< Yesaya 61 >

1 Mzimu wa Ambuye Yehova uli pa ine, chifukwa Yehova wandidzoza kuti ndilalikire uthenga wabwino kwa anthu osauka. Wandituma kuti ndikatonthoze anthu osweka mtima, ndikalengeze kwa akapolo kuti alandire ufulu ndiponso kuti ndikamasule a mʼndende.
روح خداوند یهوه بر من است زیراخداوند مرا مسح کرده است تامسکینان را بشارت دهم و مرا فرستاده تا شکسته دلان را التیام بخشم و اسیران را به رستگاری ومحبوسان را به آزادی ندا کنم.۱
2 Wandituma kuti ndikalengeze nthawi imene Yehova adzapulumutsa anthu ake; za tsiku limene Yehova adzalanga adani a anthu ake. Wandituma kuti ndikatonthoze olira.
و تا از سال پسندیده خداوند و از یوم انتقام خدای ما ندانمایم و جمیع ماتمیان را تسلی بخشم.۲
3 Wandituma kuti ndiwakonzere olira a ku Ziyoni, nkhata ya maluwa yokongola mʼmalo mwa phulusa, ndiwapatse mafuta achikondwerero mʼmalo mwa kulira. Ndiwapatse chovala cha matamando mʼmalo mwa mtima wopsinjika. Ndipo iwo adzatchedwa mitengo ya thundu yamphamvu yachilungamo, yoyidzala Yehova kuti Iye mwini apezemo ulemerero wake.
تا قراردهم برای ماتمیان صهیون و به ایشان ببخشم تاجی را به عوض خاکستر و روغن شادمانی را به عوض نوحه گری و ردای تسبیح را به‌جای روح کدورت تا ایشان درختان عدالت و مغروس خداوند به جهت تمجید وی نامیده شوند.۳
4 Adzamanganso mabwinja akale a mzinda ndipo malo amene anawonongeka kalekale aja adzakonzanso. Adzakonzanso mizinda imene inapasuka, imene yakhala yowonongeka kwa nthawi yayitali kwambiri.
و ایشان خرابه های قدیم را بنا خواهند نمودو ویرانه های سلف را بر پا خواهند داشت وشهرهای خراب شده و ویرانه های دهرهای بسیار را تعمیر خواهند نمود.۴
5 Anthu achilendo adzakutumikirani; adzazidyetsa ziweto zanu; iwo adzagwira ntchito mʼminda yanu ya mpesa.
و غریبان برپاشده، غله های شما را خواهند چرانید و بیگانگان، فلاحان و باغبانان شما خواهند بود.۵
6 Ndipo inu mudzatchedwa ansembe a Yehova, adzakutchulani kuti ndinu atumiki a Mulungu wathu. Mudzadyerera chuma cha mitundu ya anthu, ndipo mudzanyadira ulemu umene mwalandira.
و شماکاهنان خداوند نامیده خواهید شد و شما را به خدام خدای ما مسمی خواهند نمود. دولت امت‌ها را خواهید خورد و در جلال ایشان فخرخواهید نمود.۶
7 Chifukwa manyazi awo anali owirikiza; ndi kuti munalandira chitonzo ndi kutukwana, adzakondwera ndi cholowa chawo, tsono adzalandira cholowa chawo cha chigawo cha dziko mowirikiza, ndipo chimwemwe chamuyaya chidzakhala chawo.
به عوض خجالت، نصیب مضاعف خواهید یافت و به عوض رسوایی ازنصیب خود مسرور خواهند شد بنابراین ایشان درزمین خود نصیب مضاعف خواهند یافت و شادی جاودانی برای ایشان خواهد بود.۷
8 “Pakuti Ine Yehova, ndimakonda chilungamo; ndimadana ndi zakuba ndi zoyipa. Anthu anga ndidzawapatsa mphotho mokhulupirika ndikupangana nawo pangano losatha.
زیرا من که یهوه هستم عدالت را دوست می‌دارم و از غارت و ستم نفرت می‌دارم و اجرت ایشان را به راستی به ایشان خواهم داد و عهد جاودانی با ایشان خواهم بست.۸
9 Ana awo adzakhala odziwika pakati pa mitundu ya anthu ndipo adzukulu awo adzakhala otchuka pakati pa anthu a mitundu ina. Aliyense wowaona adzazindikira kuti ndi anthu amene Yehova wawadalitsa.”
و نسل ایشان در میان امت‌ها وذریت ایشان در میان قوم‌ها معروف خواهند شد. هر‌که ایشان را بیند اعتراف خواهد نمود که ایشان ذریت مبارک خداوند می‌باشند.۹
10 Ine ndikusangalala kwambiri chifukwa cha Yehova; moyo wanga ukukondwera chifukwa cha Mulungu wanga. Pakuti Iye wandiveka zovala zachipulumutso, ndipo wandiveka mkanjo wachilungamo. Zili ngati mkwati wovala nkhata ya maluwa mʼkhosi mwake, ndiponso ngati mkwatibwi wovala mikanda yamtengowapatali.
در خداوند شادی بسیار می‌کنم و جان من در خدای خود وجد می‌نماید زیرا که مرا به‌جامه نجات ملبس ساخته، ردای عدالت را به من پوشانید. چنانکه داماد خویشتن را به تاج آرایش می‌دهد و عروس، خود را به زیورها زینت می‌بخشد.۱۰
11 Monga momwe nthaka imameretsa mbewu ndiponso monga munda umakulitsa mbewu zimene anadzala, momwemonso Ambuye Yehova adzaonetsa chilungamo ndi matamando pamaso pa mitundu yonse ya anthu.
زیرا چنانکه زمین، نباتات خود رامی رویاند و باغ، زرع خویش را نمو می‌دهد، همچنان خداوند یهوه عدالت و تسبیح را پیش روی تمامی امت‌ها خواهد رویانید.۱۱

< Yesaya 61 >