< Yesaya 62 >

1 Chifukwa chokonda Ziyoni sindidzakhala chete, chifukwa chokonda Yerusalemu sindidzakhala chete, mpaka chilungamo chake chitaoneka poyera ngati kuwala, ndi chipulumutso chake chitaoneka ngati sakali yoyaka.
Pour l'amour de Sion, je ne me tairai pas, et à cause de Jérusalem, je ne me reposerai pas, jusqu'à ce que sa droiture brille comme l'aube, et son salut comme une lampe allumée.
2 Mitundu ya anthu idzaona iwe utapambana pa nkhondo ndipo mafumu onse adzaona ulemerero wako. Adzakuyitanira dzina latsopano limene adzakupatse ndi Yehova.
Les nations verront ta justice, et tous les rois ta gloire. Vous serez appelé par un nouveau nom, que la bouche de Yahvé nommera.
3 Udzakhala ngati chipewa chaulemerero mʼdzanja la Yehova, ndi ngati nduwira yaufumu mʼdzanja la Mulungu wako.
Tu seras aussi une couronne de beauté dans la main de Yahvé, et un diadème royal dans la main de ton Dieu.
4 Sadzakutchanso “Wosiyidwa,” ndipo dziko lako silidzatchedwanso “Chipululu.” Koma dzina lako latsopano lidzakhala “Ndakondwera naye.” Ndipo dziko lako lidzatchedwa “Wokwatiwa.” Chifukwa Yehova akukondwera nawe, ndipo adzakhala ngati mwamuna wa dziko lako.
On ne vous appellera plus « abandonnés », et ton pays ne sera plus appelé Désolation; mais on t'appellera Hephzibah, et ton pays Beulah; car Yahvé prend plaisir à te voir, et votre terre sera mariée.
5 Monga mnyamata amakwatira namwali, momwenso mmisiri wodzakumanga adzakukwatira; monga mkwati amakondwera ndi mkwatibwi, chonchonso Mulungu adzakondwera nawe.
Car comme un jeune homme épouse une vierge, pour que vos fils vous épousent. Comme un jeune marié se réjouit de sa fiancée, ainsi ton Dieu se réjouira à ton sujet.
6 Iwe Yerusalemu, pa malinga ako ndayikapo alonda; sadzakhala chete usana kapena usiku. Inu amene mumakumbutsa Yehova za malonjezo ake musapumule.
J'ai placé des sentinelles sur tes murs, Jérusalem. Ils ne seront jamais silencieux, ni le jour ni la nuit. Vous qui invoquez Yahvé, ne prenez pas de repos,
7 Musamupatse mpata wopuma mpaka atakhazikitsa Yerusalemu kukhala mzinda umene dziko lapansi lidzawutamande.
et ne lui donne aucun repos jusqu'à ce qu'il s'établisse, et jusqu'à ce qu'il fasse de Jérusalem une louange sur la terre.
8 Yehova analumbira atakweza dzanja lake. Anati, “Sindidzaperekanso tirigu wako kuti akhale chakudya cha adani ako, ndipo alendo sadzamwanso vinyo wako watsopano pakuti unamuvutikira.
Yahvé l'a juré par sa droite, et par le bras de sa force, « Je ne donnerai plus votre grain en pâture à vos ennemis, et les étrangers ne boiront pas le vin nouveau pour lequel vous avez travaillé,
9 Koma amene amakakolola ndiwo amene adzadye buledi ndi kutamanda Yehova, ndipo amene amasonkhanitsa pamodzi mphesa ndiwo amene adzamwe vinyo mʼmabwalo a Nyumba yanga.”
mais ceux qui l'auront récoltée la mangeront et loueront Yahvé. Ceux qui l'auront recueillie la boiront dans les parvis de mon sanctuaire. »
10 Tulukani, dutsani pa zipata! Konzerani anthu njira. Lambulani, lambulani msewu waukulu! Chotsani miyala. Kwezani mbendera kuti mitundu ya anthu izione.
Passez, passez les portes! Préparez le chemin du peuple! Construisez, construisez l'autoroute! Rassemblez les pierres! Levez une bannière pour les peuples.
11 Yehova walengeza ku dziko lonse lapansi kuti, Awuzeni anthu a ku Yerusalemu kuti, “Taonani, chipulumutso chanu chikubwera; Yehova akubwera ndi mphotho yake akubwera nazo zokuyenerani.”
Voici que Yahvé proclame jusqu'aux extrémités de la terre: « Dis à la fille de Sion, Voici que votre salut arrive! Voici, sa récompense est avec lui, et sa récompense devant lui! »
12 Iwo adzatchedwa Anthu Opatulika, owomboledwa a Yehova; ndipo adzakutchani “Okondwa a Yehova” “Mzinda umene Yehova sanawusiye.”
Ils les appelleront « le peuple saint », Les rachetés de Yahvé ». Vous serez appelé « Recherché », Une ville non abandonnée ».

< Yesaya 62 >