< Yesaya 62 >
1 Chifukwa chokonda Ziyoni sindidzakhala chete, chifukwa chokonda Yerusalemu sindidzakhala chete, mpaka chilungamo chake chitaoneka poyera ngati kuwala, ndi chipulumutso chake chitaoneka ngati sakali yoyaka.
For Zion’s sake I am not silent, And for Jerusalem’s sake I do not rest, Until her righteousness goes out as brightness, And her salvation burns as a torch.
2 Mitundu ya anthu idzaona iwe utapambana pa nkhondo ndipo mafumu onse adzaona ulemerero wako. Adzakuyitanira dzina latsopano limene adzakupatse ndi Yehova.
And nations have seen your righteousness, And all kings your glory, And He is giving a new name to you, That the mouth of YHWH defines.
3 Udzakhala ngati chipewa chaulemerero mʼdzanja la Yehova, ndi ngati nduwira yaufumu mʼdzanja la Mulungu wako.
And you have been a crown of beauty in the hand of YHWH, And a turban of royalty in the hand of your God,
4 Sadzakutchanso “Wosiyidwa,” ndipo dziko lako silidzatchedwanso “Chipululu.” Koma dzina lako latsopano lidzakhala “Ndakondwera naye.” Ndipo dziko lako lidzatchedwa “Wokwatiwa.” Chifukwa Yehova akukondwera nawe, ndipo adzakhala ngati mwamuna wa dziko lako.
It is not said of you anymore, “Forsaken!” And of your land it is not said anymore, “Desolate,” For to you is cried, “My delight [is] in her,” And to your land, “Married,” For YHWH has delighted in you, And your land is married.
5 Monga mnyamata amakwatira namwali, momwenso mmisiri wodzakumanga adzakukwatira; monga mkwati amakondwera ndi mkwatibwi, chonchonso Mulungu adzakondwera nawe.
For a young man marries a virgin, Your builders marry you, With the joy of a bridegroom over a bride, Your God rejoices over you.
6 Iwe Yerusalemu, pa malinga ako ndayikapo alonda; sadzakhala chete usana kapena usiku. Inu amene mumakumbutsa Yehova za malonjezo ake musapumule.
“On your walls, O Jerusalem, I have appointed watchmen, All the day and all the night, Continually, they are not silent.” O you remembering YHWH, do not keep silence for yourselves,
7 Musamupatse mpata wopuma mpaka atakhazikitsa Yerusalemu kukhala mzinda umene dziko lapansi lidzawutamande.
And do not give silence to Him, Until He establishes, and until He makes Jerusalem a praise in the earth.
8 Yehova analumbira atakweza dzanja lake. Anati, “Sindidzaperekanso tirigu wako kuti akhale chakudya cha adani ako, ndipo alendo sadzamwanso vinyo wako watsopano pakuti unamuvutikira.
YHWH has sworn by His right hand, Even by the arm of His strength: “I do not give your grain anymore [as] food for your enemies, Nor do sons of a stranger drink your new wine, For which you have labored.
9 Koma amene amakakolola ndiwo amene adzadye buledi ndi kutamanda Yehova, ndipo amene amasonkhanitsa pamodzi mphesa ndiwo amene adzamwe vinyo mʼmabwalo a Nyumba yanga.”
For those gathering it eat it, and have praised YHWH, And those collecting it drink it in My holy courts.”
10 Tulukani, dutsani pa zipata! Konzerani anthu njira. Lambulani, lambulani msewu waukulu! Chotsani miyala. Kwezani mbendera kuti mitundu ya anthu izione.
Pass on, pass on through the gates, Prepare the way of the people, Raise up, raise up the highway, clear it from stones, Lift up an ensign over the peoples.
11 Yehova walengeza ku dziko lonse lapansi kuti, Awuzeni anthu a ku Yerusalemu kuti, “Taonani, chipulumutso chanu chikubwera; Yehova akubwera ndi mphotho yake akubwera nazo zokuyenerani.”
Behold, YHWH has proclaimed to the end of the earth: “Say to the daughter of Zion, Behold, your salvation has come, Behold, His hire [is] with Him, And His wage before Him.”
12 Iwo adzatchedwa Anthu Opatulika, owomboledwa a Yehova; ndipo adzakutchani “Okondwa a Yehova” “Mzinda umene Yehova sanawusiye.”
And they have cried to them, “The People of the Holy One! The Redeemed of YHWH!” Indeed, to you is called, “The sought out one, a city not forsaken!”