< Yesaya 64 >

1 Inu Yehova, bwanji mukanangongʼamba mlengalenga ndi kutsika pansi, kuti mapiri agwedezeke pamaso panu!
Oh that thou would rend the heavens, that thou would come down, that the mountains might quake at thy presence,
2 Monga momwe moto umatenthera tchire ndiponso kuwiritsa madzi, tsikani kuti adani anu adziwe dzina lanu, ndiponso kuti mitundu ya anthu injenjemere pamaso panu.
as when fire kindles the brushwood, and the fire causes the waters to boil, to make thy name known to thine adversaries, that the nations may tremble at thy presence!
3 Pakuti nthawi ina pamene munatsika munachita zinthu zoopsa zimene sitinaziyembekezere, ndipo mapiri anagwedezeka pamaso panu.
When thou did fearful things which we did not look for, thou came down; the mountains quaked at thy presence.
4 Chikhalire palibe ndi mmodzi yemwe anamvapo kapena kuona Mulungu wina wonga Inu, amene amachitira zinthu zotere amene amadikira pa Iye.
For from of old men have not heard, nor perceived by the ear, neither has the eye seen, O God, besides thee, what he has prepared for him who waits for him.
5 Inu mumabwera kudzathandiza onse amene amakondwera pochita zolungama, amene amakumbukira njira zanu. Koma Inu munakwiya, ife tinapitiriza kuchimwa. Kodi nanga tingapulumutsidwe bwanji?
Thou meet him who rejoices and works righteousness, those who remember thee in thy ways. Behold, thou were angry, and we sinned. Therefore we have erred.
6 Tonsefe takhala ngati anthu amene ndi odetsedwa, ndipo ntchito zathu zili ngati sanza za msambo; tonse tafota ngati tsamba, ndipo machimo athu akutiwuluzira kutali ngati mphepo.
For we have all become as unclean, and all our righteous acts are as a polluted garment. And we all fade as a leaf. And our iniquities, like the wind, take us away.
7 Palibe amene amapemphera kwa Inu kutekeseka kuti apemphe chithandizo kwa Inu; pakuti mwatifulatira ndi kutisiya chifukwa cha machimo athu.
And there is none who calls upon thy name, who stirs himself up to take hold of thee. For thou have hid thy face from us, and have consumed us through our iniquities.
8 Komabe, Inu Yehova ndinu Atate athu. Ife ndife chowumba, Inu ndinu wowumba; ife tonse ndi ntchito ya manja anu.
But now, O Jehovah, thou are our Father. We are the clay, and thou our potter, and we are all the work of thy hand.
9 Inu Yehova, musatikwiyire kopitirira muyeso musakumbukire machimo athu mpaka muyaya. Chonde, mutiganizire, ife tikupempha, pakuti tonsefe ndi anthu anu.
Be not angry very severely, O Jehovah, nor remember iniquity forever. Behold, look, we beseech thee, we are all thy people.
10 Mizinda yanu yopatulika yasanduka chipululu; ngakhaletu Ziyoni wasanduka chipululu, Yerusalemu ndi wamasiye.
Thy holy cities have become a wilderness. Zion has become a wilderness, Jerusalem a desolation.
11 Nyumba yanu yopatulika ndi yaulemu, kumene makolo athu ankakutamandani, yatenthedwa ndi moto ndipo malo onse amene tinkawakonda asanduka bwinja.
Our holy and our beautiful house, where our fathers praised thee, is burned with fire, and all our pleasant places are laid waste.
12 Inu Yehova, zonse zachitikazi, kodi mungokhala osatithandiza? Kodi mudzapitirizabe kukhala chete ndi kutilangabe mopitirira muyeso?
Will thou restrain thyself for these things, O Jehovah? Will thou hold thy peace, and afflict us very severely?

< Yesaya 64 >