< Yesaya 61 >

1 Mzimu wa Ambuye Yehova uli pa ine, chifukwa Yehova wandidzoza kuti ndilalikire uthenga wabwino kwa anthu osauka. Wandituma kuti ndikatonthoze anthu osweka mtima, ndikalengeze kwa akapolo kuti alandire ufulu ndiponso kuti ndikamasule a mʼndende.
Дух је Господа Бога на мени, јер ме Господ помаза да јављам добре гласове кроткима, посла ме да завијем рањене у срцу, да огласим заробљенима слободу и сужњима да ће им се отворити тамница.
2 Wandituma kuti ndikalengeze nthawi imene Yehova adzapulumutsa anthu ake; za tsiku limene Yehova adzalanga adani a anthu ake. Wandituma kuti ndikatonthoze olira.
Да огласим годину милости Господње и дан освете Бога нашег, да утешим све жалосне,
3 Wandituma kuti ndiwakonzere olira a ku Ziyoni, nkhata ya maluwa yokongola mʼmalo mwa phulusa, ndiwapatse mafuta achikondwerero mʼmalo mwa kulira. Ndiwapatse chovala cha matamando mʼmalo mwa mtima wopsinjika. Ndipo iwo adzatchedwa mitengo ya thundu yamphamvu yachilungamo, yoyidzala Yehova kuti Iye mwini apezemo ulemerero wake.
Да учиним жалоснима у Сиону и дам им накит место пепела, уље радости уместо жалости, одело за похвалу уместо духа тужног, да се прозову храстови правде, сад Господњи за славу Његову.
4 Adzamanganso mabwinja akale a mzinda ndipo malo amene anawonongeka kalekale aja adzakonzanso. Adzakonzanso mizinda imene inapasuka, imene yakhala yowonongeka kwa nthawi yayitali kwambiri.
И они ће сазидати давнашње пустолине, подигнуће старе развалине и поновиће градове пусте, што леже разваљени од много нараштаја.
5 Anthu achilendo adzakutumikirani; adzazidyetsa ziweto zanu; iwo adzagwira ntchito mʼminda yanu ya mpesa.
И туђини ће стајати и пасти стада ваша, и иностранци ће бити ваши орачи и виноградари.
6 Ndipo inu mudzatchedwa ansembe a Yehova, adzakutchulani kuti ndinu atumiki a Mulungu wathu. Mudzadyerera chuma cha mitundu ya anthu, ndipo mudzanyadira ulemu umene mwalandira.
А ви ћете се звати свештеници Господњи, Слуге Бога нашег говориће вам се, благо народа јешћете и славом њиховом хвалићете се.
7 Chifukwa manyazi awo anali owirikiza; ndi kuti munalandira chitonzo ndi kutukwana, adzakondwera ndi cholowa chawo, tsono adzalandira cholowa chawo cha chigawo cha dziko mowirikiza, ndipo chimwemwe chamuyaya chidzakhala chawo.
За двоструку срамоту вашу, и што се певаше: Руг је део њихов, зато ће у земљи њиховој наследити двојином и имаће вечну радост.
8 “Pakuti Ine Yehova, ndimakonda chilungamo; ndimadana ndi zakuba ndi zoyipa. Anthu anga ndidzawapatsa mphotho mokhulupirika ndikupangana nawo pangano losatha.
Јер ја Господ љубим правду и мрзим на грабеж са жртвом паљеницом, и даћу им плату уистину, и вечан завет учинићу с њима.
9 Ana awo adzakhala odziwika pakati pa mitundu ya anthu ndipo adzukulu awo adzakhala otchuka pakati pa anthu a mitundu ina. Aliyense wowaona adzazindikira kuti ndi anthu amene Yehova wawadalitsa.”
И семе ће се њихово знати у народима и натражје њихово међу племенима; ко их год види познаће их да су семе које је благословио Господ.
10 Ine ndikusangalala kwambiri chifukwa cha Yehova; moyo wanga ukukondwera chifukwa cha Mulungu wanga. Pakuti Iye wandiveka zovala zachipulumutso, ndipo wandiveka mkanjo wachilungamo. Zili ngati mkwati wovala nkhata ya maluwa mʼkhosi mwake, ndiponso ngati mkwatibwi wovala mikanda yamtengowapatali.
Веома ћу се радовати у Господу, и душа ће се моја веселити у Богу мом, јер ме обуче у хаљине спасења и плаштем правде огрте ме, као кад женик намести накит и као кад се невеста украси уресом својим.
11 Monga momwe nthaka imameretsa mbewu ndiponso monga munda umakulitsa mbewu zimene anadzala, momwemonso Ambuye Yehova adzaonetsa chilungamo ndi matamando pamaso pa mitundu yonse ya anthu.
Јер као што из земље расте биље и у врту ниче шта се посеје, тако ће Господ Бог учинити да никне правда и похвала пред свим народима.

< Yesaya 61 >