< Yesaya 66 >

1 Yehova akuti, “Kumwamba ndi mpando wanga waufumu ndipo dziko lapansi ndilo chopondapo mapazi anga. Tsono nyumba ili kuti yomwe mundimangire, ndipo malo ali kuti amene inu mungandikonzere kuti ndizipumuliramo?
Thus saith Jehovah: Heaven is my throne, And the earth my footstool; Where is the house that ye can build me, And where is the place of my rest?
2 Kodi si manja anga amene anapanga zinthu zonsezi, motero zonsezi ndi zanga?” Akutero Yehova. “Koma munthu amene ndimakondwera naye ndi uyu: amene ali wodzichepetsa ndi wosweka mtima, ndipo amamvera mawu anga.
For all these things hath my hand made; By it do all these things exist, saith Jehovah. But to this man will I look, Even to him who is humble and of a contrite spirit, And who trembleth at my word.
3 Koma aliyense amene amapereka nsembe ngʼombe yayimuna amaphanso munthu, ndipo aliyense amene amapereka mwana wankhosa, amaphanso galu. Aliyense amene amapereka nsembe chopereka cha chakudya amaperekanso magazi a nkhumba. Ndipo amene amafukiza lubani pa guwa lansembe la chikumbutso amapembedzanso fano. Popeza iwo asankha njira zawozawo, ndiponso kusangalatsidwa ndi zonyansa zawo.
He that slayeth an ox killeth a man; He that sacrificeth a lamb beheadeth a dog; He that maketh an oblation offereth swine's blood; He that burneth incense blesseth an idol. Yea, they have chosen their own ways, And in their abominations their souls delight.
4 Inenso ndawasankhira chilango chowawa ndipo ndidzabweretsa pa iwo zimene amaziopa zija. Pakuti pamene ndinawayitana palibe amene anayankha, pamene ndinayankhula palibe amene anatchera khutu. Anachita zoyipa pamaso panga ndi kusankha kuchita zimene zimandinyansa zija.”
I also will choose their calamities; What they dread I will bring upon them; Because I called, and no one answered, I spake, and they did not hear; But they did what is evil in my sight, And chose that in which I have no delight.
5 Imvani mawu a Yehova, inu amene mumanjenjemera ndi mawu ake: “Abale anu amene amakudani, ndi kukuchotsani pakati pawo chifukwa cha dzina langa, amanena kuti, ‘Yehova alemekezeke kuti ife tione chimwemwe chanu!’ Koma ndi iwowo amene adzachite manyazi.
Hear the word of Jehovah, Ye that tremble at his word! “Your brethren that hate you, And thrust you out for my name's sake, have said, “May Jehovah be glorified, that we may see your joy!” But they shall be confounded.
6 Imvani mfuwu mu mzinda, imvani phokoso mʼNyumba ya Mulungu! Limenelo ndi liwu la Yehova, kulanga adani ake onse.
A voice of tumult from the city! A voice from the temple! The voice of Jehovah, rendering recompense to his enemies!
7 “Mzinda uli ngati amayi apakati amene asanayambe kumva zowawa wachira kale; asanayambe kumva ululu, wabala kale mwana wamwamuna.
Before she was in travail, she brought forth, Before her pangs came, she was delivered of a son.
8 Ndani anamvapo zinthu zoterezi? Ndani anazionapo zinthu zoterezi? Kodi dziko nʼkupangika tsiku limodzi, kapena mtundu wa anthu nʼkubadwa tsiku limodzi? Komatu Ziyoni atangoyamba kumva zowawa nthawi yomweyo anabereka ana ake.
Who hath heard such a thing? Who hath seen such things? Is a country brought forth in a day? Is a nation born at once? For as soon as Zion was in travail, she brought forth her children.
9 Kodi Ine ndingangofikitsa amayi apakati mpaka nthawi yake yochira, koma osalola kuti abaledi mwana?” akutero Yehova. “Kodi ndingatseke mimba pa nthawi yoti abeleke?” akutero Mulungu wako.
Shall I bring to the birth, and not cause to bring forth, saith Jehovah; Shall I, who beget, restrain the birth? saith thy God.
10 “Kondwera nayeni Yerusalemu ndipo musangalale chifukwa cha Iye, inu nonse amene mumakonda Yerusalemu, kondwera nayeni kwambiri, nonse amene mumamulira.
Rejoice ye with Jerusalem, And exult for her, all ye that love her! Be very joyful with her, all ye that mourn for her!
11 Pakuti mudzagawana naye ulemerero wake ngati kuyamwa ndi kukhuta mkaka wambiri wa mʼmawere a chitonthozo chake.”
That ye may suck, and be satisfied, from the breast of her consolations, That ye may suck and be delighted with the fulness of her glory.
12 Yehova akuti, “Ndidzamupatsa mtendere ngati mtsinje wa madzi, ndiponso chuma cha anthu a mitundu ina ngati mtsinje wosefukira. Mudzakhala ngati mwana woyamwa amene amayi ake amunyamulira pambalipa, kapena kumufungata pa miyendo yake.
For thus saith Jehovah: Behold, I will bring prosperity to her like a river, And the wealth of the nations like an overflowing stream; Ye shall suck at the breast, Ye shall be carried on the arm, And on the knees shall ye be dandled.
13 Monga momwe amayi amasangalatsira mwana wawo, moteronso Ine ndidzakusangalatsani; ndipo mudzasangalala chifukwa cha Yerusalemu.”
As one whom his mother comforteth, So will I comfort you; And in Jerusalem shall ye be comforted.
14 Mukadzaona zimenezi mitima yanu idzakondwera. Mudzabiriwira ngati udzu. Zimenezi zidzakulimbikitsani ndi kukupatsani moyo wamphamvu. Mudzadziwa kuti ndimathandiza amene amanditumikira ndi kuti ndimakwiyira adani anga.
Ye shall see, and your heart shall rejoice, And your bones shall flourish like a green plant, And the hand of Jehovah shall be manifested to his servants, And be moved with indignation against his enemies.
15 Taonani, Yehova akubwera ngati moto, ndipo magaleta ake ali ngati kamvuluvulu; Iye adzaonetsa mkwiyo wake nadzalanga adani ake ndi malawi amoto.
For behold, Jehovah cometh with fire, Like a whirlwind are his chariots, To breathe forth his anger in a glowing heat, And his rebuke in flames of fire.
16 Pakuti Yehova adzalanga anthu onse ndi moto ndi lupanga, Yehova adzapha anthu ambiri.
For with fire will Jehovah contend, And with his sword, with all flesh, And many shall be the slain of Jehovah.
17 Yehova akuti, “Amene amadzipatula ndi kudziyeretsa okha kuti apite ku minda, ali ndi mtsogoleri awo, nʼkumadya nyama ya nkhumba, mbewa ndi zinthu zina zonyansa, onsewa adzafera limodzi.”
They who sanctify and purify themselves in the groves, Following one in the midst, Who eat swine's flesh, and the abomination, and the mouse. They shall all perish together, saith Jehovah.
18 “Ndipo Ine, chifukwa cha zochita zawo ndi maganizo awo, ndili pafupi kubwera kudzasonkhanitsa mitundu yonse ya anthu ndi ziyankhulo zonse. Iwo adzabwera ndi kuona ulemerero wanga.
For I know their works, and their thoughts; The time cometh to gather all nations and tongues together; They shall come, and behold my glory.
19 “Ndidzayika chizindikiro pakati pawo, ndipo ndidzatumiza ena mwa iwowa amene anapulumuka kuti apite kwa anthu a mitundu ina inu ku Tarisisi, ku Libiya ndi ku Ludi (akatswiri a mauta) ku Tubala ndi Grisi, ndi ku mayiko akutali a mbali mwa nyanja amene sanamvepo za mbiri yanga kapena kuona ulemerero wanga. Iwo adzalalika za ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina.
And I will give a sign among them, And of those that escape I will send to the nations, To Tarshish, Phul, and Lud, who draw the bow, to Tubal and Javan, To the distant coasts, who never heard my name, And who never saw my glory; And they shall declare my glory among the nations.
20 Ndipo adzabwera nawo abale anu onse ngati mphatso yopereka kwa Yehova kuchokera kwa anthu a mitundu yonse. Iwo adzakwera nawo kupita ku Yerusalemu, phiri langa loyera ku Yerusalemu monga nsembe kwa Yehova, atakwera akavalo, magaleta ndi ngolo, ndi pa abulu ndi ngamira,” akutero Yehova. “Adzabwera nawo ngati momwe Aisraeli amabwerera ndi zopereka zachakudya ku Nyumba ya Yehova mu ziwiya zoyeretsedwa monga mwa mwambo.
And they shall bring all your brethren From all the nations, an offering to Jehovah, Upon horses, and in chariots, and in litters, and upon mules and dromedaries, To my holy mountain, Jerusalem, saith Jehovah, As the sons of Israel bring their gifts In pure vessels to the house of Jehovah.
21 Ndipo ndidzasankha ena mwa iwonso kukhala ansembe ndi Alevi,” akutero Yehova.
And of them will I also take For priests and for Levites, saith Jehovah.
22 “Monga momwe mlengalenga mwatsopano ndi dziko lapansi latsopano zimene ndidzapanga zidzakhala mpaka muyaya pamaso panga, ndi chonchonso dzina lanu ndi zidzukulu zanu zidzakhalire.” Akutero Yehova.
For as the new heavens, And the new earth, which I make, Endure before me, saith Jehovah, So shall your race and your name endure.
23 “Anthu a mitundu yonse adzabwera kudzandipembedza ku Yerusalemu, pa chikondwerero chilichonse cha pokhala pa mwezi watsopano ndi tsiku la Sabata lililonse,” akutero Yehova.
And it shall be, from new moon to new moon, And from sabbath to sabbath, That all flesh shall come and worship before me, saith Jehovah.
24 “Akamachoka adzaona mitembo ya anthu amene anandiwukira Ine. Mphutsi zawo sizidzafa, kapena moto wawo sudzazimitsidwa. Anthu a mitundu ina yonse powaona adzanyansidwa nawo.”
Then shall they go forth and see The dead bodies of the men that rebelled against me! For their worm shall not die, And their fire shall not be quenched, And they shall be an abhorrence to all flesh.

< Yesaya 66 >