< Yesaya 65 >
1 “Ndinali wokonzeka kumva mapemphero a amene sankandipempha kanthu; ndipo ndinalola kuti anthu amene ankandifunafuna kuti andipeze. Kwa mtundu wa anthu umene sunkapempha chithandizo kwa Ine, ndinati, ‘Ine ndili pano, Ine ndili pano.’
to seek to/for not to ask to find to/for not to seek me to say look! I look! I to(wards) nation not to call: call by in/on/with name my
2 Tsiku lonse ndatambasulira manja anga anthu owukira aja, amene amachita zoyipa, natsatira zokhumba zawo.
to spread hand my all [the] day to(wards) people to rebel [the] to go: walk [the] way: conduct not pleasant after plot their
3 Ndatambasulira manja anga anthu aja amene nthawi zonse amandikwiyitsa mopanda manyazi. Iwo amapereka nsembe mʼminda ndi kufukiza lubani pa maguwa ansembe a njerwa.
[the] people [the] to provoke [obj] me upon face my continually to sacrifice in/on/with garden and to offer: offer upon [the] brick
4 Amakatandala ku manda ndipo amakachezera usiku wonse kumalo obisika. Amadya nyama ya nkhumba, ndipo mʼmiphika mwawo muli msunzi wa nyama yodetsedwa.
[the] to dwell in/on/with grave and in/on/with to watch to lodge [the] to eat flesh [the] swine (and broth *Q(K)*) refuse article/utensil their
5 Amawuza ena kuti, ‘Khala patali usandiyandikire, chifukwa ungatengere kupatulika kwanga!’ Ukali wanga pa anthu otere uli ngati utsi mphuno zanga, ngati moto umene umayaka tsiku lonse.
[the] to say to present: come to(wards) you not to approach: approach in/on/with me for to consecrate: consecate you these smoke in/on/with face: nose my fire to burn all [the] day
6 “Taonani, ndatsimikiza kale mlandu ndi chilango chawo; sindidzakhala chete koma ndidzawalanga kwathunthu chifukwa cha machimo awo
behold to write to/for face: before my not be silent that if: except if: except to complete and to complete upon bosom: lap their
7 ndi a makolo awo,” akutero Yehova. “Chifukwa anapereka nsembe zopsereza pa mapiri ndi kundinyoza Ine pa zitunda zawo, Ine ndidzawalanga kwathunthu potsata zimene anachita kale.”
iniquity: crime your and iniquity: crime father your together to say LORD which to offer: offer upon [the] mountain: mount and upon [the] hill to taunt me and to measure wages their first: previous (to(wards) *Q(K)*) bosom: lap their
8 Yehova akuti, “Pamene madzi akanapezeka mu phava la mphesa ndipo anthu amati, ‘Musawononge phavalo, popeza madzi ena abwino akanalimobe mʼphavalo,’ Inenso chifukwa cha mtumiki wanga; sindidzawononga onse.
thus to say LORD like/as as which to find [the] new wine in/on/with cluster and to say not to ruin him for blessing in/on/with him so to make: do because servant/slave my to/for lest to ruin [the] all
9 Ndidzatulutsa zidzukulu mʼbanja la Yakobo, ndipo a banja la Yuda adzalandira mapiri anga ngati cholowa chawo. Anthu anga osankhidwa adzalandira zimenezi, ndipo atumiki anga adzakhala kumeneko.
and to come out: send from Jacob seed: children and from Judah to possess: possess mountain: mount my and to possess: take her chosen my and servant/slave my to dwell there [to]
10 Chigwa cha Saroni chidzakhala kodyetserako nkhosa, ndipo chigwa cha Akori chidzakhala malo opumirako ngʼombe kwa anthu anga ondifunafuna Ine.
and to be [the] Sharon to/for pasture flock and Valley (of Achor) (Valley of) Achor to/for rest cattle to/for people my which to seek me
11 “Koma inu amene mumasiya Yehova ndi kuyiwala phiri langa lopatulika, amene munamukonzera Gadi chakudya ndi kuthirira Meni chakumwa,
and you(m. p.) to leave: forsake LORD [the] forgetful [obj] mountain: mount holiness my [the] to arrange to/for Fortune table and [the] to fill to/for Destiny mixed drink
12 ndidzakuperekani ku lupanga ngati nsembe, ndipo nonse mudzaphedwa; chifukwa simunayankhe pamene ndinakuyitanani, ndinayankhula koma simunamvere. Munachita zoyipa pamaso panga ndipo munasankha kuchita zoyipa zomwe sindikondwera nazo.”
and to count [obj] you to/for sword and all your to/for slaughter to bow because to call: call to and not to answer to speak: speak and not to hear: hear and to make: do [the] bad: evil in/on/with eye my and in/on/with in which not to delight in to choose
13 Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti, “Atumiki anga adzadya, koma inu mudzakhala ndi njala; atumiki anga adzamwa, koma inu mudzakhala ndi ludzu; atumiki anga adzakondwa, koma inu mudzakhala ndi manyazi.
to/for so thus to say Lord YHWH/God behold servant/slave my to eat and you(m. p.) be hungry behold servant/slave my to drink and you(m. p.) to thirst behold servant/slave my to rejoice and you(m. p.) be ashamed
14 Atumiki anga adzayimba mosangalala, koma inu mudzalira kwambiri chifukwa chovutika mu mtima ndipo mudzalira mofuwula chifukwa mudzamva kuwawa mu mtima.
behold servant/slave my to sing from goodness heart and you(m. p.) to cry from pain heart and from breaking spirit to wail
15 Anthu anga osankhidwa adzatchula dzina lanu potemberera. Ambuye Yehova adzakuphani, koma atumiki ake adzawapatsa dzina lina.
and to rest name your to/for oath to/for chosen my and to die you Lord YHWH/God and to/for servant/slave his to call: call by name another
16 Aliyense wopempha dalitso mʼdzikomo adzachita zimenezo kwa Mulungu woona; ndipo aliyense wochita malumbiro mʼdzikomo adzalumbira mwa Mulungu woona. Pakuti mavuto akale adzayiwalika ndipo adzachotsedwa pamaso panga.
which [the] to bless in/on/with land: country/planet to bless in/on/with God amen and [the] to swear in/on/with land: country/planet to swear in/on/with God amen for to forget [the] distress [the] first: previous and for to hide from eye my
17 “Taonani, ndikulenga mlengalenga mwatsopano ndi dziko lapansi latsopano. Zinthu zakale sizidzakumbukika, zidzayiwalika kotheratu.
for look! I to create heaven new and land: country/planet new and not to remember [the] first: previous and not to ascend: rise upon heart
18 Koma inu mukhale osangalala ndi okondwa mpaka muyaya chifukwa cha zimene ndikulenga, pakuti ndikulenga Yerusalemu kukhala malo wosangalatsa ndipo anthu ake adzakhala achimwemwe.
for if: except to rejoice and to rejoice till perpetuity which I to create for look! I to create [obj] Jerusalem rejoicing and people her rejoicing
19 Ine ndidzakondwa chifuwa cha Yerusalemu ndipo ndidzasangalala chifukwa cha anthu anga. Kumeneko sikudzamvekanso kulira ndi mfuwu wodandaula.
and to rejoice in/on/with Jerusalem and to rejoice in/on/with people my and not to hear: hear in/on/with her still voice: sound weeping and voice outcry
20 “Ana sadzafa ali akhanda ndipo nkhalamba zonse zidzakwaniritsa zaka zawo zonse. Wamngʼono mwa iwo adzafa ali ndi zaka 100. Amene adzalephere kufika zaka 100 adzatengedwa kukhala wotembereredwa.
not to be from there still infant day and old which not to fill [obj] day his for [the] youth son: aged hundred year to die and [the] to sin son: aged hundred year to lighten
21 Anthu adzamanga nyumba ndi kukhalamo, adzadzala mpesa ndipo adzadya zipatso zake.
and to build house: home and to dwell and to plant vineyard and to eat fruit their
22 Sadzamanganso nyumba anthu ena nʼkukhalamo, kapena kudzala ndi ena nʼkudya. Pakuti anthu anga adzakhala ndi moyo wautali ngati mitengo. Osankhidwa anga adzakondwera ndi ntchito ya manja awo nthawi yayitali.
not to build and another to dwell not to plant and another to eat for like/as day [the] tree day people my and deed: work hand their to become old chosen my
23 Sadzagwira ntchito pachabe kapena kubereka ana kuti aone tsoka; chifukwa adzakhala anthu odalitsidwa ndi Yehova, iwowo pamodzi ndi adzukulu awo omwe.
not be weary/toil to/for vain and not to beget to/for dismay for seed: children to bless LORD they(masc.) and offspring their with them
24 Ndidzawayankha ngakhale asanathe nʼkupempha komwe. Pamene akuyankhula kumene Ine ndidzakhala nditamva kale.
and to be before to call: call to and I to answer still they(masc.) to speak: speak and I to hear: hear
25 Mʼmbulu ndi mwana wankhosa wamkazi zidzadyera pamodzi. Mkango udzadya udzu monga ngʼombe, koma fumbi ndiye chidzakhale chakudya cha njoka. Pa phiri langa lopatulika sipadzakhala chinthu chopweteka kapena chowononga,” akutero Yehova.
wolf and lamb to pasture like/as one and lion like/as cattle to eat straw and serpent dust food his not be evil and not to ruin in/on/with all mountain: mount holiness my to say LORD