< Yesaya 62 >

1 Chifukwa chokonda Ziyoni sindidzakhala chete, chifukwa chokonda Yerusalemu sindidzakhala chete, mpaka chilungamo chake chitaoneka poyera ngati kuwala, ndi chipulumutso chake chitaoneka ngati sakali yoyaka.
For Zion's sake I will not keep silence, And for Jerusalem's sake I will not rest, Until her deliverance break forth like the shining light, And her salvation like a blazing torch.
2 Mitundu ya anthu idzaona iwe utapambana pa nkhondo ndipo mafumu onse adzaona ulemerero wako. Adzakuyitanira dzina latsopano limene adzakupatse ndi Yehova.
Then shall the nations see thy prosperity, And all the kings thy glory; Thou shalt be called by a new name, Which the mouth of Jehovah shall give thee.
3 Udzakhala ngati chipewa chaulemerero mʼdzanja la Yehova, ndi ngati nduwira yaufumu mʼdzanja la Mulungu wako.
Thou shalt be a beautiful crown in the hand of Jehovah, A royal diadem in the hand of thy God.
4 Sadzakutchanso “Wosiyidwa,” ndipo dziko lako silidzatchedwanso “Chipululu.” Koma dzina lako latsopano lidzakhala “Ndakondwera naye.” Ndipo dziko lako lidzatchedwa “Wokwatiwa.” Chifukwa Yehova akukondwera nawe, ndipo adzakhala ngati mwamuna wa dziko lako.
No more shalt thou be called the Desolate, And thy land, the Forsaken. But thou shall be named My-delight-is-in-her. And thy land the wedded Matron. For Jehovah shall delight in thee, And thy land shall be married.
5 Monga mnyamata amakwatira namwali, momwenso mmisiri wodzakumanga adzakukwatira; monga mkwati amakondwera ndi mkwatibwi, chonchonso Mulungu adzakondwera nawe.
For as a young man weddeth a virgin. So shall thy children wed thee. And as a bridegroom rejoiceth in his bride, So shall thy God rejoice in thee.
6 Iwe Yerusalemu, pa malinga ako ndayikapo alonda; sadzakhala chete usana kapena usiku. Inu amene mumakumbutsa Yehova za malonjezo ake musapumule.
Upon thy walls, O Jerusalem, have I set watchmen; All the day, and all the night, shall they not keep silence; O ye that praise Jehovah, keep not silence,
7 Musamupatse mpata wopuma mpaka atakhazikitsa Yerusalemu kukhala mzinda umene dziko lapansi lidzawutamande.
And give him no rest, Until he establish Jerusalem, and make her a praise in the earth!
8 Yehova analumbira atakweza dzanja lake. Anati, “Sindidzaperekanso tirigu wako kuti akhale chakudya cha adani ako, ndipo alendo sadzamwanso vinyo wako watsopano pakuti unamuvutikira.
Jehovah hath sworn by his right hand, and his mighty arm: No more will I give thy corn to be food for thine enemies, Nor shall the sons of the stranger drink thy wine, for which thou hast labored.
9 Koma amene amakakolola ndiwo amene adzadye buledi ndi kutamanda Yehova, ndipo amene amasonkhanitsa pamodzi mphesa ndiwo amene adzamwe vinyo mʼmabwalo a Nyumba yanga.”
But they that reap the harvest shall eat it, And praise Jehovah; And they that gather the vintage shall drink it, In my holy comets.
10 Tulukani, dutsani pa zipata! Konzerani anthu njira. Lambulani, lambulani msewu waukulu! Chotsani miyala. Kwezani mbendera kuti mitundu ya anthu izione.
Pass ye, pass ye through the gates; Prepare the way for the people; Cast ye up, cast ye up the highway, Clear it from the stones; Lift up on high a standard for the tribes!
11 Yehova walengeza ku dziko lonse lapansi kuti, Awuzeni anthu a ku Yerusalemu kuti, “Taonani, chipulumutso chanu chikubwera; Yehova akubwera ndi mphotho yake akubwera nazo zokuyenerani.”
Behold, Jehovah proclaimeth to the end of the earth: “Say ye to the daughter of Zion, Behold, thy Deliverer cometh! Behold, his reward is with him, and his recompense before him!”
12 Iwo adzatchedwa Anthu Opatulika, owomboledwa a Yehova; ndipo adzakutchani “Okondwa a Yehova” “Mzinda umene Yehova sanawusiye.”
They shall be called, The holy people, The redeemed of Jehovah. And thou shalt be called, The Sought out, The Not forsaken City.

< Yesaya 62 >