< Yesaya 66 >
1 Yehova akuti, “Kumwamba ndi mpando wanga waufumu ndipo dziko lapansi ndilo chopondapo mapazi anga. Tsono nyumba ili kuti yomwe mundimangire, ndipo malo ali kuti amene inu mungandikonzere kuti ndizipumuliramo?
Thus saith the Lord: Heaven is my throne, and the earth my footstool: what is this house that you will build to me? and what is this place of my rest?
2 Kodi si manja anga amene anapanga zinthu zonsezi, motero zonsezi ndi zanga?” Akutero Yehova. “Koma munthu amene ndimakondwera naye ndi uyu: amene ali wodzichepetsa ndi wosweka mtima, ndipo amamvera mawu anga.
My hand made all these things, and all these things were made, saith the Lord. But to whom shall I have respect, but to him that is poor and little, and of a contrite spirit, and that trembleth at my words?
3 Koma aliyense amene amapereka nsembe ngʼombe yayimuna amaphanso munthu, ndipo aliyense amene amapereka mwana wankhosa, amaphanso galu. Aliyense amene amapereka nsembe chopereka cha chakudya amaperekanso magazi a nkhumba. Ndipo amene amafukiza lubani pa guwa lansembe la chikumbutso amapembedzanso fano. Popeza iwo asankha njira zawozawo, ndiponso kusangalatsidwa ndi zonyansa zawo.
He that sacrificeth an ox, is as if he slew a man: he that killeth a sheep in sacrifice, as if he should brain a dog: he that offereth an oblation, as if he should offer swine’s blood; he that remembereth incense, as if he should bless an idol. All these things have they chosen in their ways, and their soul is delighted in their abominations.
4 Inenso ndawasankhira chilango chowawa ndipo ndidzabweretsa pa iwo zimene amaziopa zija. Pakuti pamene ndinawayitana palibe amene anayankha, pamene ndinayankhula palibe amene anatchera khutu. Anachita zoyipa pamaso panga ndi kusankha kuchita zimene zimandinyansa zija.”
Wherefore I also will choose their mockeries, and will bring upon them the things they feared: because I called, and there was none that would answer; I have spoken, and they heard not; and they have done evil in my eyes, and have chosen the things that displease me.
5 Imvani mawu a Yehova, inu amene mumanjenjemera ndi mawu ake: “Abale anu amene amakudani, ndi kukuchotsani pakati pawo chifukwa cha dzina langa, amanena kuti, ‘Yehova alemekezeke kuti ife tione chimwemwe chanu!’ Koma ndi iwowo amene adzachite manyazi.
Hear the word of the Lord, you that tremble at his word: Your brethren that hate you, and cast you out for my name’s sake, have said: Let the Lord be glorified, and we shall see in your joy: but they shall be confounded.
6 Imvani mfuwu mu mzinda, imvani phokoso mʼNyumba ya Mulungu! Limenelo ndi liwu la Yehova, kulanga adani ake onse.
A voice of the people from the city, a voice from the temple, the voice of the Lord that rendereth recompense to his enemies.
7 “Mzinda uli ngati amayi apakati amene asanayambe kumva zowawa wachira kale; asanayambe kumva ululu, wabala kale mwana wamwamuna.
Before she was in labour, she brought forth; before her time came to be delivered, she brought forth a man child.
8 Ndani anamvapo zinthu zoterezi? Ndani anazionapo zinthu zoterezi? Kodi dziko nʼkupangika tsiku limodzi, kapena mtundu wa anthu nʼkubadwa tsiku limodzi? Komatu Ziyoni atangoyamba kumva zowawa nthawi yomweyo anabereka ana ake.
Who hath ever heard such a thing? and who hath seen the like to this? shall the earth bring forth in one day? or shall a nation be brought forth at once, because Sion hath been in labour, and hath brought forth her children?
9 Kodi Ine ndingangofikitsa amayi apakati mpaka nthawi yake yochira, koma osalola kuti abaledi mwana?” akutero Yehova. “Kodi ndingatseke mimba pa nthawi yoti abeleke?” akutero Mulungu wako.
Shall not I that make others to bring forth children, myself bring forth, saith the Lord? shall I, that give generation to others, be barren, saith the Lord thy God?
10 “Kondwera nayeni Yerusalemu ndipo musangalale chifukwa cha Iye, inu nonse amene mumakonda Yerusalemu, kondwera nayeni kwambiri, nonse amene mumamulira.
Rejoice with Jerusalem, and be glad with her, all you that love her: rejoice for joy with her, all you that mourn for her.
11 Pakuti mudzagawana naye ulemerero wake ngati kuyamwa ndi kukhuta mkaka wambiri wa mʼmawere a chitonthozo chake.”
That you may suck, and be filled with the breasts of her consolations: that you may milk out, and flow with delights, from the abundance of her glory.
12 Yehova akuti, “Ndidzamupatsa mtendere ngati mtsinje wa madzi, ndiponso chuma cha anthu a mitundu ina ngati mtsinje wosefukira. Mudzakhala ngati mwana woyamwa amene amayi ake amunyamulira pambalipa, kapena kumufungata pa miyendo yake.
For thus saith the Lord: Behold I will bring upon her as it were a river of peace, and as an overflowing torrent the glory of the Gentiles, which you shall suck; you shall be carried at the breasts, and upon the knees they shall caress you.
13 Monga momwe amayi amasangalatsira mwana wawo, moteronso Ine ndidzakusangalatsani; ndipo mudzasangalala chifukwa cha Yerusalemu.”
As one whom the mother caresseth, so will I comfort you, and you shall be comforted in Jerusalem.
14 Mukadzaona zimenezi mitima yanu idzakondwera. Mudzabiriwira ngati udzu. Zimenezi zidzakulimbikitsani ndi kukupatsani moyo wamphamvu. Mudzadziwa kuti ndimathandiza amene amanditumikira ndi kuti ndimakwiyira adani anga.
You shall see and your heart shall rejoice, and your bones shall flourish like an herb, and the hand of the Lord shall be known to his servants, and he shall be angry with his enemies.
15 Taonani, Yehova akubwera ngati moto, ndipo magaleta ake ali ngati kamvuluvulu; Iye adzaonetsa mkwiyo wake nadzalanga adani ake ndi malawi amoto.
For behold the Lord will come with fire, and his chariots are like a whirlwind, to render his wrath in indignation, and his rebuke with flames of fire.
16 Pakuti Yehova adzalanga anthu onse ndi moto ndi lupanga, Yehova adzapha anthu ambiri.
For the Lord shall judge by fire, and by his sword unto all flesh, and the slain of the Lord shall be many.
17 Yehova akuti, “Amene amadzipatula ndi kudziyeretsa okha kuti apite ku minda, ali ndi mtsogoleri awo, nʼkumadya nyama ya nkhumba, mbewa ndi zinthu zina zonyansa, onsewa adzafera limodzi.”
They that were sanctified, and thought themselves clean in the gardens behind the gate within, they that did eat swine’s flesh, and the abomination, and the mouse: they shall be consumed together, saith the Lord.
18 “Ndipo Ine, chifukwa cha zochita zawo ndi maganizo awo, ndili pafupi kubwera kudzasonkhanitsa mitundu yonse ya anthu ndi ziyankhulo zonse. Iwo adzabwera ndi kuona ulemerero wanga.
But I know their works, and their thoughts: I come that I may gather them together with all nations and tongues: and they shall come and shall see my glory.
19 “Ndidzayika chizindikiro pakati pawo, ndipo ndidzatumiza ena mwa iwowa amene anapulumuka kuti apite kwa anthu a mitundu ina inu ku Tarisisi, ku Libiya ndi ku Ludi (akatswiri a mauta) ku Tubala ndi Grisi, ndi ku mayiko akutali a mbali mwa nyanja amene sanamvepo za mbiri yanga kapena kuona ulemerero wanga. Iwo adzalalika za ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina.
And I will set a sign among them, and I will send of them that shall be saved, to the Gentiles into the sea, into Africa, and Lydia them that draw the bow: into Italy, and Greece, to the islands afar off, to them that have not heard of me, and have not seen my glory. And they shall declare my glory to the Gentiles:
20 Ndipo adzabwera nawo abale anu onse ngati mphatso yopereka kwa Yehova kuchokera kwa anthu a mitundu yonse. Iwo adzakwera nawo kupita ku Yerusalemu, phiri langa loyera ku Yerusalemu monga nsembe kwa Yehova, atakwera akavalo, magaleta ndi ngolo, ndi pa abulu ndi ngamira,” akutero Yehova. “Adzabwera nawo ngati momwe Aisraeli amabwerera ndi zopereka zachakudya ku Nyumba ya Yehova mu ziwiya zoyeretsedwa monga mwa mwambo.
And they shall bring all your brethren out of all nations for a gift to the Lord, upon horses, and in chariots, and in litters, and on mules, and in coaches, to my holy mountain Jerusalem, saith the Lord, as if the children of Israel should bring an offering in a clean vessel into the house of the Lord.
21 Ndipo ndidzasankha ena mwa iwonso kukhala ansembe ndi Alevi,” akutero Yehova.
And I will take of them to be priests, and Levites, saith the Lord.
22 “Monga momwe mlengalenga mwatsopano ndi dziko lapansi latsopano zimene ndidzapanga zidzakhala mpaka muyaya pamaso panga, ndi chonchonso dzina lanu ndi zidzukulu zanu zidzakhalire.” Akutero Yehova.
For as the new heavens, and the new earth, which I will make to stand before me, saith the Lord: so shall your seed stand, and your name.
23 “Anthu a mitundu yonse adzabwera kudzandipembedza ku Yerusalemu, pa chikondwerero chilichonse cha pokhala pa mwezi watsopano ndi tsiku la Sabata lililonse,” akutero Yehova.
And there shall be month after month, and sabbath after sabbath: and all flesh shall come to adore before my face, saith the Lord.
24 “Akamachoka adzaona mitembo ya anthu amene anandiwukira Ine. Mphutsi zawo sizidzafa, kapena moto wawo sudzazimitsidwa. Anthu a mitundu ina yonse powaona adzanyansidwa nawo.”
And they shall go out, and see the carcasses of the men that have transgressed against me: their worm shall not die, and their fire shall not be quenched: and they shall be a loathsome sight to all flesh.