< Yesaya 61 >

1 Mzimu wa Ambuye Yehova uli pa ine, chifukwa Yehova wandidzoza kuti ndilalikire uthenga wabwino kwa anthu osauka. Wandituma kuti ndikatonthoze anthu osweka mtima, ndikalengeze kwa akapolo kuti alandire ufulu ndiponso kuti ndikamasule a mʼndende.
Mathoenaw koe kamthang dei hanelah BAWIPA ni satui na awi dawkvah, Bawipa Jehovah e Muitha teh kai dawk ao. Ahni ni a lungkareknaw dam sak hane hoi sannaw koe hloutnae pathang pouh hane hoi, pâkhi teh thongkabawtnaw koe thongim paawng pouh hanelah na patoun.
2 Wandituma kuti ndikalengeze nthawi imene Yehova adzapulumutsa anthu ake; za tsiku limene Yehova adzalanga adani a anthu ake. Wandituma kuti ndikatonthoze olira.
BAWIPA lungyouk kum hoi, Cathut moipathung hnin dei hane hoi, a lungkamathout e pueng lungpahawi hanelah na patoun.
3 Wandituma kuti ndiwakonzere olira a ku Ziyoni, nkhata ya maluwa yokongola mʼmalo mwa phulusa, ndiwapatse mafuta achikondwerero mʼmalo mwa kulira. Ndiwapatse chovala cha matamando mʼmalo mwa mtima wopsinjika. Ndipo iwo adzatchedwa mitengo ya thundu yamphamvu yachilungamo, yoyidzala Yehova kuti Iye mwini apezemo ulemerero wake.
Ama teh pholen lah ao vaiteh, ahnimouh teh BAWIPA ni ung e, lannae thingkung telah kaw thai nahanelah, hraba yueng lah luhuem, lungmathoenae yueng lah lunghawinae satui, muitha thayounnae yueng lah pholennae khohna ahnimouh poe hane hoi, Zion vah lungkamathoutnaw lungpahawi hanelah na patoun telah ati.
4 Adzamanganso mabwinja akale a mzinda ndipo malo amene anawonongeka kalekale aja adzakonzanso. Adzakonzanso mizinda imene inapasuka, imene yakhala yowonongeka kwa nthawi yayitali kwambiri.
Ayan vah ka rawk e hah bout a sak awh han. Ayan vah a raphoe awh e hah bout a thawng awh han. Se moikapap ka rawk tangcoung e hah bout a pathoup awh han.
5 Anthu achilendo adzakutumikirani; adzazidyetsa ziweto zanu; iwo adzagwira ntchito mʼminda yanu ya mpesa.
Imyinnaw ni kangdout awh vaiteh, nangmae saring a khoum awh han. Ramlouknaw ni nangmouh hanelah law a sak awh vaiteh, misur takha a sak awh han.
6 Ndipo inu mudzatchedwa ansembe a Yehova, adzakutchulani kuti ndinu atumiki a Mulungu wathu. Mudzadyerera chuma cha mitundu ya anthu, ndipo mudzanyadira ulemu umene mwalandira.
Hatei, nangmouh teh BAWIPA e vaihma, telah na kaw awh vaiteh, Cathut e san telah ati awh han. Jentelnaw tawnta e hah na cat awh vaiteh, ahnimae bawilennae dawk na kâoup awh han.
7 Chifukwa manyazi awo anali owirikiza; ndi kuti munalandira chitonzo ndi kutukwana, adzakondwera ndi cholowa chawo, tsono adzalandira cholowa chawo cha chigawo cha dziko mowirikiza, ndipo chimwemwe chamuyaya chidzakhala chawo.
Na kayanae yueng lah let hni touh bari lah na awm awh vaiteh, barihoehnae yueng lah amamae ham dawk a konawm awh han. Hatdawkvah, amamae ram dawk let hni touh hoi coe awh vaiteh, a yungyoe konawmnae teh ahnimae lah ao han.
8 “Pakuti Ine Yehova, ndimakonda chilungamo; ndimadana ndi zakuba ndi zoyipa. Anthu anga ndidzawapatsa mphotho mokhulupirika ndikupangana nawo pangano losatha.
Bangkongtetpawiteh, kai Jehovah ni kângingnae hah ka lungpataw teh, lawp e hoi payonnae hateh, ka hmuma. Yuemkamculah ahnimanaw hah a tawk e ka poe vaiteh, ahnimouh hoi a yungyoe lawkkam ka sak han.
9 Ana awo adzakhala odziwika pakati pa mitundu ya anthu ndipo adzukulu awo adzakhala otchuka pakati pa anthu a mitundu ina. Aliyense wowaona adzazindikira kuti ndi anthu amene Yehova wawadalitsa.”
Amamae catounnaw teh, Jentelnaw koe kamthang awh vaiteh, a canaw teh tamipueng koe panue e lah ao awh han. Ahnimouh ka hmawt e pueng ni BAWIPA ni yawhawi a poe e miphun doeh tie hah a panue awh han.
10 Ine ndikusangalala kwambiri chifukwa cha Yehova; moyo wanga ukukondwera chifukwa cha Mulungu wanga. Pakuti Iye wandiveka zovala zachipulumutso, ndipo wandiveka mkanjo wachilungamo. Zili ngati mkwati wovala nkhata ya maluwa mʼkhosi mwake, ndiponso ngati mkwatibwi wovala mikanda yamtengowapatali.
BAWIPA dawk ka o a nawm katang han. Ka hringnae teh ka Cathut dawk a lunghawi katang han. Bangkongtetpawiteh, yu kalatkung ni luhuem a huem e patetlah thoseh, vâ ka sak hane langa ni a kamthoup e patetlah thoseh, rungngangnae khohna hoi kai hah na pathoup teh, lannae angkidung hoi kai hah na khu toe.
11 Monga momwe nthaka imameretsa mbewu ndiponso monga munda umakulitsa mbewu zimene anadzala, momwemonso Ambuye Yehova adzaonetsa chilungamo ndi matamando pamaso pa mitundu yonse ya anthu.
Bangkongtetpawiteh, talai ni pho a dâwn sak e patetlah Bawipa Jehovah ni tami pueng e hmalah, lannae hoi pholennae hah a dâwn sak van han.

< Yesaya 61 >