< Yesaya 60 >

1 “Dzuka, wala, pakuti kuwala kwako kwafika, ndipo ulemerero wa Yehova wakuwalira.
Светися, светися Иерусалиме, прииде бо твой свет, и слава Господня на тебе возсия.
2 Taona, mdima waphimba dziko lapansi ndipo mdima wandiweyani wagwa pa anthu a mitundu ina, koma Yehova adzakuwalira iwe, ndipo ulemerero wake udzaoneka pa iwe.
Се, тма покрыет землю, и мрак на языки, на тебе же явится Господь, и слава Его на тебе узрится.
3 Mitundu ya anthu idzatsata kuwunika kwako ndipo mafumu adzalondola kunyezimira kwa mʼbandakucha wako.
И пойдут царие светом твоим, и языцы светлостию твоею.
4 “Tukula maso ako, yangʼanayangʼana ndipo ona zimene zikuchitika. Onse akusonkhana ndipo akubwera kwa iwe; ana ako a amuna akubwera kuchokera kutali ndipo ana ako aakazi anyamulidwa mʼmanja.
Возведи окрест очи твои и виждь собраная чада твоя: се, приидоша вси сынове твои издалеча, и дщери твоя на рамех возмутся.
5 Ukadzaona zimenezi udzasangalala kwambiri, mtima wako udzalumpha ndi kudzaza ndi chimwemwe; chuma chakunyanja chidzabwera kwa iwe chuma cha mitundu ya anthu chidzabwera kwa iwe.
Тогда узриши и возрадуешися, и убоишися и ужаснешися сердцем, яко преложится к тебе богатство морское и языков и людий:
6 Gulu la ngamira lidzaphimba dziko lako, ngamira zingʼonozingʼono zidzachokera ku Midiyani ndi ku Efai. Ndipo onse a ku Seba adzabwera atanyamula golide ndi lubani uku akutamanda Yehova.
и приидут к тебе стада велблюд, и покрыют тя велблюди Мадиамстии и Гефарстии: вси от Савы приидут, носяще злато, и Ливан принесут и камень честен, и спасение Господне благовозвестят:
7 Ziweto zonse za ku Kedara adzazisonkhanitsa kwa inu, nkhosa zazimuna za ku Nabayoti zidzakutumikirani; zidzalandiridwa monga chopereka pa guwa langa la nsembe, ndipo ndidzakongoletsa Nyumba yanga.
и вся овцы Кидарския соберутся тебе, и овни Навеофстии приидут к тебе, и вознесутся приятная на жертвенник Мой, и дом молитвы Моея прославится.
8 “Kodi ndi zayani izo zikuwuluka ngati mitambo, ngati kapena nkhunda zobwerera ku zisa zawo?
Кии суть, иже яко облацы летят, и яко голубие со птенцы ко мне?
9 Ndithu, izi ndi sitima za pa madzi zochokera ku mayiko akutali; patsogolo pali sitima zapamadzi za ku Tarisisi, zikubweretsa ana ako ochokera kutali, pamodzi ndi siliva wawo ndi golide wawo, kudzalemekeza Yehova Mulungu wako, Woyerayo wa Israeli, pakuti Iye wakuvekani inu ulemerero.
Мене острови ждаша, и корабли Фарсийстии во первых, привести чада твоя издалеча, и сребро и злато их с ними, имене ради Господня Святаго, и за еже Святому Израилеву славну быти.
10 “Alendo adzamanganso malinga ako, ndipo mafumu awo adzakutumikira. Ngakhale ndinakukantha ndili wokwiya, koma tsopano ndidzakukomera mtima ndikukuchitira chifundo.
И созиждут сынове инороднии стены твоя, и царие их предстояти будут тебе: за гнев бо Мой поразих тя и за милость Мою возлюбих тя.
11 Zipata zako zidzakhala zotsekula nthawi zonse, sadzazitseka nthawi zonse, usana ndi usiku, kotero anthu adzabwera kwa iwe ndi chuma chawo, akuyenda pa mdipiti mafumu awo ali patsogolo.
И отверзутся врата твоя присно, день и нощь не затворятся, ввести к тебе силу язык и цари их ведомыя.
12 Pakuti mtundu wa anthu ndi mafumu amene sakutumikira iwe; adzawonongeka kotheratu.
Языцы бо и царие, иже не поработают ти, погибнут, и языцы запустением запустеют.
13 “Adzabwera nayo kwa iwe mitengo ya payini, mkuyu ndi naphini imene ili mʼnkhalango ya Lebanoni kuti adzakongoletsere malo a nyumba yanga yopatulika; ndipo ndidzalemekeza malo amene Ine ndimapondapo.
И слава Ливанова к тебе приидет, кипарисом и певгом и кедром вкупе, прославити место святое Мое, и место ногу Моею прославлю.
14 Ana aja amene anakuzunzani adzabwera ndipo adzakugwadirani; onse amene anakunyozani adzagwada pansi pa mapazi anu. Ndipo adzakutchani kuti Mzinda wa Yehova; Ziyoni mzinda wa Woyerayo wa Israeli.
И пойдут к тебе боящеся сынове смиривших тя и раздраживших тя, и поклонятся следам ногу твоею вси прогневавшии тя, и наречешися град Господень, Сион Святаго Израилева.
15 “Ngakhale anthu anakusiya nadana nawe, koma Ine ndidzakukuza mpaka muyaya, ndipo udzakhala malo a chimwemwe cha anthu amibado yonse.
За сие, яко был еси оставлен и возненавиден и не бе помагающаго ти, положу тя в радость вечную, веселие родом родов.
16 Udzamwa mkaka wa mitundu ya anthu ndi kuleredwa pa maere aufumu, motero udzadziwa kuti Ine Yehova, ndine Mpulumutsi wako, Momboli wako ndiye Wamphamvu wa Yakobo.
И изссеши млеко языков и богатство царей снеси, и уразумееши, яко Аз Господь Спасаяй тя и Избавляяй тя Бог Израилев.
17 Ndidzakupatsa golide mʼmalo mwa mkuwa, ndi siliva mʼmalo mwa chitsulo. Ndidzakupatsa mkuwa mʼmalo mwa thabwa ndi chitsulo mʼmalo mwa miyala. Olamulira ako adzakhala a mtendere. Ndidzasandutsa okulamulira kuti akhale achilungamo.
И вместо меди принесу ти злато, и вместо железа принесу ти сребро, и вместо древес принесу ти медь, и вместо камения железо: и вдам князи твоя в мир и надзиратели твоя в правду.
18 Ziwawa sizidzamvekanso mʼdziko lako, bwinja kapena chiwonongeko sizidzapezeka mʼdziko lako, ndidzakhala malinga ako okuteteza ndipo udzanditamanda.
И не услышится посем неправда в земли твоей, ни сокрушение ни бедность во пределех твоих, но прозовется спасение забрала твоя и врата твоя хвала.
19 Sipadzakhala dzuwa kuti likuwunikire, kapena mwezi kuti uwunikire usiku, pakuti Yehova ndiye adzakhale kuwunika kwako kwa muyaya, ndipo Mulungu wako adzakhala ulemerero wako.
И не будет тебе ктому солнце во свет дне, ниже восход луны просветит твою нощь, но будет тебе Господь свет вечный и Бог слава твоя.
20 Dzuwa lako silidzalowanso, ndipo mwezi wako sudzazimiriranso; Yehova adzakhala kuwunika kwako kwamuyaya, ndipo masiku a mavuto ako adzatha.
Не зайдет бо солнце тебе, и луна не оскудеет тебе: будет бо Господь тебе свет вечный, и исполнятся дние рыдания твоего.
21 Ndipo anthu ako onse adzakhala olungama ndipo dzikolo lidzakhala lawo mpaka muyaya. Iwo ndi mphukira imene Ine ndayidzala, ntchito ya manja anga, kuti aonetse ulemerero wanga.
И людие твои вси праведнии в век наследят землю, храняще сад дела руку Его в славу.
22 Kabanja kakangʼono kadzasanduka fuko, kafuko kakangʼono kudzasanduka mtundu wamphamvu. Ine ndine Yehova, nthawi yake ikafika ndidzazichita zimenezi mofulumira.”
Малый будет в тысящы, а малейший во язык велик: Аз Господь по времени соберу их.

< Yesaya 60 >