< Yesaya 64 >
1 Inu Yehova, bwanji mukanangongʼamba mlengalenga ndi kutsika pansi, kuti mapiri agwedezeke pamaso panu!
Oh! si vous ouvriez les cieux, si vous descendiez! devant votre face les montagnes s’écouleraient.
2 Monga momwe moto umatenthera tchire ndiponso kuwiritsa madzi, tsikani kuti adani anu adziwe dzina lanu, ndiponso kuti mitundu ya anthu injenjemere pamaso panu.
Comme un embrasement elles se consumeraient, les eaux s’embraseraient, afin que votre nom fût connu à vos ennemis, et que devant votre face les nations fussent troublées.
3 Pakuti nthawi ina pamene munatsika munachita zinthu zoopsa zimene sitinaziyembekezere, ndipo mapiri anagwedezeka pamaso panu.
Lorsque vous ferez des merveilles, nous ne les soutiendrons pas; vous êtes descendu, et devant votre face se sont écoulées les montagnes.
4 Chikhalire palibe ndi mmodzi yemwe anamvapo kapena kuona Mulungu wina wonga Inu, amene amachitira zinthu zotere amene amadikira pa Iye.
Dès les temps anciens on n’a pas entendu, et on n’a pas prêté l’oreille; l’œil n’a pas vu, ô Dieu, hors vous, ce que vous avez préparé à ceux qui vous attendent.
5 Inu mumabwera kudzathandiza onse amene amakondwera pochita zolungama, amene amakumbukira njira zanu. Koma Inu munakwiya, ife tinapitiriza kuchimwa. Kodi nanga tingapulumutsidwe bwanji?
Vous êtes allé à la rencontre de celui qui était dans la joie, et qui pratiquait la justice; dans vos voies ils se souviendront de vous; voilà que vous vous êtes irrité, et nous avons péché; dans les péchés nous avons toujours été, mais nous serons sauvés.
6 Tonsefe takhala ngati anthu amene ndi odetsedwa, ndipo ntchito zathu zili ngati sanza za msambo; tonse tafota ngati tsamba, ndipo machimo athu akutiwuluzira kutali ngati mphepo.
Et nous sommes devenus nous tous comme un homme impur, et comme un linge souillé est toute notre justice; nous sommes tombés tous comme la feuille, et nos iniquités comme le vent nous ont emportés.
7 Palibe amene amapemphera kwa Inu kutekeseka kuti apemphe chithandizo kwa Inu; pakuti mwatifulatira ndi kutisiya chifukwa cha machimo athu.
Il n’y a personne qui invoque votre nom, qui se lève et qui vous retienne; vous nous avez caché votre face, et vous nous avez brisés dans la main de notre iniquité.
8 Komabe, Inu Yehova ndinu Atate athu. Ife ndife chowumba, Inu ndinu wowumba; ife tonse ndi ntchito ya manja anu.
Et maintenant, Seigneur, vous êtes notre père, vous; mais nous de l’argile, et vous nous avez formés, et nous sommes tous les ouvrages de vos mains.
9 Inu Yehova, musatikwiyire kopitirira muyeso musakumbukire machimo athu mpaka muyaya. Chonde, mutiganizire, ife tikupempha, pakuti tonsefe ndi anthu anu.
Ne vous irritez pas trop, Seigneur, et ne vous souvenez plus de notre iniquité; regardez plutôt, nous sommes tous votre peuple.
10 Mizinda yanu yopatulika yasanduka chipululu; ngakhaletu Ziyoni wasanduka chipululu, Yerusalemu ndi wamasiye.
La cité de votre saint est devenue déserte, Sion est devenue déserte, Jérusalem est désolée.
11 Nyumba yanu yopatulika ndi yaulemu, kumene makolo athu ankakutamandani, yatenthedwa ndi moto ndipo malo onse amene tinkawakonda asanduka bwinja.
La maison de notre sanctification et de notre gloire, où vous ont loué nos pères, a été embrasée, et tous nos bâtiments précieux ont été changés en ruines.
12 Inu Yehova, zonse zachitikazi, kodi mungokhala osatithandiza? Kodi mudzapitirizabe kukhala chete ndi kutilangabe mopitirira muyeso?
Est-ce qu’après cela vous vous contiendrez, Seigneur, vous vous tairez, et vous nous affligerez sans mesure?