< Yesaya 65 >
1 “Ndinali wokonzeka kumva mapemphero a amene sankandipempha kanthu; ndipo ndinalola kuti anthu amene ankandifunafuna kuti andipeze. Kwa mtundu wa anthu umene sunkapempha chithandizo kwa Ine, ndinati, ‘Ine ndili pano, Ine ndili pano.’
Ngadingwa yilabo abangangicelanga; ngatholwa yilabo abangangidinganga. Ngathi: Ngikhangelani, ngikhangelani, esizweni esingabizwa ngebizo lami.
2 Tsiku lonse ndatambasulira manja anga anthu owukira aja, amene amachita zoyipa, natsatira zokhumba zawo.
Ngelule izandla zami usuku lonke ebantwini abavukelayo, abahamba ngendlela engalunganga, belandela imicabango yabo;
3 Ndatambasulira manja anga anthu aja amene nthawi zonse amandikwiyitsa mopanda manyazi. Iwo amapereka nsembe mʼminda ndi kufukiza lubani pa maguwa ansembe a njerwa.
abantu abangithukuthelisayo njalonjalo ebusweni bami, abenza imihlatshelo ezivandeni, betshisa impepha phezu kwezitina;
4 Amakatandala ku manda ndipo amakachezera usiku wonse kumalo obisika. Amadya nyama ya nkhumba, ndipo mʼmiphika mwawo muli msunzi wa nyama yodetsedwa.
abahlala emangcwabeni, balale endaweni ezisithekileyo, abadla inyama yengulube, lomhluzi wezinto ezinengekayo emiganwini yabo.
5 Amawuza ena kuti, ‘Khala patali usandiyandikire, chifukwa ungatengere kupatulika kwanga!’ Ukali wanga pa anthu otere uli ngati utsi mphuno zanga, ngati moto umene umayaka tsiku lonse.
Abathi: Xeka wena, ungasondeli kimi; ngoba ngingcwele kulawe. Laba bayintuthu emakhaleni ami, umlilo otshisayo usuku lonke.
6 “Taonani, ndatsimikiza kale mlandu ndi chilango chawo; sindidzakhala chete koma ndidzawalanga kwathunthu chifukwa cha machimo awo
Khangela, kubhaliwe phambi kwami: Kangiyikuthula, kodwa ngizaphindisela, yebo ngiphindisele esifubeni sabo,
7 ndi a makolo awo,” akutero Yehova. “Chifukwa anapereka nsembe zopsereza pa mapiri ndi kundinyoza Ine pa zitunda zawo, Ine ndidzawalanga kwathunthu potsata zimene anachita kale.”
iziphambeko zenu, leziphambeko zaboyihlo kanyekanye, itsho iNkosi, abatshise impepha phezu kwezintaba, bangithuka phezu kwamaqaqa; ngakho ngizalinganisa imisebenzi yabo yakuqala esifubeni sabo.
8 Yehova akuti, “Pamene madzi akanapezeka mu phava la mphesa ndipo anthu amati, ‘Musawononge phavalo, popeza madzi ena abwino akanalimobe mʼphavalo,’ Inenso chifukwa cha mtumiki wanga; sindidzawononga onse.
Itsho njalo iNkosi: Njengewayini elitsha litholwa ehlukuzweni, lomunye athi: Ungalibhubhisi, ngoba isibusiso sikulo; ngizakwenza njalo ngenxa yenceku zami, ukuze ngingazibhubhisi zonke.
9 Ndidzatulutsa zidzukulu mʼbanja la Yakobo, ndipo a banja la Yuda adzalandira mapiri anga ngati cholowa chawo. Anthu anga osankhidwa adzalandira zimenezi, ndipo atumiki anga adzakhala kumeneko.
Njalo ngizaveza inzalo ivela kuJakobe, lakoJuda kuvele indlalifa yezintaba zami; labakhethiweyo bami bazakudla ilifa lazo, lenceku zami zihlale khona.
10 Chigwa cha Saroni chidzakhala kodyetserako nkhosa, ndipo chigwa cha Akori chidzakhala malo opumirako ngʼombe kwa anthu anga ondifunafuna Ine.
Njalo iSharoni izakuba yisibaya semihlambi, lesihotsha seAkori sibe yindawo yokulala yenkomo, eyabantu bami abangidingayo.
11 “Koma inu amene mumasiya Yehova ndi kuyiwala phiri langa lopatulika, amene munamukonzera Gadi chakudya ndi kuthirira Meni chakumwa,
Kodwa lina elidela iNkosi, elikhohlwa intaba yami engcwele, elihlelele leloviyo itafula, njalo eligcwalisele lelonani umnikelo wokunathwayo.
12 ndidzakuperekani ku lupanga ngati nsembe, ndipo nonse mudzaphedwa; chifukwa simunayankhe pamene ndinakuyitanani, ndinayankhula koma simunamvere. Munachita zoyipa pamaso panga ndipo munasankha kuchita zoyipa zomwe sindikondwera nazo.”
Ngakho ngizalimisela inkemba, njalo lonke lizakhothamela ukuhlatshwa; ngoba ngalibiza, kodwa kaliphendulanga, ngakhuluma, kodwa kalizwanga, kodwa lenza okubi emehlweni ami, lakhetha lokho engingathokozanga ngakho.
13 Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti, “Atumiki anga adzadya, koma inu mudzakhala ndi njala; atumiki anga adzamwa, koma inu mudzakhala ndi ludzu; atumiki anga adzakondwa, koma inu mudzakhala ndi manyazi.
Ngakho itsho njalo iNkosi uJehova: Khangela, izinceku zami zizakudla, kodwa lina lizalamba; khangela, inceku zami zizanatha, kodwa lina lizakoma; khangela, inceku zami zizathokoza, kodwa lina lizayangeka;
14 Atumiki anga adzayimba mosangalala, koma inu mudzalira kwambiri chifukwa chovutika mu mtima ndipo mudzalira mofuwula chifukwa mudzamva kuwawa mu mtima.
khangela, inceku zami zizahlabela ngentokozo yenhliziyo, kodwa lina lizakhala ngenxa yokudabuka kwenhliziyo, liqhinqe isililo ngenxa yokudabuka komoya.
15 Anthu anga osankhidwa adzatchula dzina lanu potemberera. Ambuye Yehova adzakuphani, koma atumiki ake adzawapatsa dzina lina.
Njalo lizatshiya ibizo lenu libe yisiqalekiso kwabakhethiweyo bami, ngoba iNkosi uJehova izalibulala; kodwa izabiza inceku zayo ngelinye ibizo;
16 Aliyense wopempha dalitso mʼdzikomo adzachita zimenezo kwa Mulungu woona; ndipo aliyense wochita malumbiro mʼdzikomo adzalumbira mwa Mulungu woona. Pakuti mavuto akale adzayiwalika ndipo adzachotsedwa pamaso panga.
ukuthi lowo ozibusisa emhlabeni uzazibusisa kuNkulunkulu weqiniso, lalowo ofunga emhlabeni uzafunga ngoNkulunkulu weqiniso; ngoba inhlupheko zakuqala sezikhohlakele, njalo ngoba zisithekile emehlweni ami.
17 “Taonani, ndikulenga mlengalenga mwatsopano ndi dziko lapansi latsopano. Zinthu zakale sizidzakumbukika, zidzayiwalika kotheratu.
Ngoba khangela, ngidala amazulu amatsha lomhlaba omutsha; okwakuqala kakusayikukhunjulwa, kumbe kuvele enhliziyweni.
18 Koma inu mukhale osangalala ndi okondwa mpaka muyaya chifukwa cha zimene ndikulenga, pakuti ndikulenga Yerusalemu kukhala malo wosangalatsa ndipo anthu ake adzakhala achimwemwe.
Kodwa jabulani, lithokoze kuze kube laphakade ngengikudalayo, ngoba khangela, ngidala iJerusalema ibe yintokozo, labantu bayo babe yinjabulo.
19 Ine ndidzakondwa chifuwa cha Yerusalemu ndipo ndidzasangalala chifukwa cha anthu anga. Kumeneko sikudzamvekanso kulira ndi mfuwu wodandaula.
Ngizathokoza-ke ngeJerusalema, ngijabule ngabantu bami; njalo kalisayikuzwakala kuyo ilizwi lokulila lelizwi lokukhala.
20 “Ana sadzafa ali akhanda ndipo nkhalamba zonse zidzakwaniritsa zaka zawo zonse. Wamngʼono mwa iwo adzafa ali ndi zaka 100. Amene adzalephere kufika zaka 100 adzatengedwa kukhala wotembereredwa.
Kusukela lapho kakusayikuba khona usane lwezinsuku, kumbe ixhegu elingagcwalisi insuku zalo; ngoba omutsha uzakufa eleminyaka elikhulu, kodwa isoni esileminyaka elikhulu sizaqalekiswa.
21 Anthu adzamanga nyumba ndi kukhalamo, adzadzala mpesa ndipo adzadya zipatso zake.
Njalo bazakwakha izindlu, bahlale kuzo; bahlanyele izivini, badle izithelo zazo.
22 Sadzamanganso nyumba anthu ena nʼkukhalamo, kapena kudzala ndi ena nʼkudya. Pakuti anthu anga adzakhala ndi moyo wautali ngati mitengo. Osankhidwa anga adzakondwera ndi ntchito ya manja awo nthawi yayitali.
Kabayikwakha, kuhlale-ke omunye; kabayikuhlanyela, kudle-ke omunye; ngoba insuku zabantu bami zizakuba njengensuku zesihlahla, labakhethwa bami bazakholisa umsebenzi wezandla zabo okwesikhathi eside.
23 Sadzagwira ntchito pachabe kapena kubereka ana kuti aone tsoka; chifukwa adzakhala anthu odalitsidwa ndi Yehova, iwowo pamodzi ndi adzukulu awo omwe.
Kabayikutshikatshikela ize, loba bazalele uhlupho; ngoba bayinzalo yababusisiweyo beNkosi, lembewu yabo kanye labo.
24 Ndidzawayankha ngakhale asanathe nʼkupempha komwe. Pamene akuyankhula kumene Ine ndidzakhala nditamva kale.
Kuzakuthi-ke bengakabizi, mina ngiphendule; lapho besakhuluma, mina-ke ngizwe.
25 Mʼmbulu ndi mwana wankhosa wamkazi zidzadyera pamodzi. Mkango udzadya udzu monga ngʼombe, koma fumbi ndiye chidzakhale chakudya cha njoka. Pa phiri langa lopatulika sipadzakhala chinthu chopweteka kapena chowononga,” akutero Yehova.
Impisi lewundlu kuzakudla ndawonye, lesilwane sidle amahlanga njengenkomo, lothuli lube yikudla kwenyoka. Kaziyikulimaza kumbe zibhubhise kuyo yonke intaba yami engcwele, itsho iNkosi.