< Yesaya 65 >
1 “Ndinali wokonzeka kumva mapemphero a amene sankandipempha kanthu; ndipo ndinalola kuti anthu amene ankandifunafuna kuti andipeze. Kwa mtundu wa anthu umene sunkapempha chithandizo kwa Ine, ndinati, ‘Ine ndili pano, Ine ndili pano.’
Я прихиля́вся до тих, що Мене не пита́ли, Я зна́йдений тими, що Мене не шукали. Я казав: „Оце Я, оце Я!“до наро́ду, що Йме́нням Моїм не був зва́ний.
2 Tsiku lonse ndatambasulira manja anga anthu owukira aja, amene amachita zoyipa, natsatira zokhumba zawo.
Я ввесь день простяга́в Свої руки до люду запе́клого, що він, за своїми думка́ми, доро́гою ходить недоброю,
3 Ndatambasulira manja anga anthu aja amene nthawi zonse amandikwiyitsa mopanda manyazi. Iwo amapereka nsembe mʼminda ndi kufukiza lubani pa maguwa ansembe a njerwa.
до наро́ду, що в очі Мене прогнівля́є пості́йно, що жертви прино́сить в садка́х та що па́лить кадило на це́глах,
4 Amakatandala ku manda ndipo amakachezera usiku wonse kumalo obisika. Amadya nyama ya nkhumba, ndipo mʼmiphika mwawo muli msunzi wa nyama yodetsedwa.
що сидить у гроба́х та ночує по я́мах, їсть свини́ну, і в їхньому по́суді — ю́шка нечиста,
5 Amawuza ena kuti, ‘Khala patali usandiyandikire, chifukwa ungatengere kupatulika kwanga!’ Ukali wanga pa anthu otere uli ngati utsi mphuno zanga, ngati moto umene umayaka tsiku lonse.
що говорить: „Спини́сь, не зближа́йся до ме́не, бо святий я для тебе!“Оце дим в Моїй ні́здрі, огонь, що палає ввесь день!
6 “Taonani, ndatsimikiza kale mlandu ndi chilango chawo; sindidzakhala chete koma ndidzawalanga kwathunthu chifukwa cha machimo awo
Ось напи́сане перед обличчям Моїм: Я не буду мовча́ти, але відплачу́, і надолу́жу на їхньому ло́ні!
7 ndi a makolo awo,” akutero Yehova. “Chifukwa anapereka nsembe zopsereza pa mapiri ndi kundinyoza Ine pa zitunda zawo, Ine ndidzawalanga kwathunthu potsata zimene anachita kale.”
Укупі пере́ступи ваші й пере́ступи ваших батькі́в, — говорить Госпо́дь, — що кади́ли на го́рах і на взгі́р'ях Мене зневажа́ли, — і запла́ту їм ви́міряю Я найпе́рше до їхнього ло́ня!
8 Yehova akuti, “Pamene madzi akanapezeka mu phava la mphesa ndipo anthu amati, ‘Musawononge phavalo, popeza madzi ena abwino akanalimobe mʼphavalo,’ Inenso chifukwa cha mtumiki wanga; sindidzawononga onse.
Так говорить Господь: Коли в гро́ні знахо́диться сік виногра́дний, і хтось ска́же: „Не псуй ти його, бо благослове́ння у ньо́му“, — отак Я зроблю́ ради рабів Своїх, щоб усього не ни́щити!
9 Ndidzatulutsa zidzukulu mʼbanja la Yakobo, ndipo a banja la Yuda adzalandira mapiri anga ngati cholowa chawo. Anthu anga osankhidwa adzalandira zimenezi, ndipo atumiki anga adzakhala kumeneko.
І насіння Я ви́веду з Якова, а з Юди — спадкоє́мця гір Моїх, і вибра́нці Мої одіди́чать її, і раби Мої жи́тимуть там.
10 Chigwa cha Saroni chidzakhala kodyetserako nkhosa, ndipo chigwa cha Akori chidzakhala malo opumirako ngʼombe kwa anthu anga ondifunafuna Ine.
І стане Шаро́н пасови́ськом ота́ри, а долина Ахо́р за ліжни́цю худо́би великої, для наро́ду Мого, що шукали Мене.
11 “Koma inu amene mumasiya Yehova ndi kuyiwala phiri langa lopatulika, amene munamukonzera Gadi chakudya ndi kuthirira Meni chakumwa,
А ви, що Господа кидаєте, забуваєте го́ру святу Мою, що ставите Ґаду трапе́зу, а для Ме́ні випо́внюєте жертву литу,
12 ndidzakuperekani ku lupanga ngati nsembe, ndipo nonse mudzaphedwa; chifukwa simunayankhe pamene ndinakuyitanani, ndinayankhula koma simunamvere. Munachita zoyipa pamaso panga ndipo munasankha kuchita zoyipa zomwe sindikondwera nazo.”
то вас відрахо́вую Я для меча́, й на коліна впаде́те ви всі на зарі́з, бо кликав Я вас, та ви відповіді не дали́, говорив був, але́ ви не чули й робили лихе́ в Моїх о́чах, і чого́ не хотів, вибира́ли собі!
13 Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti, “Atumiki anga adzadya, koma inu mudzakhala ndi njala; atumiki anga adzamwa, koma inu mudzakhala ndi ludzu; atumiki anga adzakondwa, koma inu mudzakhala ndi manyazi.
Тому Господь Бог каже так: Ось будуть раби Мої їсти, а ви бу́дете голодува́ти, ось будуть раби Мої пити, а ви будете спра́гнені, ось будуть раби Мої радіти, а ви посоро́млені бу́дете.
14 Atumiki anga adzayimba mosangalala, koma inu mudzalira kwambiri chifukwa chovutika mu mtima ndipo mudzalira mofuwula chifukwa mudzamva kuwawa mu mtima.
Ось раби Мої будуть співати від радости серця свого, ви ж крича́тимете від серде́чного бо́лю, і від скру́шення духа заво́дити бу́дете.
15 Anthu anga osankhidwa adzatchula dzina lanu potemberera. Ambuye Yehova adzakuphani, koma atumiki ake adzawapatsa dzina lina.
І ви своє йме́ння дасте́ на прокля́ття вибра́нцям Моїм, — і Господь Бог тебе вб'є, а рабам Своїм дасть інше йме́ння,
16 Aliyense wopempha dalitso mʼdzikomo adzachita zimenezo kwa Mulungu woona; ndipo aliyense wochita malumbiro mʼdzikomo adzalumbira mwa Mulungu woona. Pakuti mavuto akale adzayiwalika ndipo adzachotsedwa pamaso panga.
так що хто на землі благосло́влений бу́де, буде поблагосло́влений він вірним Богом, а хто на землі присяга́є, вірним Богом прися́гне, бо забу́дуться у́тиски давні і захо́вані будуть вони від оче́й Моїх!
17 “Taonani, ndikulenga mlengalenga mwatsopano ndi dziko lapansi latsopano. Zinthu zakale sizidzakumbukika, zidzayiwalika kotheratu.
Бо ось Я створю́ нове небо та зе́млю нову́, і не згада́ються ре́чі коли́шні, і не при́йдуть на серце!
18 Koma inu mukhale osangalala ndi okondwa mpaka muyaya chifukwa cha zimene ndikulenga, pakuti ndikulenga Yerusalemu kukhala malo wosangalatsa ndipo anthu ake adzakhala achimwemwe.
Тож навіки радійте та ті́штеся тим, що творю́ Я, бо ось Я створю́ Єрусалима на радість, а наро́да його — на весе́лість!
19 Ine ndidzakondwa chifuwa cha Yerusalemu ndipo ndidzasangalala chifukwa cha anthu anga. Kumeneko sikudzamvekanso kulira ndi mfuwu wodandaula.
І бу́ду Я Єрусалимом раді́ти, і втіша́тися буду наро́дом Своїм, — і не почу́ється в ньому вже голос плачу́ й голос зо́йку!
20 “Ana sadzafa ali akhanda ndipo nkhalamba zonse zidzakwaniritsa zaka zawo zonse. Wamngʼono mwa iwo adzafa ali ndi zaka 100. Amene adzalephere kufika zaka 100 adzatengedwa kukhala wotembereredwa.
З цього ча́су не буде вже ю́ного днями й старо́го, який своїх днів не попо́внить, бо сторо́кий помре́ як юна́к, а грішник і в віці ста літ буде про́клятий!
21 Anthu adzamanga nyumba ndi kukhalamo, adzadzala mpesa ndipo adzadya zipatso zake.
І доми́ побуду́ють, і ме́шкати будуть, і заса́дять вони виноградники, і будуть їхній плід спожива́ти.
22 Sadzamanganso nyumba anthu ena nʼkukhalamo, kapena kudzala ndi ena nʼkudya. Pakuti anthu anga adzakhala ndi moyo wautali ngati mitengo. Osankhidwa anga adzakondwera ndi ntchito ya manja awo nthawi yayitali.
Не бу́дуть вони будува́ти, щоб інший сидів, не будуть сади́ти, щоб інший спожи́в, дні бо наро́ду Мого — як дні де́рева, і вибра́нці Мої зужива́тимуть чин Своїх рук!
23 Sadzagwira ntchito pachabe kapena kubereka ana kuti aone tsoka; chifukwa adzakhala anthu odalitsidwa ndi Yehova, iwowo pamodzi ndi adzukulu awo omwe.
Не будуть вони працювати нада́рмо, і не будуть роди́ти на страх, вони бо насі́ння, благосло́влене Господом, і наща́дки їхні з ними.
24 Ndidzawayankha ngakhale asanathe nʼkupempha komwe. Pamene akuyankhula kumene Ine ndidzakhala nditamva kale.
І ста́неться, поки покли́чуть, то Я відпові́м, — вони будуть іще говорити, а Я вже почу́ю!
25 Mʼmbulu ndi mwana wankhosa wamkazi zidzadyera pamodzi. Mkango udzadya udzu monga ngʼombe, koma fumbi ndiye chidzakhale chakudya cha njoka. Pa phiri langa lopatulika sipadzakhala chinthu chopweteka kapena chowononga,” akutero Yehova.
Вовк та вівця́ будуть па́стися ра́зом, і лев буде їсти солому, немов та худо́ба, а га́дові хлібом його буде по́рох! Вони не чини́тимуть зла й вигубля́ти не будуть на всій святій Моїй горі, говорить Госпо́дь.