< Yesaya 65 >

1 “Ndinali wokonzeka kumva mapemphero a amene sankandipempha kanthu; ndipo ndinalola kuti anthu amene ankandifunafuna kuti andipeze. Kwa mtundu wa anthu umene sunkapempha chithandizo kwa Ine, ndinati, ‘Ine ndili pano, Ine ndili pano.’
I allowed myself to be sought by those that asked not; I let myself be found by those that sought me not: I said, Here am I, here am I, unto a nation that called itself not by my name.
2 Tsiku lonse ndatambasulira manja anga anthu owukira aja, amene amachita zoyipa, natsatira zokhumba zawo.
I spread out my hands all the time unto a rebellious people, that walk in the way which is not good, after their own thoughts;
3 Ndatambasulira manja anga anthu aja amene nthawi zonse amandikwiyitsa mopanda manyazi. Iwo amapereka nsembe mʼminda ndi kufukiza lubani pa maguwa ansembe a njerwa.
[To] the people that provoke me to anger to my face continually; that sacrifice in gardens and burn incense upon [altars of] brick,
4 Amakatandala ku manda ndipo amakachezera usiku wonse kumalo obisika. Amadya nyama ya nkhumba, ndipo mʼmiphika mwawo muli msunzi wa nyama yodetsedwa.
That sit about among the graves, and lodge in the vaults, that eat the flesh of the swine, and [have] broth of abominations [in] their vessels;
5 Amawuza ena kuti, ‘Khala patali usandiyandikire, chifukwa ungatengere kupatulika kwanga!’ Ukali wanga pa anthu otere uli ngati utsi mphuno zanga, ngati moto umene umayaka tsiku lonse.
That say, Stand by thyself, come not near to me; for I am holier than thou. These are a smoke in my nose, a fire that burneth all the time.
6 “Taonani, ndatsimikiza kale mlandu ndi chilango chawo; sindidzakhala chete koma ndidzawalanga kwathunthu chifukwa cha machimo awo
Behold, it is written before me; I will not keep silence, till I have recompensed, yea, recompensed into their bosom.—
7 ndi a makolo awo,” akutero Yehova. “Chifukwa anapereka nsembe zopsereza pa mapiri ndi kundinyoza Ine pa zitunda zawo, Ine ndidzawalanga kwathunthu potsata zimene anachita kale.”
Your iniquities and the iniquities of your fathers together, saith the Lord, who have burnt incense upon the mountains, and upon the hills have blasphemed me: and I will measure out their work at first into their bosom.
8 Yehova akuti, “Pamene madzi akanapezeka mu phava la mphesa ndipo anthu amati, ‘Musawononge phavalo, popeza madzi ena abwino akanalimobe mʼphavalo,’ Inenso chifukwa cha mtumiki wanga; sindidzawononga onse.
Thus hath said the Lord, As the new wine is found in the cluster of grapes, and one saith, Destroy it not, for a blessing is in it; so will I do for the sake of my servants, that I will not destroy the whole;
9 Ndidzatulutsa zidzukulu mʼbanja la Yakobo, ndipo a banja la Yuda adzalandira mapiri anga ngati cholowa chawo. Anthu anga osankhidwa adzalandira zimenezi, ndipo atumiki anga adzakhala kumeneko.
And I let come forth out of Jacob a seed, and out of Judah an inheritor of my mountains; and my elect shall inherit it, and my servants shall dwell there.
10 Chigwa cha Saroni chidzakhala kodyetserako nkhosa, ndipo chigwa cha Akori chidzakhala malo opumirako ngʼombe kwa anthu anga ondifunafuna Ine.
And Sharon shall become a fold of flocks, and the valley of 'Achor a resting-place for herds, for my people that have sought me.
11 “Koma inu amene mumasiya Yehova ndi kuyiwala phiri langa lopatulika, amene munamukonzera Gadi chakudya ndi kuthirira Meni chakumwa,
But ye who forsake the Lord, who forget my holy mountain, that set out a table for the god of Fortune, and that fill for Destiny the drink-offering.—
12 ndidzakuperekani ku lupanga ngati nsembe, ndipo nonse mudzaphedwa; chifukwa simunayankhe pamene ndinakuyitanani, ndinayankhula koma simunamvere. Munachita zoyipa pamaso panga ndipo munasankha kuchita zoyipa zomwe sindikondwera nazo.”
Yea, I will destine you to the sword, and all of you shall kneel down to the slaughter; because when I called, ye did not answer; when I spoke, ye did not hear; but ye did what is evil in my eyes, and that wherein I had no delight did ye choose.
13 Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti, “Atumiki anga adzadya, koma inu mudzakhala ndi njala; atumiki anga adzamwa, koma inu mudzakhala ndi ludzu; atumiki anga adzakondwa, koma inu mudzakhala ndi manyazi.
Therefore thus hath said the Lord Eternal, Behold, my servants shall eat, but ye shall be hungry; behold, my servants shall drink, but ye shall be thirsty; behold, my servants shall rejoice, but ye shall be made ashamed;
14 Atumiki anga adzayimba mosangalala, koma inu mudzalira kwambiri chifukwa chovutika mu mtima ndipo mudzalira mofuwula chifukwa mudzamva kuwawa mu mtima.
Behold, my servants shall sing for joy of heart, but ye shall cry out from pain of heart, and from a broken spirit shall ye howl;
15 Anthu anga osankhidwa adzatchula dzina lanu potemberera. Ambuye Yehova adzakuphani, koma atumiki ake adzawapatsa dzina lina.
And ye shall leave behind your name for an oath unto my elect ones, when the Lord Eternal will slay thee; but his servants will he call by another name.
16 Aliyense wopempha dalitso mʼdzikomo adzachita zimenezo kwa Mulungu woona; ndipo aliyense wochita malumbiro mʼdzikomo adzalumbira mwa Mulungu woona. Pakuti mavuto akale adzayiwalika ndipo adzachotsedwa pamaso panga.
Whoever there be that blesseth himself on the earth shall bless himself by the true God; and that sweareth on the earth shall swear by the true God; because the former troubles are forgotten, and because they are hidden from my eyes.
17 “Taonani, ndikulenga mlengalenga mwatsopano ndi dziko lapansi latsopano. Zinthu zakale sizidzakumbukika, zidzayiwalika kotheratu.
For, behold, I will create new heavens and a new earth; and the former shall not be remembered, nor come into mind;
18 Koma inu mukhale osangalala ndi okondwa mpaka muyaya chifukwa cha zimene ndikulenga, pakuti ndikulenga Yerusalemu kukhala malo wosangalatsa ndipo anthu ake adzakhala achimwemwe.
But be ye glad and rejoice unto all eternity in what I create; for, behold, I will create Jerusalem for rejoicing, and her people for gladness.
19 Ine ndidzakondwa chifuwa cha Yerusalemu ndipo ndidzasangalala chifukwa cha anthu anga. Kumeneko sikudzamvekanso kulira ndi mfuwu wodandaula.
And I will rejoice over Jerusalem, and be glad in my people: and there shall not be heard in her any more the voice of weeping, nor the voice of complaint.
20 “Ana sadzafa ali akhanda ndipo nkhalamba zonse zidzakwaniritsa zaka zawo zonse. Wamngʼono mwa iwo adzafa ali ndi zaka 100. Amene adzalephere kufika zaka 100 adzatengedwa kukhala wotembereredwa.
There shall no more come thence an infant of few days, nor an old man that shall not have the full length of his days; for as a lad shall one die a hundred years old; and as a sinner shall be accursed he who [dieth] at a hundred years old.
21 Anthu adzamanga nyumba ndi kukhalamo, adzadzala mpesa ndipo adzadya zipatso zake.
And they shall build houses, and inhabit them; and they shall plant vineyards, and eat their fruit.
22 Sadzamanganso nyumba anthu ena nʼkukhalamo, kapena kudzala ndi ena nʼkudya. Pakuti anthu anga adzakhala ndi moyo wautali ngati mitengo. Osankhidwa anga adzakondwera ndi ntchito ya manja awo nthawi yayitali.
They shall not build, and another inhabit; they shall not plant, and another eat; for as the days of a tree are the days of my people, and the work of their hands shall my elect wear out.
23 Sadzagwira ntchito pachabe kapena kubereka ana kuti aone tsoka; chifukwa adzakhala anthu odalitsidwa ndi Yehova, iwowo pamodzi ndi adzukulu awo omwe.
They shall not toil in vain, nor bring forth unto an early death; for the seed of the blessed of the Lord are they, and their offspring with them.
24 Ndidzawayankha ngakhale asanathe nʼkupempha komwe. Pamene akuyankhula kumene Ine ndidzakhala nditamva kale.
And it shall come to pass, that before yet they call will I answer; and while they are still speaking will I hear.
25 Mʼmbulu ndi mwana wankhosa wamkazi zidzadyera pamodzi. Mkango udzadya udzu monga ngʼombe, koma fumbi ndiye chidzakhale chakudya cha njoka. Pa phiri langa lopatulika sipadzakhala chinthu chopweteka kapena chowononga,” akutero Yehova.
The wolf and the lamb shall feed together, and the lion shall like the bullock eat straw: and the serpent—dust shall be his food. They shall not hurt nor destroy in all my holy mountain, saith the Lord.

< Yesaya 65 >