< Yesaya 61 >
1 Mzimu wa Ambuye Yehova uli pa ine, chifukwa Yehova wandidzoza kuti ndilalikire uthenga wabwino kwa anthu osauka. Wandituma kuti ndikatonthoze anthu osweka mtima, ndikalengeze kwa akapolo kuti alandire ufulu ndiponso kuti ndikamasule a mʼndende.
Ngun lun LEUM GOD Fulatlana oan fuk. El suleyula, mosrweyula ac supweyume In use pweng wo nu sin mwet sukasrup, In akkeyala insien mwet su munasla finsrak la, In fahkak lah God El aksukosokye mwet sruoh, Ac El tulala elos su muta in kapir.
2 Wandituma kuti ndikalengeze nthawi imene Yehova adzapulumutsa anthu ake; za tsiku limene Yehova adzalanga adani a anthu ake. Wandituma kuti ndikatonthoze olira.
El supweyume in sulkakin Lah pacl uh summa Ke LEUM GOD El fah molela mwet lal, Ac kutangla mwet lokoalok lalos. El supweyume in akwoyalos nukewa su asor,
3 Wandituma kuti ndiwakonzere olira a ku Ziyoni, nkhata ya maluwa yokongola mʼmalo mwa phulusa, ndiwapatse mafuta achikondwerero mʼmalo mwa kulira. Ndiwapatse chovala cha matamando mʼmalo mwa mtima wopsinjika. Ndipo iwo adzatchedwa mitengo ya thundu yamphamvu yachilungamo, yoyidzala Yehova kuti Iye mwini apezemo ulemerero wake.
Ac in oru tuh elos su mwemelil in Zion In engan ac insewowo, ac tia asor, Tuh elos in onkakin soko on in kaksak ac tia on in asor. Elos ac fah oana sak Ma LEUM GOD sifacna El yukwiya. Elos nukewa fah oru ma suwohs, Ac mwet uh fah kaksakin God ke ma El orala.
4 Adzamanganso mabwinja akale a mzinda ndipo malo amene anawonongeka kalekale aja adzakonzanso. Adzakonzanso mizinda imene inapasuka, imene yakhala yowonongeka kwa nthawi yayitali kwambiri.
Elos fah sifil musaela siti ma oanna sruala ke pacl na loes, Ac aksasuye acn ma musalla ke fwil puspis somla.
5 Anthu achilendo adzakutumikirani; adzazidyetsa ziweto zanu; iwo adzagwira ntchito mʼminda yanu ya mpesa.
Mwet luk, mwetsac ac fah kulansupwekowos. Elos ac fah karingin un kosro nutuwos Ac imai acn suwos, ac liyaung ima in grape sunowos.
6 Ndipo inu mudzatchedwa ansembe a Yehova, adzakutchulani kuti ndinu atumiki a Mulungu wathu. Mudzadyerera chuma cha mitundu ya anthu, ndipo mudzanyadira ulemu umene mwalandira.
Ac fah eteyuk kowos lah kowos mwet tol lun LEUM GOD, Mwet kulansap lun God lasr. Kowos fah engankin mwe kasrup lun mutunfacl puspis, Ac konkin lah ma ingan ma lowos.
7 Chifukwa manyazi awo anali owirikiza; ndi kuti munalandira chitonzo ndi kutukwana, adzakondwera ndi cholowa chawo, tsono adzalandira cholowa chawo cha chigawo cha dziko mowirikiza, ndipo chimwemwe chamuyaya chidzakhala chawo.
Mwe mwekin ac mwe akkoluk nu suwos uh safla. Kowos fah muta in facl suwos sifacna, Ac mwe kasrup lowos ac fah yokelik pacl luo. Engan lowos fah oanna nwe tok.
8 “Pakuti Ine Yehova, ndimakonda chilungamo; ndimadana ndi zakuba ndi zoyipa. Anthu anga ndidzawapatsa mphotho mokhulupirika ndikupangana nawo pangano losatha.
LEUM GOD El fahk, “Nga lungse nununku suwohs, ac nga srunga pisrapasr ac orekma sesuwos. Nga fah oaru in sang ma lacne nu sin mwet luk, Ac nga fah oru sie wuleang kawil yorolos.
9 Ana awo adzakhala odziwika pakati pa mitundu ya anthu ndipo adzukulu awo adzakhala otchuka pakati pa anthu a mitundu ina. Aliyense wowaona adzazindikira kuti ndi anthu amene Yehova wawadalitsa.”
Elos ac fah pwengpeng inmasrlon mutunfacl uh. Mwet nukewa su liyalos fah etu Lah elos mwet su nga akinsewowoye.”
10 Ine ndikusangalala kwambiri chifukwa cha Yehova; moyo wanga ukukondwera chifukwa cha Mulungu wanga. Pakuti Iye wandiveka zovala zachipulumutso, ndipo wandiveka mkanjo wachilungamo. Zili ngati mkwati wovala nkhata ya maluwa mʼkhosi mwake, ndiponso ngati mkwatibwi wovala mikanda yamtengowapatali.
Jerusalem el arulana engankin ma LEUM GOD El oru. God El nokmulang ke molela ac kutangla, Ac ma inge oana mwe naweyuk lun mutan se ac mukul se su akola in marut.
11 Monga momwe nthaka imameretsa mbewu ndiponso monga munda umakulitsa mbewu zimene anadzala, momwemonso Ambuye Yehova adzaonetsa chilungamo ndi matamando pamaso pa mitundu yonse ya anthu.
In oana ke fita uh ac srunak ac kapak, Ouinge LEUM GOD Fulatlana El fah molela mwet lal, Ac mutunfacl nukewa fah kaksakunul.