< Yesaya 63 >

1 Kodi ndani uyo akubwera kuchokera ku Edomu, atavala zovala za ku Bozira za madontho ofiira? Kodi uyu ndani, amene wavala zovala zokongola, akuyenda mwa mphamvu zake? “Ndi Ineyo, woyankhula zachilungamo ndiponso wamphamvu zopulumutsa.”
Qui est celui qui vient d'Edom, avec des vêtements teints de Bozrah? Qui est celui qui est glorieux dans ses vêtements, marchant dans la grandeur de sa force? « C'est moi qui parle en justice, puissant pour sauver. »
2 Nanga bwanji zovala zanu zili psuu, ngati za munthu wofinya mphesa?
Pourquoi vos vêtements sont rouges, et tes vêtements comme celui qui foule dans la cuve à vin?
3 “Ndapondereza ndekha anthu a mitundu ina ngati mphesa, palibe ndi mmodzi yemwe anali nane. Ndinawapondereza ndili wokwiya ndipo ndinawapondereza ndili ndi ukali; magazi awo anadothera pa zovala zanga, ndipo zovala zanga zonse zinathimbirira.
« J'ai foulé seul le pressoir. Parmi les peuples, personne n'était avec moi. Oui, je les ai piétinés dans ma colère et je les ai piétinés dans ma colère. Leur sang est répandu sur mes vêtements, et j'ai taché tous mes vêtements.
4 Pakuti ndinatsimikiza mu mtima mwanga kuti lafika tsiku lolipsira anthu anga; ndipo chaka cha kuwomboledwa kwanga chafika.
Car le jour de la vengeance était dans mon cœur, et l'année de mes rachetés est arrivée.
5 Ndinayangʼana ndipo panalibe munthu wondithandiza. Ndinadabwa kwambiri kuti panalibe wondichirikiza; choncho ndinapambana ndi mphamvu zanga, ndipo mkwiyo wanga unandilimbitsa.
J'ai regardé, et il n'y avait personne pour m'aider; et je m'étonne qu'il n'y ait personne à soutenir. C'est donc mon propre bras qui m'a sauvé. Ma propre colère m'a soutenu.
6 Ndinapondereza mitundu ya anthu ndili wokwiya; ndipo ndinawasakaza ndipo ndinathira magazi awo pansi.”
J'ai foulé les peuples dans ma colère. et je les ai rendus ivres de ma colère. J'ai répandu leur sang sur la terre. »
7 Ndidzafotokoza za kukoma mtima kwa Yehova, ntchito zimene Iye ayenera kutamandidwa. Ndidzatamanda Yehova chifukwa cha zonse zimene watichitira. Inde, mwa chifundo ndi kukoma mtima kwake Yehova wachitira nyumba ya Israeli zinthu zabwino zambiri.
Je raconterai les bontés de l'Éternel. et les louanges de Yahvé, selon tout ce que Yahvé nous a donné, et la grande bonté envers la maison d'Israël, qu'il leur a donné selon sa miséricorde, et selon la multitude de ses bontés.
8 Yehova anati, “Ndithu awa ndi anthu anga, ana anga amene sadzandinyenga Ine.” Choncho anawapulumutsa.
Car il a dit: « Certainement, ils sont mon peuple, des enfants qui ne commettront pas de fautes; » Il est donc devenu leur Sauveur.
9 Iyenso anasautsidwa mʼmasautso awo onse, ndipo mngelo wochokera kwa Iye anawapulumutsa. Mwa chikondi ndi chifundo chake iye anawapulumutsa, anawanyamula ndikuwatenga kuyambira kale lomwe.
Dans toute leur affliction, il a été affligé, et l'ange de sa présence les a sauvés. Dans son amour et dans sa pitié, il les a rachetés. Il les a portés, et les a portées tous les jours d'autrefois.
10 Komabe iwo anawukira ndi kumvetsa chisoni Mzimu Woyera. Motero Yehova anatembenuka nakhala mdani wawo ndipo Iye mwini anamenyana nawo.
Mais ils se sont rebellés et ont attristé son Saint-Esprit. Il s'est donc retourné et est devenu leur ennemi, et il a lui-même combattu contre eux.
11 Pamenepo anthu ake anakumbukira masiku amakedzana, masiku a Mose mtumiki wake; ndipo anafunsa kuti, “Ali kuti Yehova amene anawawolotsa pa nyanja, pamodzi ndi Mose mʼbusa wawo? Ali kuti Iye amene anayika Mzimu Woyera pakati pawo?
Et il se souvint des jours d'autrefois, Moïse et son peuple, en disant, « Où est celui qui les a fait remonter de la mer avec les bergers de son troupeau? ". Où est celui qui a mis son Saint-Esprit au milieu d'eux? »
12 Ali kuti amene anachita zinthu zodabwitsa ndi mphamvu zake zazikulu kudzera mwa Mose? Ali kuti amene anagawa madzi pa nyanja anthu ake akuona, kuti dzina lake limveke mpaka muyaya,
Qui a fait en sorte que son bras glorieux soit à la droite de Moïse? Qui a divisé les eaux devant eux, pour se faire un nom éternel?
13 amene anawayendetsa pa nyanja yozama? Monga kavalo woyendayenda mʼchipululu, iwo sanapunthwe;
qui les a conduits à travers les profondeurs, comme un cheval dans le désert, pour qu'ils ne trébuchent pas?
14 Mzimu Woyera unawapumulitsa ngati mmene ngʼombe zimapumulira. Umu ndi mmene Inu munatsogolera anthu anu kuti dzina lanu lilemekezeke.”
Comme le bétail qui descend dans la vallée, L'Esprit de Yahvé les a fait se reposer. Vous avez donc conduit votre peuple pour vous faire un nom glorieux.
15 Inu Yehova amene muli kumwambako, pa mpando wanu wolemekezeka, wopatulika ndi waulemerero, tiyangʼaneni ife. Kodi changu chanu ndi mphamvu zanu zili kuti? Simukutionetsanso kukoma mtima kwanu ndi chifundo chanu.
Regardez du haut du ciel, et voir depuis la demeure de ta sainteté et de ta gloire. Où sont votre zèle et vos actes puissants? Le désir ardent de ton cœur et ta compassion sont retenus envers moi.
16 Koma Inu ndinu Atate athu, ngakhale Abrahamu satidziwa kapena Israeli kutivomereza ife; Inu Yehova, ndinu Atate athu, kuyambira kale dzina lanu ndinu Mpulumutsi wathu.
Car tu es notre Père, même si Abraham ne nous connaît pas, et Israël ne nous reconnaît pas. Toi, Yahvé, tu es notre Père. Notre Rédempteur de toujours est ton nom.
17 Chifukwa chiyani, Inu Yehova, mukutisocheretsa pa njira zanu? Bwanji mukutilola kuti tikhale owuma mitima kotero kuti sitikukuopaninso? Bwererani chifukwa cha atumiki anu; mafuko a anthu amene ali cholowa chanu.
O Yahvé, pourquoi nous fais-tu errer loin de tes voies? et endurcir notre cœur face à ta crainte? Reviens pour le bien de tes serviteurs, les tribus de votre héritage.
18 Anthu anu atangokhala pa malo anu opatulika pa kanthawi kochepa, adani athu anasakaza malo anu opatulika.
Ton peuple saint ne l'a possédé que peu de temps. Nos adversaires ont foulé ton sanctuaire.
19 Ife tili ngati anthu amene simunawalamulirepo ngati iwo amene sanakhalepo anthu anu.
Noussommes devenus comme ceux sur lesquels tu n'as jamais régné, comme ceux qui n'ont pas été appelés par ton nom.

< Yesaya 63 >