< Yesaya 61 >

1 Mzimu wa Ambuye Yehova uli pa ine, chifukwa Yehova wandidzoza kuti ndilalikire uthenga wabwino kwa anthu osauka. Wandituma kuti ndikatonthoze anthu osweka mtima, ndikalengeze kwa akapolo kuti alandire ufulu ndiponso kuti ndikamasule a mʼndende.
O Espírito do Senhor Yahweh está em mim, porque Yahweh me ungiu para pregar boas notícias aos humildes. Ele me enviou para amarrar o coração partido, para proclamar a liberdade aos cativos e liberação para aqueles que estão vinculados,
2 Wandituma kuti ndikalengeze nthawi imene Yehova adzapulumutsa anthu ake; za tsiku limene Yehova adzalanga adani a anthu ake. Wandituma kuti ndikatonthoze olira.
para proclamar o ano do favor de Yahweh e o dia da vingança de nosso Deus, para confortar a todos que choram,
3 Wandituma kuti ndiwakonzere olira a ku Ziyoni, nkhata ya maluwa yokongola mʼmalo mwa phulusa, ndiwapatse mafuta achikondwerero mʼmalo mwa kulira. Ndiwapatse chovala cha matamando mʼmalo mwa mtima wopsinjika. Ndipo iwo adzatchedwa mitengo ya thundu yamphamvu yachilungamo, yoyidzala Yehova kuti Iye mwini apezemo ulemerero wake.
para atender àqueles que choram em Zion, para dar a eles uma grinalda para cinzas, o óleo da alegria para o luto, a veste de louvor pelo espírito do peso, que podem ser chamadas de árvores da retidão, o plantio de Yahweh, que ele possa ser glorificado.
4 Adzamanganso mabwinja akale a mzinda ndipo malo amene anawonongeka kalekale aja adzakonzanso. Adzakonzanso mizinda imene inapasuka, imene yakhala yowonongeka kwa nthawi yayitali kwambiri.
They irá reconstruir as velhas ruínas. Eles irão erguer os antigos lugares devastados. Eles irão reparar as cidades arruinadas que têm sido devastadas por muitas gerações.
5 Anthu achilendo adzakutumikirani; adzazidyetsa ziweto zanu; iwo adzagwira ntchito mʼminda yanu ya mpesa.
Os estranhos ficarão de pé e alimentarão seus rebanhos. Os estrangeiros trabalharão seus campos e seus vinhedos.
6 Ndipo inu mudzatchedwa ansembe a Yehova, adzakutchulani kuti ndinu atumiki a Mulungu wathu. Mudzadyerera chuma cha mitundu ya anthu, ndipo mudzanyadira ulemu umene mwalandira.
Mas vocês serão chamados de sacerdotes de Yahweh. Os homens lhe chamarão de servos de nosso Deus. Você vai comer a riqueza das nações. Você se orgulhará de sua glória.
7 Chifukwa manyazi awo anali owirikiza; ndi kuti munalandira chitonzo ndi kutukwana, adzakondwera ndi cholowa chawo, tsono adzalandira cholowa chawo cha chigawo cha dziko mowirikiza, ndipo chimwemwe chamuyaya chidzakhala chawo.
Em vez de sua vergonha, você terá o dobro. Em vez de desonrar, eles se regozijarão com sua porção. Portanto, em suas terras eles possuirão o dobro. A alegria eterna será para eles.
8 “Pakuti Ine Yehova, ndimakonda chilungamo; ndimadana ndi zakuba ndi zoyipa. Anthu anga ndidzawapatsa mphotho mokhulupirika ndikupangana nawo pangano losatha.
“Para mim, Yahweh, amo a justiça. Odeio roubo e iniqüidade. Eu lhes darei sua recompensa em verdade e eu farei com eles um pacto eterno.
9 Ana awo adzakhala odziwika pakati pa mitundu ya anthu ndipo adzukulu awo adzakhala otchuka pakati pa anthu a mitundu ina. Aliyense wowaona adzazindikira kuti ndi anthu amene Yehova wawadalitsa.”
Sua descendência será conhecida entre as nações, e sua descendência entre os povos. Todos os que os vêem os reconhecerão, que eles são a progênie que Yahweh abençoou”.
10 Ine ndikusangalala kwambiri chifukwa cha Yehova; moyo wanga ukukondwera chifukwa cha Mulungu wanga. Pakuti Iye wandiveka zovala zachipulumutso, ndipo wandiveka mkanjo wachilungamo. Zili ngati mkwati wovala nkhata ya maluwa mʼkhosi mwake, ndiponso ngati mkwatibwi wovala mikanda yamtengowapatali.
Eu me regozijarei muito em Yahweh! Minha alma estará alegre em meu Deus, pois ele me vestiu com as vestes da salvação. Ele me cobriu com o manto da retidão, como um convés de noivo com uma grinalda e como uma noiva se enfeita com suas jóias.
11 Monga momwe nthaka imameretsa mbewu ndiponso monga munda umakulitsa mbewu zimene anadzala, momwemonso Ambuye Yehova adzaonetsa chilungamo ndi matamando pamaso pa mitundu yonse ya anthu.
Pois enquanto a terra produz seu rebento, e como o jardim faz brotar as coisas que nele são semeadas, Assim, o Senhor Javé fará brotar a justiça e o louvor diante de todas as nações.

< Yesaya 61 >