< Yesaya 63 >

1 Kodi ndani uyo akubwera kuchokera ku Edomu, atavala zovala za ku Bozira za madontho ofiira? Kodi uyu ndani, amene wavala zovala zokongola, akuyenda mwa mphamvu zake? “Ndi Ineyo, woyankhula zachilungamo ndiponso wamphamvu zopulumutsa.”
Kdož jest to, ješto se béře z Edom, v ubroceném rouše z Bozra, ten ozdobený rouchem svým, kráčeje u velikosti síly své? Jáť jsem, kterýž mluvím spravedlivě, dostatečný k vysvobození.
2 Nanga bwanji zovala zanu zili psuu, ngati za munthu wofinya mphesa?
Proč jest červené roucho tvé, a oděv tvůj jako toho, kterýž tlačí v presu?
3 “Ndapondereza ndekha anthu a mitundu ina ngati mphesa, palibe ndi mmodzi yemwe anali nane. Ndinawapondereza ndili wokwiya ndipo ndinawapondereza ndili ndi ukali; magazi awo anadothera pa zovala zanga, ndipo zovala zanga zonse zinathimbirira.
Pres jsem tlačil sám, aniž kdo z lidí byl se mnou. Tlačil jsem nepřátely v hněvě svém, a pošlapal jsem je v prchlivosti své, až stříkala krev i nejsilnějších jejich na roucho mé, a tak všecken oděv svůj zkálel jsem.
4 Pakuti ndinatsimikiza mu mtima mwanga kuti lafika tsiku lolipsira anthu anga; ndipo chaka cha kuwomboledwa kwanga chafika.
Den zajisté pomsty v srdci mém, a léto, v němž mají vykoupeni býti moji, přišlo.
5 Ndinayangʼana ndipo panalibe munthu wondithandiza. Ndinadabwa kwambiri kuti panalibe wondichirikiza; choncho ndinapambana ndi mphamvu zanga, ndipo mkwiyo wanga unandilimbitsa.
Když jsem pak viděl, že není žádného spomocníka, až jsem se užasl, že žádného nebylo, kdo by podpíral. A protož mi vysvobození způsobilo rámě mé, a prchlivost má, ta mne podepřela.
6 Ndinapondereza mitundu ya anthu ndili wokwiya; ndipo ndinawasakaza ndipo ndinathira magazi awo pansi.”
I pošlapal jsem národy v hněvě svém, a opojil jsem je prchlivostí svou, a porazil jsem na zem nejsilnější reky jejich.
7 Ndidzafotokoza za kukoma mtima kwa Yehova, ntchito zimene Iye ayenera kutamandidwa. Ndidzatamanda Yehova chifukwa cha zonse zimene watichitira. Inde, mwa chifundo ndi kukoma mtima kwake Yehova wachitira nyumba ya Israeli zinthu zabwino zambiri.
Milosrdenství Hospodinova připomínati budu, a chvály Hospodinovy ze všeho, což učinil nám Hospodin, i množství dobroty, kteréž dokazoval k domu Izraelskému z veliké lítosti své, a z velikého milosrdenství svého.
8 Yehova anati, “Ndithu awa ndi anthu anga, ana anga amene sadzandinyenga Ine.” Choncho anawapulumutsa.
Nebo řekl: Vždyť jsou lidem mým, jsou synové, neučiníť mi nevěrně. A protož byl jejich spasitelem.
9 Iyenso anasautsidwa mʼmasautso awo onse, ndipo mngelo wochokera kwa Iye anawapulumutsa. Mwa chikondi ndi chifundo chake iye anawapulumutsa, anawanyamula ndikuwatenga kuyambira kale lomwe.
Ve všelikém ssoužení jejich i on měl ssoužení, a anděl přístojící jemu vysvobozval je. Z milování svého a z lítosti své on sám vykoupil je, a pěstoval je, i nosil je po všecky dny věků.
10 Komabe iwo anawukira ndi kumvetsa chisoni Mzimu Woyera. Motero Yehova anatembenuka nakhala mdani wawo ndipo Iye mwini anamenyana nawo.
Ale oni zpurní byli, a zarmucovali Ducha svatého jeho; pročež obrátil se jim v nepřítele, a sám bojoval proti nim.
11 Pamenepo anthu ake anakumbukira masiku amakedzana, masiku a Mose mtumiki wake; ndipo anafunsa kuti, “Ali kuti Yehova amene anawawolotsa pa nyanja, pamodzi ndi Mose mʼbusa wawo? Ali kuti Iye amene anayika Mzimu Woyera pakati pawo?
I rozpomínal se lid jeho na dny starodávní, i na Mojžíše: Kdež jest ten, kterýž je vyvedl z moře s pastýřem stáda svého? Kde jest ten, kterýž položil u prostřed něho Ducha svatého svého?
12 Ali kuti amene anachita zinthu zodabwitsa ndi mphamvu zake zazikulu kudzera mwa Mose? Ali kuti amene anagawa madzi pa nyanja anthu ake akuona, kuti dzina lake limveke mpaka muyaya,
Kterýž je vedl ramenem velebnosti své po pravici Mojžíšově, kterýž rozdělil vody před nimi, aby sobě způsobil jméno věčné,
13 amene anawayendetsa pa nyanja yozama? Monga kavalo woyendayenda mʼchipululu, iwo sanapunthwe;
Kterýž je provedl skrze hlubiny jako koně po poušti, ani se nepoklesli.
14 Mzimu Woyera unawapumulitsa ngati mmene ngʼombe zimapumulira. Umu ndi mmene Inu munatsogolera anthu anu kuti dzina lanu lilemekezeke.”
Jako když hovádko do údolí sstupuje, tak Duch Hospodinův poznenáhlu vedl z nich každého. Tak jsi vedl lid svůj, abys sobě způsobil jméno slavné.
15 Inu Yehova amene muli kumwambako, pa mpando wanu wolemekezeka, wopatulika ndi waulemerero, tiyangʼaneni ife. Kodi changu chanu ndi mphamvu zanu zili kuti? Simukutionetsanso kukoma mtima kwanu ndi chifundo chanu.
Popatřiž s nebe, a pohleď z příbytku svatosti své a okrasy své. Kdež jest horlivost tvá a veliká síla tvá? Kde množství milosrdenství tvých a slitování tvých? Mně-liž se zadržovati budou?
16 Koma Inu ndinu Atate athu, ngakhale Abrahamu satidziwa kapena Israeli kutivomereza ife; Inu Yehova, ndinu Atate athu, kuyambira kale dzina lanu ndinu Mpulumutsi wathu.
Ty jsi zajisté otec náš; nebo Abraham nic neví o nás, a Izrael nezná nás. Ty jsi, Hospodine, otec náš, vykupitel náš, toť jest od věčnosti jméno tvé.
17 Chifukwa chiyani, Inu Yehova, mukutisocheretsa pa njira zanu? Bwanji mukutilola kuti tikhale owuma mitima kotero kuti sitikukuopaninso? Bwererani chifukwa cha atumiki anu; mafuko a anthu amene ali cholowa chanu.
Pročež jsi nám dal zblouditi, Hospodine, od cest svých, zatvrdil jsi srdce naše, abychom se nebáli tebe? Navratiž se zase pro služebníky své, pokolení dědictví svého.
18 Anthu anu atangokhala pa malo anu opatulika pa kanthawi kochepa, adani athu anasakaza malo anu opatulika.
Nejšpatnější vládne lidem svatosti tvé, nepřátelé naši pošlapali svatyni tvou.
19 Ife tili ngati anthu amene simunawalamulirepo ngati iwo amene sanakhalepo anthu anu.
My tvoji jsme od věků; nad nimi jsi nikdy nepanoval, aniž nad nimi jméno tvé vzýváno jest.

< Yesaya 63 >