< Yesaya 65 >
1 “Ndinali wokonzeka kumva mapemphero a amene sankandipempha kanthu; ndipo ndinalola kuti anthu amene ankandifunafuna kuti andipeze. Kwa mtundu wa anthu umene sunkapempha chithandizo kwa Ine, ndinati, ‘Ine ndili pano, Ine ndili pano.’
“Ngaziveza kulabo abangangicelanga; ngafunyanwa yilabo abangangidinganga. Isizwe esingakhulekanga kimi ngathi kuso, ‘Ngilapha, ngilapha.’
2 Tsiku lonse ndatambasulira manja anga anthu owukira aja, amene amachita zoyipa, natsatira zokhumba zawo.
Ilanga lonke ngelula izandla zami ebantwini abayiziqholo, abahamba ngezindlela ezingalunganga belandela iminakano yabo,
3 Ndatambasulira manja anga anthu aja amene nthawi zonse amandikwiyitsa mopanda manyazi. Iwo amapereka nsembe mʼminda ndi kufukiza lubani pa maguwa ansembe a njerwa.
abantu abahlezi bengicunula bengikhangele, benikela imihlatshelo emasimini, betshisa impepha phezu kwezitina;
4 Amakatandala ku manda ndipo amakachezera usiku wonse kumalo obisika. Amadya nyama ya nkhumba, ndipo mʼmiphika mwawo muli msunzi wa nyama yodetsedwa.
abahlala emangcwabeni balale besenza imilindelo eyimfihlo ebusuku; abadla inyama yengulube, abambiza zabo zigcina umhluzi wenyama engcolileyo;
5 Amawuza ena kuti, ‘Khala patali usandiyandikire, chifukwa ungatengere kupatulika kwanga!’ Ukali wanga pa anthu otere uli ngati utsi mphuno zanga, ngati moto umene umayaka tsiku lonse.
abathi, ‘Hlala khatshana, ungasondeli phansi kwami, ngoba ngingcwele kulawe!’ Abantu abanjalo banjengentuthu emakhaleni ami, umlilo ovuthayo ilanga lonke.
6 “Taonani, ndatsimikiza kale mlandu ndi chilango chawo; sindidzakhala chete koma ndidzawalanga kwathunthu chifukwa cha machimo awo
Khangela, kulotshiwe phambi kwami ukuthi: Angiyikuthula, kodwa ngizaphindisela ngokugcweleyo; ngizaphindisela ngokupheleleyo,
7 ndi a makolo awo,” akutero Yehova. “Chifukwa anapereka nsembe zopsereza pa mapiri ndi kundinyoza Ine pa zitunda zawo, Ine ndidzawalanga kwathunthu potsata zimene anachita kale.”
kokubili izono zenu lezono zabokhokho benu,” kutsho uThixo. “Ngoba batshisa imihlatshelo phezu kwezintaba bangihlambaza phezu kwamaqaqa. Ngizaphindisela kubo ngokugcweleyo ngenxa yezenzo zabo abazenza ngaphambili.”
8 Yehova akuti, “Pamene madzi akanapezeka mu phava la mphesa ndipo anthu amati, ‘Musawononge phavalo, popeza madzi ena abwino akanalimobe mʼphavalo,’ Inenso chifukwa cha mtumiki wanga; sindidzawononga onse.
Nanku akutshoyo uThixo: “Njengalapho umhluzi usatholakala ehlukuzweni lamavini labantu besithi, ungalibhidlizi, kusekhona okuhle kulo, ngizazenzela okunjalo izinceku zami; angiyikuzibhubhisa zonke.
9 Ndidzatulutsa zidzukulu mʼbanja la Yakobo, ndipo a banja la Yuda adzalandira mapiri anga ngati cholowa chawo. Anthu anga osankhidwa adzalandira zimenezi, ndipo atumiki anga adzakhala kumeneko.
Ngizaletha isizukulwane esivela kuJakhobe, lakoJuda kuvele abazakuba ngabanikazi bezintaba zami; zizakuba yilifa labakhethiweyo bami, izinceku zami zizahlala khona.
10 Chigwa cha Saroni chidzakhala kodyetserako nkhosa, ndipo chigwa cha Akori chidzakhala malo opumirako ngʼombe kwa anthu anga ondifunafuna Ine.
ISharoni izakuba ngamadlelo emihlambi lesiGodi sase-Akhori sibe yindawo yokuphumulela imihlambi, yabantu bami abangidingayo.
11 “Koma inu amene mumasiya Yehova ndi kuyiwala phiri langa lopatulika, amene munamukonzera Gadi chakudya ndi kuthirira Meni chakumwa,
Kodwa lina elilahla uThixo likhohlwe intaba yami engcwele; liphakele unkulunkulu uNhlanhla ukudla libuye ligcwalisele unkulunkulu uSimiselo iwayini elixutshiweyo,
12 ndidzakuperekani ku lupanga ngati nsembe, ndipo nonse mudzaphedwa; chifukwa simunayankhe pamene ndinakuyitanani, ndinayankhula koma simunamvere. Munachita zoyipa pamaso panga ndipo munasankha kuchita zoyipa zomwe sindikondwera nazo.”
ngizalimisela inkemba, njalo lonke lizakhothamela ukubulawa, ngoba ngamemeza kodwa kalisabelanga, ngakhuluma kodwa lina kalilalelanga. Lenza okubi phambi kwami lakhetha okungicunulayo.”
13 Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti, “Atumiki anga adzadya, koma inu mudzakhala ndi njala; atumiki anga adzamwa, koma inu mudzakhala ndi ludzu; atumiki anga adzakondwa, koma inu mudzakhala ndi manyazi.
Ngakho-ke uThixo Wobukhosi uthi: “Izinceku zami zizakudla, kodwa lina lizalamba; izinceku zami zizanatha, kodwa lina lizakoma; izinceku zami zizathokoza, kodwa lina lizayangiswa.
14 Atumiki anga adzayimba mosangalala, koma inu mudzalira kwambiri chifukwa chovutika mu mtima ndipo mudzalira mofuwula chifukwa mudzamva kuwawa mu mtima.
Izinceku zami zizahlabelela ngentokozo yezinhliziyo zazo, kodwa lina lizakhala ngobuhlungu bezinhliziyo njalo lilile ngokudabuka komoya.
15 Anthu anga osankhidwa adzatchula dzina lanu potemberera. Ambuye Yehova adzakuphani, koma atumiki ake adzawapatsa dzina lina.
Lizatshiya ibizo lenu njengesithuko kwabakhethiweyo bami; uThixo Wobukhosi uzalibulala, kodwa izinceku zakhe uzazinika elinye ibizo.
16 Aliyense wopempha dalitso mʼdzikomo adzachita zimenezo kwa Mulungu woona; ndipo aliyense wochita malumbiro mʼdzikomo adzalumbira mwa Mulungu woona. Pakuti mavuto akale adzayiwalika ndipo adzachotsedwa pamaso panga.
Lowo okhulekela isibusiso elizweni uzakwenza lokho ngoNkulunkulu weqiniso; lalowo owenza isifungo elizweni, uzafunga ngoNkulunkulu weqiniso. Ngoba inhlupheko ezedlulayo zizakhohlakala zifihlakale emehlweni ami.”
17 “Taonani, ndikulenga mlengalenga mwatsopano ndi dziko lapansi latsopano. Zinthu zakale sizidzakumbukika, zidzayiwalika kotheratu.
“Khangelani, ngizadala izulu elitsha lomhlaba omutsha. Izinto zakuqala aziyikukhunjulwa, kumbe zifike engqondweni.
18 Koma inu mukhale osangalala ndi okondwa mpaka muyaya chifukwa cha zimene ndikulenga, pakuti ndikulenga Yerusalemu kukhala malo wosangalatsa ndipo anthu ake adzakhala achimwemwe.
Kodwa thabani lijabule kokuphela ngalokho engizakudala, ngoba ngizadala iJerusalema libe yintokozo labantu balo babe yinjabulo.
19 Ine ndidzakondwa chifuwa cha Yerusalemu ndipo ndidzasangalala chifukwa cha anthu anga. Kumeneko sikudzamvekanso kulira ndi mfuwu wodandaula.
Ngizathokoza ngeJerusalema njalo ngijabule ngabantu bami; ukulila lokukhala akusayikuzwakala kulo futhi.
20 “Ana sadzafa ali akhanda ndipo nkhalamba zonse zidzakwaniritsa zaka zawo zonse. Wamngʼono mwa iwo adzafa ali ndi zaka 100. Amene adzalephere kufika zaka 100 adzatengedwa kukhala wotembereredwa.
Kulo akusayikuba khona futhi usane oluphila insuku ezilutshwane kumbe umuntu omdala ongaphelelisi iminyaka yakhe; lowo ofa elekhulu leminyaka uzakhangelwa njengomntwana nje; lowo ongafikiyo ekhulwini uzakhangelwa njengoqalekisiweyo.
21 Anthu adzamanga nyumba ndi kukhalamo, adzadzala mpesa ndipo adzadya zipatso zake.
Bazakwakha izindlu bahlale kuzo; bazahlanyela izivini badle izithelo zazo.
22 Sadzamanganso nyumba anthu ena nʼkukhalamo, kapena kudzala ndi ena nʼkudya. Pakuti anthu anga adzakhala ndi moyo wautali ngati mitengo. Osankhidwa anga adzakondwera ndi ntchito ya manja awo nthawi yayitali.
Kabasayikwakha izindlu zihlalwe ngabanye kumbe bahlanyele, kudle abanye. Ngoba njengezinsuku zesihlahla, zizakuba njalo insuku zabantu bami; abakhethiweyo bami bazakholisa umsebenzi wezandla zabo okwesikhathi eside.
23 Sadzagwira ntchito pachabe kapena kubereka ana kuti aone tsoka; chifukwa adzakhala anthu odalitsidwa ndi Yehova, iwowo pamodzi ndi adzukulu awo omwe.
Kabayikusebenzela ize, kumbe abantwababo bazalelwe ukuhlupheka, ngoba bazakuba ngabantu ababusisiweyo nguThixo, bona kanye lezizukulwane zabo.
24 Ndidzawayankha ngakhale asanathe nʼkupempha komwe. Pamene akuyankhula kumene Ine ndidzakhala nditamva kale.
Ngizabaphendula bengakakhuleki; ngibezwe besakhuluma.
25 Mʼmbulu ndi mwana wankhosa wamkazi zidzadyera pamodzi. Mkango udzadya udzu monga ngʼombe, koma fumbi ndiye chidzakhale chakudya cha njoka. Pa phiri langa lopatulika sipadzakhala chinthu chopweteka kapena chowononga,” akutero Yehova.
Impisi lewundlu kuzakudla ndawonye, lesilwane sizakudla utshani njengenkomo, kodwa inyoka izakudla uthuli. Kaziyikulimaza kumbe zibhubhise kuyo yonke intaba yami engcwele,” kutsho uThixo.