< Yesaya 66 >

1 Yehova akuti, “Kumwamba ndi mpando wanga waufumu ndipo dziko lapansi ndilo chopondapo mapazi anga. Tsono nyumba ili kuti yomwe mundimangire, ndipo malo ali kuti amene inu mungandikonzere kuti ndizipumuliramo?
The Lord seith these thingis, Heuene is my seete, and the erthe is the stool of my feet. Which is this hous, which ye schulen bilde to me, and which is this place of my reste?
2 Kodi si manja anga amene anapanga zinthu zonsezi, motero zonsezi ndi zanga?” Akutero Yehova. “Koma munthu amene ndimakondwera naye ndi uyu: amene ali wodzichepetsa ndi wosweka mtima, ndipo amamvera mawu anga.
Myn hond made alle these thingis, and alle these thingis ben maad, seith the Lord; but to whom schal Y biholde, no but to a pore man and contrit in spirit, and greetli dredynge my wordis?
3 Koma aliyense amene amapereka nsembe ngʼombe yayimuna amaphanso munthu, ndipo aliyense amene amapereka mwana wankhosa, amaphanso galu. Aliyense amene amapereka nsembe chopereka cha chakudya amaperekanso magazi a nkhumba. Ndipo amene amafukiza lubani pa guwa lansembe la chikumbutso amapembedzanso fano. Popeza iwo asankha njira zawozawo, ndiponso kusangalatsidwa ndi zonyansa zawo.
He that offrith an oxe, is as he that sleeth a man; he that sleeth a scheep, is as he that brayneth a dogge; he that offrith an offryng, is as he that offrith swynes blood; he that thenketh on encense, is as he that blessith an idol; thei chesiden alle thes thingis in her weies, and her soule delitide in her abhomynaciouns.
4 Inenso ndawasankhira chilango chowawa ndipo ndidzabweretsa pa iwo zimene amaziopa zija. Pakuti pamene ndinawayitana palibe amene anayankha, pamene ndinayankhula palibe amene anatchera khutu. Anachita zoyipa pamaso panga ndi kusankha kuchita zimene zimandinyansa zija.”
Wherfor and Y schal chese the scornyngis of hem, and Y schal brynge to hem tho thingis whiche thei dredden; for Y clepide, and noon was that answeride; Y spak, and thei herden not; and thei diden yuel bifor myn iyen, and chesiden tho thingis whiche Y nolde.
5 Imvani mawu a Yehova, inu amene mumanjenjemera ndi mawu ake: “Abale anu amene amakudani, ndi kukuchotsani pakati pawo chifukwa cha dzina langa, amanena kuti, ‘Yehova alemekezeke kuti ife tione chimwemwe chanu!’ Koma ndi iwowo amene adzachite manyazi.
Here ye the word of the Lord, whiche quaken at his word; youre britheren hatynge you, and castynge a wey for my name, seiden, The Lord be glorified, and we schulen se in youre gladnesse; forsothe thei schulen be schent.
6 Imvani mfuwu mu mzinda, imvani phokoso mʼNyumba ya Mulungu! Limenelo ndi liwu la Yehova, kulanga adani ake onse.
The vois of the puple fro the citee, the vois fro the temple, the vois of the Lord yeldynge a reward to hise enemyes.
7 “Mzinda uli ngati amayi apakati amene asanayambe kumva zowawa wachira kale; asanayambe kumva ululu, wabala kale mwana wamwamuna.
Bifor that sche trauelide of child, sche childide; bifor that the sorewe of hir child beryng cam, sche childide a sone.
8 Ndani anamvapo zinthu zoterezi? Ndani anazionapo zinthu zoterezi? Kodi dziko nʼkupangika tsiku limodzi, kapena mtundu wa anthu nʼkubadwa tsiku limodzi? Komatu Ziyoni atangoyamba kumva zowawa nthawi yomweyo anabereka ana ake.
Who herde euere suche a thing, and who siy a thing lijk this? Whether the erthe schal trauele of child in o dai, ether whether a folk schal be childide togidere? For whi Sion trauelede of child, and childide hir sones.
9 Kodi Ine ndingangofikitsa amayi apakati mpaka nthawi yake yochira, koma osalola kuti abaledi mwana?” akutero Yehova. “Kodi ndingatseke mimba pa nthawi yoti abeleke?” akutero Mulungu wako.
Whether that Y `my silf that make othere to bere child, schal not ber child? seith the Lord. Whether Y that yyue generacioun to othere men, schal be bareyn? seith thi Lord God.
10 “Kondwera nayeni Yerusalemu ndipo musangalale chifukwa cha Iye, inu nonse amene mumakonda Yerusalemu, kondwera nayeni kwambiri, nonse amene mumamulira.
Be ye glad with Jerusalem, and alle ye that louen that, make ful out ioye ther ynne; alle ye that mourenen on that Jerusalem, make ye ioye with it in ioie;
11 Pakuti mudzagawana naye ulemerero wake ngati kuyamwa ndi kukhuta mkaka wambiri wa mʼmawere a chitonthozo chake.”
that bothe ye souke, and be fillid of the tetis and coumfort therof, that ye mylke, and flowe in delicis, of al maner glorie therof.
12 Yehova akuti, “Ndidzamupatsa mtendere ngati mtsinje wa madzi, ndiponso chuma cha anthu a mitundu ina ngati mtsinje wosefukira. Mudzakhala ngati mwana woyamwa amene amayi ake amunyamulira pambalipa, kapena kumufungata pa miyendo yake.
For whi the Lord seith these thingis, Lo! Y schal bowe doun on it, as a flood of pees, and as a flowynge streem the glorie of hethene men, which ye schulen souke; ye schulen be borun at tetis, and on knees thei schulen speke plesauntly to you.
13 Monga momwe amayi amasangalatsira mwana wawo, moteronso Ine ndidzakusangalatsani; ndipo mudzasangalala chifukwa cha Yerusalemu.”
As if a modir spekith faire to ony child, so Y schal coumforte you, and ye schulen be coumfortid in Jerusalem.
14 Mukadzaona zimenezi mitima yanu idzakondwera. Mudzabiriwira ngati udzu. Zimenezi zidzakulimbikitsani ndi kukupatsani moyo wamphamvu. Mudzadziwa kuti ndimathandiza amene amanditumikira ndi kuti ndimakwiyira adani anga.
Ye schulen se, and youre herte schal haue ioie, and youre boonys schulen buriowne as an erbe. And the hond of the Lord schal be knowun in hise seruauntis, and he schal haue indignacioun to hise enemyes.
15 Taonani, Yehova akubwera ngati moto, ndipo magaleta ake ali ngati kamvuluvulu; Iye adzaonetsa mkwiyo wake nadzalanga adani ake ndi malawi amoto.
For lo! the Lord schal come in fier, and as a whirlwynd hise charis, to yelde in indignacioun hise strong veniaunce, and his blamyng in the flawme of fier.
16 Pakuti Yehova adzalanga anthu onse ndi moto ndi lupanga, Yehova adzapha anthu ambiri.
For whi the Lord schal deme in fier, and in hys swerd to ech fleisch; and slayn men of the Lord schulen be multiplied,
17 Yehova akuti, “Amene amadzipatula ndi kudziyeretsa okha kuti apite ku minda, ali ndi mtsogoleri awo, nʼkumadya nyama ya nkhumba, mbewa ndi zinthu zina zonyansa, onsewa adzafera limodzi.”
that weren halewid, and gessiden hem cleene, in gardyns aftir o yate with ynne; that eten swynes fleisch, and abhomynacioun, and a mows, thei schulen be waastid togidere, seith the Lord.
18 “Ndipo Ine, chifukwa cha zochita zawo ndi maganizo awo, ndili pafupi kubwera kudzasonkhanitsa mitundu yonse ya anthu ndi ziyankhulo zonse. Iwo adzabwera ndi kuona ulemerero wanga.
Forsothe Y come to gadere togidere the werkis of hem, and the thouytis of hem, with alle folkis and langagis; and thei schulen come, and schulen se my glorie.
19 “Ndidzayika chizindikiro pakati pawo, ndipo ndidzatumiza ena mwa iwowa amene anapulumuka kuti apite kwa anthu a mitundu ina inu ku Tarisisi, ku Libiya ndi ku Ludi (akatswiri a mauta) ku Tubala ndi Grisi, ndi ku mayiko akutali a mbali mwa nyanja amene sanamvepo za mbiri yanga kapena kuona ulemerero wanga. Iwo adzalalika za ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina.
And Y schal sette a signe in hem, and Y schal sende of hem that ben sauyd to hethene men, in to the see, in to Affrik, and in to Liddia, and to hem that holden arowe, in to Italie, and Greek lond, to ilis fer, to hem that herden not of me, and sien not my glorie. And thei schulen telle my glorie to hethene men,
20 Ndipo adzabwera nawo abale anu onse ngati mphatso yopereka kwa Yehova kuchokera kwa anthu a mitundu yonse. Iwo adzakwera nawo kupita ku Yerusalemu, phiri langa loyera ku Yerusalemu monga nsembe kwa Yehova, atakwera akavalo, magaleta ndi ngolo, ndi pa abulu ndi ngamira,” akutero Yehova. “Adzabwera nawo ngati momwe Aisraeli amabwerera ndi zopereka zachakudya ku Nyumba ya Yehova mu ziwiya zoyeretsedwa monga mwa mwambo.
and thei schulen brynge alle youre britheren of alle folkis a yifte to the Lord, in horsis, and charis, and in literis, and in mulis, and in cartis, to myn hooli hil, Jerusalem, seith the Lord; as if the sones of Israel bryngen a yifte in a cleene vessel in to the hous of the Lord.
21 Ndipo ndidzasankha ena mwa iwonso kukhala ansembe ndi Alevi,” akutero Yehova.
And Y schal take of hem in to preestis and dekenes, seith the Lord.
22 “Monga momwe mlengalenga mwatsopano ndi dziko lapansi latsopano zimene ndidzapanga zidzakhala mpaka muyaya pamaso panga, ndi chonchonso dzina lanu ndi zidzukulu zanu zidzakhalire.” Akutero Yehova.
For as newe heuenes and newe erthe, whiche Y make to stonde bifore me, seith the Lord, so youre seed schal stonde, and youre name.
23 “Anthu a mitundu yonse adzabwera kudzandipembedza ku Yerusalemu, pa chikondwerero chilichonse cha pokhala pa mwezi watsopano ndi tsiku la Sabata lililonse,” akutero Yehova.
And a monethe schal be of monethe, and a sabat of sabat; ech man schal come for to worschipe bifore my face, seith the Lord.
24 “Akamachoka adzaona mitembo ya anthu amene anandiwukira Ine. Mphutsi zawo sizidzafa, kapena moto wawo sudzazimitsidwa. Anthu a mitundu ina yonse powaona adzanyansidwa nawo.”
And thei schulen go out, and schulen se the careyns of men, that trespassiden ayens me; the worm of hem schal not die, and the fier of hem schal not be quenchid; and thei schulen be `til to fillyng of siyt to ech man.

< Yesaya 66 >