< Yesaya 66 >

1 Yehova akuti, “Kumwamba ndi mpando wanga waufumu ndipo dziko lapansi ndilo chopondapo mapazi anga. Tsono nyumba ili kuti yomwe mundimangire, ndipo malo ali kuti amene inu mungandikonzere kuti ndizipumuliramo?
Thus says the Lord: Heaven is my throne, and the earth is my footstool. What is this house that you would build for me? And what is this place of my rest?
2 Kodi si manja anga amene anapanga zinthu zonsezi, motero zonsezi ndi zanga?” Akutero Yehova. “Koma munthu amene ndimakondwera naye ndi uyu: amene ali wodzichepetsa ndi wosweka mtima, ndipo amamvera mawu anga.
My hand has made all these things, and all these things have been made, says the Lord. But upon whom will I look with favor, except upon a poor little one, who is contrite in spirit, and who trembles at my words?
3 Koma aliyense amene amapereka nsembe ngʼombe yayimuna amaphanso munthu, ndipo aliyense amene amapereka mwana wankhosa, amaphanso galu. Aliyense amene amapereka nsembe chopereka cha chakudya amaperekanso magazi a nkhumba. Ndipo amene amafukiza lubani pa guwa lansembe la chikumbutso amapembedzanso fano. Popeza iwo asankha njira zawozawo, ndiponso kusangalatsidwa ndi zonyansa zawo.
Whoever immolates an ox, it is as if he slaughters a man. Whoever sacrifices a sheep, it is as if he is smashing the head of a dog. Whoever offers an oblation, it is as if he is offering swine’s blood. Whoever makes remembrance with incense, it is as if he is blessing an idol. All these things, they have chosen according to their own ways, and their soul has taken delight in their own abominations.
4 Inenso ndawasankhira chilango chowawa ndipo ndidzabweretsa pa iwo zimene amaziopa zija. Pakuti pamene ndinawayitana palibe amene anayankha, pamene ndinayankhula palibe amene anatchera khutu. Anachita zoyipa pamaso panga ndi kusankha kuchita zimene zimandinyansa zija.”
Therefore, I also will choose their illusions, and I will lead over them the things that they feared. For I called, and there was no one who would respond. I have spoken, and they have not listened. And they have done evil in my eyes; and what I did not will, they have chosen.
5 Imvani mawu a Yehova, inu amene mumanjenjemera ndi mawu ake: “Abale anu amene amakudani, ndi kukuchotsani pakati pawo chifukwa cha dzina langa, amanena kuti, ‘Yehova alemekezeke kuti ife tione chimwemwe chanu!’ Koma ndi iwowo amene adzachite manyazi.
Listen to the word of the Lord, you who tremble at his word. Your brothers, who hate you and who cast you out because of my name, have said: “Let the Lord be glorified, and we will see by your rejoicing.” But they themselves will be confounded.
6 Imvani mfuwu mu mzinda, imvani phokoso mʼNyumba ya Mulungu! Limenelo ndi liwu la Yehova, kulanga adani ake onse.
A voice of the people from the city! A voice from the temple! The voice of the Lord repaying retribution to his enemies!
7 “Mzinda uli ngati amayi apakati amene asanayambe kumva zowawa wachira kale; asanayambe kumva ululu, wabala kale mwana wamwamuna.
Before she was in labor, she gave birth. Before her time arrived for delivery, she gave birth to a male child.
8 Ndani anamvapo zinthu zoterezi? Ndani anazionapo zinthu zoterezi? Kodi dziko nʼkupangika tsiku limodzi, kapena mtundu wa anthu nʼkubadwa tsiku limodzi? Komatu Ziyoni atangoyamba kumva zowawa nthawi yomweyo anabereka ana ake.
Who has ever heard of such a thing? And who has seen anything like this? Will the earth give birth in one day? Or will a nation be born all at once? For Zion has been in labor, and she has given birth to her sons.
9 Kodi Ine ndingangofikitsa amayi apakati mpaka nthawi yake yochira, koma osalola kuti abaledi mwana?” akutero Yehova. “Kodi ndingatseke mimba pa nthawi yoti abeleke?” akutero Mulungu wako.
Will I, who causes others to give birth, not also give birth myself, says the Lord? Will I, who bestows generation upon others, be barren myself, says the Lord your God?
10 “Kondwera nayeni Yerusalemu ndipo musangalale chifukwa cha Iye, inu nonse amene mumakonda Yerusalemu, kondwera nayeni kwambiri, nonse amene mumamulira.
Rejoice with Jerusalem, and exult in her, all you who love her! Rejoice greatly with her, all you who mourn over her!
11 Pakuti mudzagawana naye ulemerero wake ngati kuyamwa ndi kukhuta mkaka wambiri wa mʼmawere a chitonthozo chake.”
So may you nurse and be filled, from the breasts of her consolations. So may you receive milk and overflow with delights, from every portion of her glory.
12 Yehova akuti, “Ndidzamupatsa mtendere ngati mtsinje wa madzi, ndiponso chuma cha anthu a mitundu ina ngati mtsinje wosefukira. Mudzakhala ngati mwana woyamwa amene amayi ake amunyamulira pambalipa, kapena kumufungata pa miyendo yake.
For thus says the Lord: Behold, I will turn a river of peace toward her, with an inundating torrent: the glory of the Gentiles, from which you will nurse. You will be carried at the breasts, and they will caress you upon the knees.
13 Monga momwe amayi amasangalatsira mwana wawo, moteronso Ine ndidzakusangalatsani; ndipo mudzasangalala chifukwa cha Yerusalemu.”
In the manner of one whom a mother caresses, so will I console you. And you will be consoled in Jerusalem.
14 Mukadzaona zimenezi mitima yanu idzakondwera. Mudzabiriwira ngati udzu. Zimenezi zidzakulimbikitsani ndi kukupatsani moyo wamphamvu. Mudzadziwa kuti ndimathandiza amene amanditumikira ndi kuti ndimakwiyira adani anga.
You will see, and your heart will be glad, and your bones will flourish like a plant, and the hand of the Lord will be known to his servants, and he will be angry with his enemies.
15 Taonani, Yehova akubwera ngati moto, ndipo magaleta ake ali ngati kamvuluvulu; Iye adzaonetsa mkwiyo wake nadzalanga adani ake ndi malawi amoto.
For behold, the Lord will arrive with fire, and his four-horse chariots will be like a whirlwind: to render his wrath with indignation, and his rebuke with flames of fire.
16 Pakuti Yehova adzalanga anthu onse ndi moto ndi lupanga, Yehova adzapha anthu ambiri.
For the Lord will divide with fire, and with his sword among all flesh, and those slain by the Lord will be many.
17 Yehova akuti, “Amene amadzipatula ndi kudziyeretsa okha kuti apite ku minda, ali ndi mtsogoleri awo, nʼkumadya nyama ya nkhumba, mbewa ndi zinthu zina zonyansa, onsewa adzafera limodzi.”
Those who were sanctified, who thought themselves to be clean in the gardens behind the inner gate, who were eating swine’s flesh, and the abomination, and the mouse: they will be consumed all at once, says the Lord.
18 “Ndipo Ine, chifukwa cha zochita zawo ndi maganizo awo, ndili pafupi kubwera kudzasonkhanitsa mitundu yonse ya anthu ndi ziyankhulo zonse. Iwo adzabwera ndi kuona ulemerero wanga.
But I know their works and their thoughts. I am arriving, so that I may gather them together with all nations and languages. And they will approach, and they will see my glory.
19 “Ndidzayika chizindikiro pakati pawo, ndipo ndidzatumiza ena mwa iwowa amene anapulumuka kuti apite kwa anthu a mitundu ina inu ku Tarisisi, ku Libiya ndi ku Ludi (akatswiri a mauta) ku Tubala ndi Grisi, ndi ku mayiko akutali a mbali mwa nyanja amene sanamvepo za mbiri yanga kapena kuona ulemerero wanga. Iwo adzalalika za ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina.
And I will set a sign among them. And I will send some of those who will have been saved to the Gentiles in the sea, to Africa, and to those who draw the bow in Lydia, to Italy and Greece, to islands far away, to those who have not heard of me, and to those who have not seen my glory. And they will announce my glory to the Gentiles.
20 Ndipo adzabwera nawo abale anu onse ngati mphatso yopereka kwa Yehova kuchokera kwa anthu a mitundu yonse. Iwo adzakwera nawo kupita ku Yerusalemu, phiri langa loyera ku Yerusalemu monga nsembe kwa Yehova, atakwera akavalo, magaleta ndi ngolo, ndi pa abulu ndi ngamira,” akutero Yehova. “Adzabwera nawo ngati momwe Aisraeli amabwerera ndi zopereka zachakudya ku Nyumba ya Yehova mu ziwiya zoyeretsedwa monga mwa mwambo.
And they will lead all of your brothers from all of the Gentiles as a gift to the Lord, on horses, and in four-horse chariots, and on stretchers, and on mules, and in coaches, to my holy mountain Jerusalem, says the Lord, in the same manner that the sons of Israel would carry an offering in a pure vessel into the house of the Lord.
21 Ndipo ndidzasankha ena mwa iwonso kukhala ansembe ndi Alevi,” akutero Yehova.
And I will take from them to be priests and Levites, says the Lord.
22 “Monga momwe mlengalenga mwatsopano ndi dziko lapansi latsopano zimene ndidzapanga zidzakhala mpaka muyaya pamaso panga, ndi chonchonso dzina lanu ndi zidzukulu zanu zidzakhalire.” Akutero Yehova.
For in like manner as the new heavens and the new earth, which I will cause to stand before me, says the Lord, so will your offspring and your name stand.
23 “Anthu a mitundu yonse adzabwera kudzandipembedza ku Yerusalemu, pa chikondwerero chilichonse cha pokhala pa mwezi watsopano ndi tsiku la Sabata lililonse,” akutero Yehova.
And there will be month after month, and Sabbath after Sabbath. And all flesh will approach, so as to adore before my face, says the Lord.
24 “Akamachoka adzaona mitembo ya anthu amene anandiwukira Ine. Mphutsi zawo sizidzafa, kapena moto wawo sudzazimitsidwa. Anthu a mitundu ina yonse powaona adzanyansidwa nawo.”
And they will go out, and they will view the carcasses of the men who have transgressed against me. Their worm will not die, and their fire will not be extinguished. And they will be a sight to all flesh even unto revulsion.

< Yesaya 66 >