon nom n'a jamais été prononcé, où l'on n'a point vu ma gloire; et ils publieront ma gloire parmi les nations.
20 Ndipo adzabwera nawo abale anu onse ngati mphatso yopereka kwa Yehova kuchokera kwa anthu a mitundu yonse. Iwo adzakwera nawo kupita ku Yerusalemu, phiri langa loyera ku Yerusalemu monga nsembe kwa Yehova, atakwera akavalo, magaleta ndi ngolo, ndi pa abulu ndi ngamira,” akutero Yehova. “Adzabwera nawo ngati momwe Aisraeli amabwerera ndi zopereka zachakudya ku Nyumba ya Yehova mu ziwiya zoyeretsedwa monga mwa mwambo.
Et ils amèneront vos frères de toutes les nations pour en faire offrande au Seigneur, avec des chevaux et des litières freinées par des mules empanachées, dans la ville sainte, dit le Seigneur; comme lorsque les fils d'Israël offraient leurs sacrifices, en chantant des psaumes, dans le temple du Seigneur.
21 Ndipo ndidzasankha ena mwa iwonso kukhala ansembe ndi Alevi,” akutero Yehova.
Et je choisirai parmi eux des prêtres et des lévites, dit le Seigneur.
22 “Monga momwe mlengalenga mwatsopano ndi dziko lapansi latsopano zimene ndidzapanga zidzakhala mpaka muyaya pamaso panga, ndi chonchonso dzina lanu ndi zidzukulu zanu zidzakhalire.” Akutero Yehova.
Car de même que le ciel nouveau et la terre nouvelle que je créerai subsisteront devant moi, dit le Seigneur, de même votre race et votre nom seront fermement établis.
23 “Anthu a mitundu yonse adzabwera kudzandipembedza ku Yerusalemu, pa chikondwerero chilichonse cha pokhala pa mwezi watsopano ndi tsiku la Sabata lililonse,” akutero Yehova.
Et ceci sera de lune en lune, de sabbat en sabbat: toute chair viendra en Jérusalem pour adorer devant moi, dit le Seigneur.
24 “Akamachoka adzaona mitembo ya anthu amene anandiwukira Ine. Mphutsi zawo sizidzafa, kapena moto wawo sudzazimitsidwa. Anthu a mitundu ina yonse powaona adzanyansidwa nawo.”
Et ils sortiront, et ils verront les membres épars de ceux qui auront péché contre moi; car le ver qui les rongera ne finira point; le feu qui les brûlera ne sera jamais éteint, et ils seront exposés à la vue de toute chair.