< Yesaya 62 >

1 Chifukwa chokonda Ziyoni sindidzakhala chete, chifukwa chokonda Yerusalemu sindidzakhala chete, mpaka chilungamo chake chitaoneka poyera ngati kuwala, ndi chipulumutso chake chitaoneka ngati sakali yoyaka.
For Zions Skyld vil jeg ikke tie, og for Jerusalems Skyld vil jeg ikke være stille, indtil dens Retfærdighed gaar frem som Straaleglans og dens Frelse som et Blus, der brænder.
2 Mitundu ya anthu idzaona iwe utapambana pa nkhondo ndipo mafumu onse adzaona ulemerero wako. Adzakuyitanira dzina latsopano limene adzakupatse ndi Yehova.
Og Hedningerne skulle se din Retfærdighed og alle Konger din Herlighed; og du skal kaldes med et nyt Navn, hvilket Herrens Mund skal nævne.
3 Udzakhala ngati chipewa chaulemerero mʼdzanja la Yehova, ndi ngati nduwira yaufumu mʼdzanja la Mulungu wako.
Og du skal være en dejlig Krone i Herrens Haand og et kongeligt Hovedsmykke i din Guds Haand.
4 Sadzakutchanso “Wosiyidwa,” ndipo dziko lako silidzatchedwanso “Chipululu.” Koma dzina lako latsopano lidzakhala “Ndakondwera naye.” Ndipo dziko lako lidzatchedwa “Wokwatiwa.” Chifukwa Yehova akukondwera nawe, ndipo adzakhala ngati mwamuna wa dziko lako.
Man skal ikke ydermere kalde dig „den forladte‟, ej heller skal dit Land ydermere kaldes „det ødelagte‟; men du skal kaldes „min Lyst er i det‟, og dit Land skal kaldes „Ægtehustruen‟; thi Herren har Lyst til dig, og dit Land skal faa sin Ægteherre.
5 Monga mnyamata amakwatira namwali, momwenso mmisiri wodzakumanga adzakukwatira; monga mkwati amakondwera ndi mkwatibwi, chonchonso Mulungu adzakondwera nawe.
Thi som en Ungkarl ægter en Jomfru, saa skulle dine Børn holde Ægteskab med dig; og som en Brudgom glæder sig ved Bruden, saa skal din Gud glæde sig ved dig.
6 Iwe Yerusalemu, pa malinga ako ndayikapo alonda; sadzakhala chete usana kapena usiku. Inu amene mumakumbutsa Yehova za malonjezo ake musapumule.
Paa dine Mure, o Jerusalem! har jeg beskikket Vægtere, de skulle aldrig tie den ganske Dag eller den ganske Nat; I, som paaminde om Herren, tier ikke!
7 Musamupatse mpata wopuma mpaka atakhazikitsa Yerusalemu kukhala mzinda umene dziko lapansi lidzawutamande.
Og lader ham ingen Ro, indtil han faar grundlagt og gjort Jerusalem til Lovprisning paa Jorden.
8 Yehova analumbira atakweza dzanja lake. Anati, “Sindidzaperekanso tirigu wako kuti akhale chakudya cha adani ako, ndipo alendo sadzamwanso vinyo wako watsopano pakuti unamuvutikira.
Herren svor ved sin højre Haand og ved sin Magts Arm: Jeg vil ikke mere give dine Fjender dit Korn til Spise, ej heller skulle Udlændinge drikke din Vin, som du har arbejdet for.
9 Koma amene amakakolola ndiwo amene adzadye buledi ndi kutamanda Yehova, ndipo amene amasonkhanitsa pamodzi mphesa ndiwo amene adzamwe vinyo mʼmabwalo a Nyumba yanga.”
Men de, som have indsanket hint, skulle æde det og love Herren; og de, som have indhøstet denne, skulle drikke den i min Helligdoms Forgaarde.
10 Tulukani, dutsani pa zipata! Konzerani anthu njira. Lambulani, lambulani msewu waukulu! Chotsani miyala. Kwezani mbendera kuti mitundu ya anthu izione.
Drager frem, drager frem igennem Portene, bereder Folket Vej; baner, ja baner Vej, sanker Stenene deraf, opløfter et Banner for Folkene!
11 Yehova walengeza ku dziko lonse lapansi kuti, Awuzeni anthu a ku Yerusalemu kuti, “Taonani, chipulumutso chanu chikubwera; Yehova akubwera ndi mphotho yake akubwera nazo zokuyenerani.”
Se, Herren har ladet det høre til Jordens Ende; siger til Zions Datter: Se, din Frelse kommer; se, hans Løn er med ham, og Gengældelsen fra ham er for hans Ansigt.
12 Iwo adzatchedwa Anthu Opatulika, owomboledwa a Yehova; ndipo adzakutchani “Okondwa a Yehova” “Mzinda umene Yehova sanawusiye.”
Og man skal kalde dem et helligt Folk, Herrens genløste; og dig skal man kalde „den søgte Stad, den ej forladte‟.

< Yesaya 62 >