< Yesaya 62 >

1 Chifukwa chokonda Ziyoni sindidzakhala chete, chifukwa chokonda Yerusalemu sindidzakhala chete, mpaka chilungamo chake chitaoneka poyera ngati kuwala, ndi chipulumutso chake chitaoneka ngati sakali yoyaka.
Не буду мовчати я ради Сіо́ну, і ради Єрусалиму не буду спокі́йний, аж поки не ви́йде, як ся́йво, його праведність, а спасі́ння його — як горю́чий світи́льник!
2 Mitundu ya anthu idzaona iwe utapambana pa nkhondo ndipo mafumu onse adzaona ulemerero wako. Adzakuyitanira dzina latsopano limene adzakupatse ndi Yehova.
І побачать наро́ди твою праведність, а славу твою — всі царі́, і йме́нням нови́м будуть звати тебе, що уста Господні докла́дно озна́чать його́.
3 Udzakhala ngati chipewa chaulemerero mʼdzanja la Yehova, ndi ngati nduwira yaufumu mʼdzanja la Mulungu wako.
І ти станеш короною слави в Господній руці й діяде́мою царства в долоні Бога свого!
4 Sadzakutchanso “Wosiyidwa,” ndipo dziko lako silidzatchedwanso “Chipululu.” Koma dzina lako latsopano lidzakhala “Ndakondwera naye.” Ndipo dziko lako lidzatchedwa “Wokwatiwa.” Chifukwa Yehova akukondwera nawe, ndipo adzakhala ngati mwamuna wa dziko lako.
Вже не скажуть на тебе „поки́нута“, а на край твій не будуть казати вже „пустиня“, бо тебе будуть кли́кати „в ній моя втіха“, а край твій „замі́жня“, бо Господь пожада́є тебе, і твій край буде взятий за жінку!
5 Monga mnyamata amakwatira namwali, momwenso mmisiri wodzakumanga adzakukwatira; monga mkwati amakondwera ndi mkwatibwi, chonchonso Mulungu adzakondwera nawe.
Як юна́к бере панну за жінку, так з тобою одру́житься Сам Будівни́чий, і як ті́шиться той молоди́й нарече́ною, так раді́тиме Бог твій тобо́ю!
6 Iwe Yerusalemu, pa malinga ako ndayikapo alonda; sadzakhala chete usana kapena usiku. Inu amene mumakumbutsa Yehova za malonjezo ake musapumule.
На му́рах твоїх, Єрусалиме, Я поставив сторо́жу, — ніко́ли не буде мовчати вона цілий день та всю ніч. Ви, хто пригадує Господа, не замо́вкніть, —
7 Musamupatse mpata wopuma mpaka atakhazikitsa Yerusalemu kukhala mzinda umene dziko lapansi lidzawutamande.
і перед Ним не вмовкайте, аж поки не змі́цнить, і аж поки не вчи́нить Він Єрусалима за славу Свою́ на землі!
8 Yehova analumbira atakweza dzanja lake. Anati, “Sindidzaperekanso tirigu wako kuti akhale chakudya cha adani ako, ndipo alendo sadzamwanso vinyo wako watsopano pakuti unamuvutikira.
Господь присягну́в був Своєю прави́цею й поту́жним раме́ном Своїм: Направду, не дам уже збі́жжя твого ворога́м твоїм, і пити не будуть чужи́нці твого виногра́дного со́ку, що ти працюва́в біля нього!
9 Koma amene amakakolola ndiwo amene adzadye buledi ndi kutamanda Yehova, ndipo amene amasonkhanitsa pamodzi mphesa ndiwo amene adzamwe vinyo mʼmabwalo a Nyumba yanga.”
Бо ті, хто збирає його́, будуть їсти його та й хвали́тимуть Господа, і ті, хто грома́дить його́, будуть пити його на подві́р'ях святині Моєї!
10 Tulukani, dutsani pa zipata! Konzerani anthu njira. Lambulani, lambulani msewu waukulu! Chotsani miyala. Kwezani mbendera kuti mitundu ya anthu izione.
Проходьте, проходьте ви бра́мами, чи́стьте доро́гу наро́дові! Будуйте доро́гу, будуйте дорогу, дорогу ту биту, очи́стьте від ка́меня, підіймі́ть над наро́дами пра́пора!
11 Yehova walengeza ku dziko lonse lapansi kuti, Awuzeni anthu a ku Yerusalemu kuti, “Taonani, chipulumutso chanu chikubwera; Yehova akubwera ndi mphotho yake akubwera nazo zokuyenerani.”
Ось звіщає Господь аж до кра́ю землі: Розкажі́те сіо́нській дочці́: Ось прихо́дить Спасі́ння твоє, ось із Ним нагоро́да Його, і заплата Його перед Ним!
12 Iwo adzatchedwa Anthu Opatulika, owomboledwa a Yehova; ndipo adzakutchani “Okondwa a Yehova” “Mzinda umene Yehova sanawusiye.”
І будуть їх звати наро́дом святим, вику́пленцями Господа, а на тебе закличуть „жада́на“, незали́шене місто!

< Yesaya 62 >