< Yesaya 61 >

1 Mzimu wa Ambuye Yehova uli pa ine, chifukwa Yehova wandidzoza kuti ndilalikire uthenga wabwino kwa anthu osauka. Wandituma kuti ndikatonthoze anthu osweka mtima, ndikalengeze kwa akapolo kuti alandire ufulu ndiponso kuti ndikamasule a mʼndende.
Herran, Herran Henki on minun päälläni, sillä hän on voidellut minut julistamaan ilosanomaa nöyrille, lähettänyt minut sitomaan särjettyjä sydämiä, julistamaan vangituille vapautusta ja kahlituille kirvoitusta,
2 Wandituma kuti ndikalengeze nthawi imene Yehova adzapulumutsa anthu ake; za tsiku limene Yehova adzalanga adani a anthu ake. Wandituma kuti ndikatonthoze olira.
julistamaan Herran otollista vuotta ja meidän Jumalamme kostonpäivää, lohduttamaan kaikkia murheellisia,
3 Wandituma kuti ndiwakonzere olira a ku Ziyoni, nkhata ya maluwa yokongola mʼmalo mwa phulusa, ndiwapatse mafuta achikondwerero mʼmalo mwa kulira. Ndiwapatse chovala cha matamando mʼmalo mwa mtima wopsinjika. Ndipo iwo adzatchedwa mitengo ya thundu yamphamvu yachilungamo, yoyidzala Yehova kuti Iye mwini apezemo ulemerero wake.
panemaan Siionin murheellisten päähän-antamaan heille-juhlapäähineen tuhkan sijaan, iloöljyä murheen sijaan, ylistyksen vaipan masentuneen hengen sijaan; ja heidän nimensä on oleva "vanhurskauden tammet", "Herran istutus", hänen kirkkautensa ilmoitukseksi.
4 Adzamanganso mabwinja akale a mzinda ndipo malo amene anawonongeka kalekale aja adzakonzanso. Adzakonzanso mizinda imene inapasuka, imene yakhala yowonongeka kwa nthawi yayitali kwambiri.
Ja he rakentavat jälleen ikivanhat rauniot, kohottavat ennalleen esi-isien autiot paikat; ja he uudistavat rauniokaupungit, jotka ovat olleet autiot polvesta polveen.
5 Anthu achilendo adzakutumikirani; adzazidyetsa ziweto zanu; iwo adzagwira ntchito mʼminda yanu ya mpesa.
Vieraat ovat teidän laumojenne paimenina, muukalaiset teidän peltomiehinänne ja viinitarhureinanne.
6 Ndipo inu mudzatchedwa ansembe a Yehova, adzakutchulani kuti ndinu atumiki a Mulungu wathu. Mudzadyerera chuma cha mitundu ya anthu, ndipo mudzanyadira ulemu umene mwalandira.
Mutta teitä kutsutaan Herran papeiksi, sanotaan meidän Jumalamme palvelijoiksi; te saatte nauttia kansain rikkaudet ja periä heidän kunniansa.
7 Chifukwa manyazi awo anali owirikiza; ndi kuti munalandira chitonzo ndi kutukwana, adzakondwera ndi cholowa chawo, tsono adzalandira cholowa chawo cha chigawo cha dziko mowirikiza, ndipo chimwemwe chamuyaya chidzakhala chawo.
Häpeänne hyvitetään teille kaksin kerroin, ja pilkatut saavat riemuita osastansa. Niin he saavat kaksinkertaisen perinnön maassansa; heillä on oleva iankaikkinen ilo.
8 “Pakuti Ine Yehova, ndimakonda chilungamo; ndimadana ndi zakuba ndi zoyipa. Anthu anga ndidzawapatsa mphotho mokhulupirika ndikupangana nawo pangano losatha.
Sillä minä, Herra, rakastan oikeutta, vihaan vääryyttä ja ryöstöä; ja minä annan heille palkan uskollisesti ja teen heidän kanssansa iankaikkisen liiton.
9 Ana awo adzakhala odziwika pakati pa mitundu ya anthu ndipo adzukulu awo adzakhala otchuka pakati pa anthu a mitundu ina. Aliyense wowaona adzazindikira kuti ndi anthu amene Yehova wawadalitsa.”
Heidän siemenensä tulee tunnetuksi kansain keskuudessa ja heidän jälkeläisensä kansakuntien keskellä; kaikki, jotka näkevät heitä, tuntevat heidät Herran siunaamaksi siemeneksi.
10 Ine ndikusangalala kwambiri chifukwa cha Yehova; moyo wanga ukukondwera chifukwa cha Mulungu wanga. Pakuti Iye wandiveka zovala zachipulumutso, ndipo wandiveka mkanjo wachilungamo. Zili ngati mkwati wovala nkhata ya maluwa mʼkhosi mwake, ndiponso ngati mkwatibwi wovala mikanda yamtengowapatali.
Minä iloitsen suuresti Herrassa, minun sieluni riemuitsee minun Jumalassani, sillä hän pukee minun ylleni autuuden vaatteet ja verhoaa minut vanhurskauden viittaan, yljän kaltaiseksi, joka kantaa juhlapäähinettä niinkuin pappi, ja morsiamen kaltaiseksi, joka on koruillansa kaunistettu.
11 Monga momwe nthaka imameretsa mbewu ndiponso monga munda umakulitsa mbewu zimene anadzala, momwemonso Ambuye Yehova adzaonetsa chilungamo ndi matamando pamaso pa mitundu yonse ya anthu.
Sillä niinkuin maa tuottaa kasvunsa ja niinkuin kasvitarha saa siemenkylvönsä versomaan, niin saattaa Herra, Herra versomaan vanhurskauden ja kiitoksen kaikkien kansojen nähden.

< Yesaya 61 >