< Yesaya 64 >
1 Inu Yehova, bwanji mukanangongʼamba mlengalenga ndi kutsika pansi, kuti mapiri agwedezeke pamaso panu!
if to tear heaven to go down from face your mountain: mount to shake
2 Monga momwe moto umatenthera tchire ndiponso kuwiritsa madzi, tsikani kuti adani anu adziwe dzina lanu, ndiponso kuti mitundu ya anthu injenjemere pamaso panu.
like/as to kindle fire brushwood water to enquire fire to/for to know name your to/for enemy your from face your nation to tremble
3 Pakuti nthawi ina pamene munatsika munachita zinthu zoopsa zimene sitinaziyembekezere, ndipo mapiri anagwedezeka pamaso panu.
in/on/with to make: do you to fear: revere not to await to go down from face your mountain: mount to shake
4 Chikhalire palibe ndi mmodzi yemwe anamvapo kapena kuona Mulungu wina wonga Inu, amene amachitira zinthu zotere amene amadikira pa Iye.
and from forever: antiquity not to hear: hear not to listen eye not to see: see God exception you to make: do to/for to wait to/for him
5 Inu mumabwera kudzathandiza onse amene amakondwera pochita zolungama, amene amakumbukira njira zanu. Koma Inu munakwiya, ife tinapitiriza kuchimwa. Kodi nanga tingapulumutsidwe bwanji?
to fall on [obj] to rejoice and to make: do righteousness in/on/with way: conduct your to remember you look! you(m. s.) be angry and to sin in/on/with them forever: antiquity and to save
6 Tonsefe takhala ngati anthu amene ndi odetsedwa, ndipo ntchito zathu zili ngati sanza za msambo; tonse tafota ngati tsamba, ndipo machimo athu akutiwuluzira kutali ngati mphepo.
and to be like/as unclean all our and like/as garment filth all righteousness our and to wither like/as leaf all our and iniquity: crime our like/as spirit: breath to lift: bear us
7 Palibe amene amapemphera kwa Inu kutekeseka kuti apemphe chithandizo kwa Inu; pakuti mwatifulatira ndi kutisiya chifukwa cha machimo athu.
and nothing to call: call to in/on/with name your to rouse to/for to strengthen: hold in/on/with you for to hide face your from us and to melt us in/on/with hand: themselves iniquity: crime our
8 Komabe, Inu Yehova ndinu Atate athu. Ife ndife chowumba, Inu ndinu wowumba; ife tonse ndi ntchito ya manja anu.
and now LORD father our you(m. s.) we [the] clay and you(m. s.) to form: potter us and deed: work hand your all our
9 Inu Yehova, musatikwiyire kopitirira muyeso musakumbukire machimo athu mpaka muyaya. Chonde, mutiganizire, ife tikupempha, pakuti tonsefe ndi anthu anu.
not be angry LORD till much and not to/for perpetuity to remember iniquity: crime look! to look please people your all our
10 Mizinda yanu yopatulika yasanduka chipululu; ngakhaletu Ziyoni wasanduka chipululu, Yerusalemu ndi wamasiye.
city holiness your to be wilderness Zion wilderness to be Jerusalem devastation
11 Nyumba yanu yopatulika ndi yaulemu, kumene makolo athu ankakutamandani, yatenthedwa ndi moto ndipo malo onse amene tinkawakonda asanduka bwinja.
house: temple holiness our and beauty our which to boast: praise you father our to be to/for fire fire and all desire our to be to/for desolation
12 Inu Yehova, zonse zachitikazi, kodi mungokhala osatithandiza? Kodi mudzapitirizabe kukhala chete ndi kutilangabe mopitirira muyeso?
upon these to refrain LORD be silent and to afflict us till much