< Yesaya 61 >

1 Mzimu wa Ambuye Yehova uli pa ine, chifukwa Yehova wandidzoza kuti ndilalikire uthenga wabwino kwa anthu osauka. Wandituma kuti ndikatonthoze anthu osweka mtima, ndikalengeze kwa akapolo kuti alandire ufulu ndiponso kuti ndikamasule a mʼndende.
Duch Panovníka Hospodina jest nade mnou, proto že pomazal mne Hospodin, abych kázal evangelium tichým. Poslal mne, abych uvázal rány skroušených srdcem, abych vyhlásil jatým svobodu, a vězňům otevření žaláře,
2 Wandituma kuti ndikalengeze nthawi imene Yehova adzapulumutsa anthu ake; za tsiku limene Yehova adzalanga adani a anthu ake. Wandituma kuti ndikatonthoze olira.
Abych vyhlásil léto milostivé Hospodinovo, a den pomsty Boha našeho, abych těšil všecky kvílící,
3 Wandituma kuti ndiwakonzere olira a ku Ziyoni, nkhata ya maluwa yokongola mʼmalo mwa phulusa, ndiwapatse mafuta achikondwerero mʼmalo mwa kulira. Ndiwapatse chovala cha matamando mʼmalo mwa mtima wopsinjika. Ndipo iwo adzatchedwa mitengo ya thundu yamphamvu yachilungamo, yoyidzala Yehova kuti Iye mwini apezemo ulemerero wake.
Abych způsobil radost kvílícím Sionským, a dal jim okrasu místo popela, olej veselé místo smutku, oděv chvály místo ducha sevřeného. I nazvání budou stromové spravedlnosti, štípení Hospodinovo, abych oslavován byl.
4 Adzamanganso mabwinja akale a mzinda ndipo malo amene anawonongeka kalekale aja adzakonzanso. Adzakonzanso mizinda imene inapasuka, imene yakhala yowonongeka kwa nthawi yayitali kwambiri.
Tedy vzdělají pustiny starodávní, pouště staré spraví, a obnoví města zpuštěná, pustá po mnohé národy.
5 Anthu achilendo adzakutumikirani; adzazidyetsa ziweto zanu; iwo adzagwira ntchito mʼminda yanu ya mpesa.
Nebo postaví se cizozemci, a pásti budou stáda vaše, a synové cizozemců oráči vaši a vinaři vaši budou.
6 Ndipo inu mudzatchedwa ansembe a Yehova, adzakutchulani kuti ndinu atumiki a Mulungu wathu. Mudzadyerera chuma cha mitundu ya anthu, ndipo mudzanyadira ulemu umene mwalandira.
Vy pak kněží Hospodinovi nazváni budete, služebníci Boha našeho slouti budete, zboží pohanů užívati budete, a v slávě jejich zvýšeni budete.
7 Chifukwa manyazi awo anali owirikiza; ndi kuti munalandira chitonzo ndi kutukwana, adzakondwera ndi cholowa chawo, tsono adzalandira cholowa chawo cha chigawo cha dziko mowirikiza, ndipo chimwemwe chamuyaya chidzakhala chawo.
Za dvojnásobní zahanbení vaše a pohanění prozpěvovati budete, z podílu jejich a v zemi jejich dvojnásobní dědictví obdržíte, a tak veselé věčné míti budete.
8 “Pakuti Ine Yehova, ndimakonda chilungamo; ndimadana ndi zakuba ndi zoyipa. Anthu anga ndidzawapatsa mphotho mokhulupirika ndikupangana nawo pangano losatha.
Já zajisté Hospodin miluji soud, a nenávidím loupeže při oběti, a protož způsobím, aby skutkové jejich dáli se v pravdě, a smlouvu věčnou s nimi učiním.
9 Ana awo adzakhala odziwika pakati pa mitundu ya anthu ndipo adzukulu awo adzakhala otchuka pakati pa anthu a mitundu ina. Aliyense wowaona adzazindikira kuti ndi anthu amene Yehova wawadalitsa.”
I vejdeť v známost mezi pohany símě jejich, a potomci jejich u prostřed národů. Všickni, kteříž je uzří, poznají je, že jsou símě, jemuž požehnal Hospodin.
10 Ine ndikusangalala kwambiri chifukwa cha Yehova; moyo wanga ukukondwera chifukwa cha Mulungu wanga. Pakuti Iye wandiveka zovala zachipulumutso, ndipo wandiveka mkanjo wachilungamo. Zili ngati mkwati wovala nkhata ya maluwa mʼkhosi mwake, ndiponso ngati mkwatibwi wovala mikanda yamtengowapatali.
Velice se budu radovati v Hospodinu, a plésati bude duše má v Bohu mém; nebo mne oblékl v roucho spasení, a pláštěm spravedlnosti přioděl mne jako ženicha, kterýž se strojí ozdobně, a jako nevěstu okrašlující se ozdobami svými.
11 Monga momwe nthaka imameretsa mbewu ndiponso monga munda umakulitsa mbewu zimene anadzala, momwemonso Ambuye Yehova adzaonetsa chilungamo ndi matamando pamaso pa mitundu yonse ya anthu.
Nebo jakož země vydává zrostlinu svou, a jakož zahrada símě své vyvodí, tak Panovník Hospodin vyvede spravedlnost a chválu přede všemi národy.

< Yesaya 61 >