< Yesaya 60 >

1 “Dzuka, wala, pakuti kuwala kwako kwafika, ndipo ulemerero wa Yehova wakuwalira.
Lève-toi, sois illuminée! Car ta lumière est venue, et la gloire de l'Éternel s'est levée sur toi!
2 Taona, mdima waphimba dziko lapansi ndipo mdima wandiweyani wagwa pa anthu a mitundu ina, koma Yehova adzakuwalira iwe, ndipo ulemerero wake udzaoneka pa iwe.
Car voici, les ténèbres couvriront la terre, et l'obscurité couvrira les peuples; mais sur toi se lèvera l'Éternel, et sur toi paraîtra sa gloire.
3 Mitundu ya anthu idzatsata kuwunika kwako ndipo mafumu adzalondola kunyezimira kwa mʼbandakucha wako.
Et les nations marcheront à ta lumière, et les rois à la clarté de tes rayons.
4 “Tukula maso ako, yangʼanayangʼana ndipo ona zimene zikuchitika. Onse akusonkhana ndipo akubwera kwa iwe; ana ako a amuna akubwera kuchokera kutali ndipo ana ako aakazi anyamulidwa mʼmanja.
Jette les yeux autour de toi et regarde: tous ceux-ci se rassemblent, ils viennent à toi; tes fils viennent de loin, et tes filles sont portées sur les bras.
5 Ukadzaona zimenezi udzasangalala kwambiri, mtima wako udzalumpha ndi kudzaza ndi chimwemwe; chuma chakunyanja chidzabwera kwa iwe chuma cha mitundu ya anthu chidzabwera kwa iwe.
Alors tu le verras, et tu resplendiras de joie, ton cœur tressaillira et s'épanouira; car l'abondance de la mer se tournera vers toi, et la puissance des nations viendra chez toi.
6 Gulu la ngamira lidzaphimba dziko lako, ngamira zingʼonozingʼono zidzachokera ku Midiyani ndi ku Efai. Ndipo onse a ku Seba adzabwera atanyamula golide ndi lubani uku akutamanda Yehova.
Une multitude de chameaux couvrira ton pays, les dromadaires de Madian et d'Épha; tous ils viendront de Shéba; ils apporteront de l'or et de l'encens, et publieront les louanges de l'Éternel.
7 Ziweto zonse za ku Kedara adzazisonkhanitsa kwa inu, nkhosa zazimuna za ku Nabayoti zidzakutumikirani; zidzalandiridwa monga chopereka pa guwa langa la nsembe, ndipo ndidzakongoletsa Nyumba yanga.
Toutes les brebis de Kédar seront rassemblées vers toi, les béliers de Nébajoth seront à ton service; ils monteront en agréable offrande sur mon autel, et je rendrai magnifique la maison de ma gloire.
8 “Kodi ndi zayani izo zikuwuluka ngati mitambo, ngati kapena nkhunda zobwerera ku zisa zawo?
Qui sont ceux-là, volant comme des nuages, comme des pigeons vers leurs colombiers?
9 Ndithu, izi ndi sitima za pa madzi zochokera ku mayiko akutali; patsogolo pali sitima zapamadzi za ku Tarisisi, zikubweretsa ana ako ochokera kutali, pamodzi ndi siliva wawo ndi golide wawo, kudzalemekeza Yehova Mulungu wako, Woyerayo wa Israeli, pakuti Iye wakuvekani inu ulemerero.
Car les îles s'attendront à moi, et les navires de Tarsis les premiers, pour amener de loin tes enfants, avec leur argent et leur or, à la gloire du nom de l'Éternel ton Dieu, et du Saint d'Israël qui te glorifie.
10 “Alendo adzamanganso malinga ako, ndipo mafumu awo adzakutumikira. Ngakhale ndinakukantha ndili wokwiya, koma tsopano ndidzakukomera mtima ndikukuchitira chifundo.
Les fils de l'étranger rebâtiront tes murs, et leurs rois te serviront; car je t'ai frappée dans ma colère, mais, dans ma bienveillance, j'ai compassion de toi.
11 Zipata zako zidzakhala zotsekula nthawi zonse, sadzazitseka nthawi zonse, usana ndi usiku, kotero anthu adzabwera kwa iwe ndi chuma chawo, akuyenda pa mdipiti mafumu awo ali patsogolo.
Tes portes seront continuellement ouvertes; elles ne seront fermées ni jour ni nuit, pour faire entrer chez toi la puissance des nations et leurs rois, qui seront conduits vers toi.
12 Pakuti mtundu wa anthu ndi mafumu amene sakutumikira iwe; adzawonongeka kotheratu.
Car la nation et le royaume qui ne te serviront pas, périront, et ces nations-là seront entièrement détruites.
13 “Adzabwera nayo kwa iwe mitengo ya payini, mkuyu ndi naphini imene ili mʼnkhalango ya Lebanoni kuti adzakongoletsere malo a nyumba yanga yopatulika; ndipo ndidzalemekeza malo amene Ine ndimapondapo.
La gloire du Liban viendra chez toi, le cyprès, l'orme et le buis ensemble, pour orner le lieu de mon sanctuaire, et je glorifierai le lieu où reposent mes pieds.
14 Ana aja amene anakuzunzani adzabwera ndipo adzakugwadirani; onse amene anakunyozani adzagwada pansi pa mapazi anu. Ndipo adzakutchani kuti Mzinda wa Yehova; Ziyoni mzinda wa Woyerayo wa Israeli.
Et les fils de ceux qui t'opprimaient viendront vers toi en se courbant; tous ceux qui te méprisaient se prosterneront jusque sous tes pieds, et t'appelleront la ville de l'Éternel, la Sion du Saint d'Israël.
15 “Ngakhale anthu anakusiya nadana nawe, koma Ine ndidzakukuza mpaka muyaya, ndipo udzakhala malo a chimwemwe cha anthu amibado yonse.
Au lieu que tu étais délaissée et haïe, et que personne ne passait chez toi, je ferai de toi une magnificence éternelle, une joie qui durera d'âge en âge.
16 Udzamwa mkaka wa mitundu ya anthu ndi kuleredwa pa maere aufumu, motero udzadziwa kuti Ine Yehova, ndine Mpulumutsi wako, Momboli wako ndiye Wamphamvu wa Yakobo.
Et tu suceras le lait des nations; tu suceras la mamelle des rois, et tu sauras que moi, l'Éternel, je suis ton Sauveur, que le Puissant de Jacob est ton Rédempteur.
17 Ndidzakupatsa golide mʼmalo mwa mkuwa, ndi siliva mʼmalo mwa chitsulo. Ndidzakupatsa mkuwa mʼmalo mwa thabwa ndi chitsulo mʼmalo mwa miyala. Olamulira ako adzakhala a mtendere. Ndidzasandutsa okulamulira kuti akhale achilungamo.
Au lieu de l'airain je ferai venir de l'or, au lieu de fer je ferai venir de l'argent; au lieu du bois, de l'airain, et au lieu des pierres, du fer. Je te donnerai pour gouverneurs la paix, et pour dominateurs la justice.
18 Ziwawa sizidzamvekanso mʼdziko lako, bwinja kapena chiwonongeko sizidzapezeka mʼdziko lako, ndidzakhala malinga ako okuteteza ndipo udzanditamanda.
On n'entendra plus parler de violence dans ton pays, de ravage ni de ruine dans tes frontières; mais tu appelleras tes murailles Salut, et tes portes Louange.
19 Sipadzakhala dzuwa kuti likuwunikire, kapena mwezi kuti uwunikire usiku, pakuti Yehova ndiye adzakhale kuwunika kwako kwa muyaya, ndipo Mulungu wako adzakhala ulemerero wako.
Tu n'auras plus le soleil pour lumière pendant le jour, et la lueur de la lune ne t'éclairera plus; mais l'Éternel sera pour toi une lumière éternelle, et ton Dieu sera ta gloire.
20 Dzuwa lako silidzalowanso, ndipo mwezi wako sudzazimiriranso; Yehova adzakhala kuwunika kwako kwamuyaya, ndipo masiku a mavuto ako adzatha.
Ton soleil ne se couchera plus, et ta lune ne disparaîtra plus; car l'Éternel sera pour toi une lumière éternelle, et les jours de ton deuil seront finis.
21 Ndipo anthu ako onse adzakhala olungama ndipo dzikolo lidzakhala lawo mpaka muyaya. Iwo ndi mphukira imene Ine ndayidzala, ntchito ya manja anga, kuti aonetse ulemerero wanga.
Ceux de ton peuple seront tous des justes; ils posséderont le pays à perpétuité, rejeton que j'aurai planté, ouvrage de mes mains, pour me glorifier.
22 Kabanja kakangʼono kadzasanduka fuko, kafuko kakangʼono kudzasanduka mtundu wamphamvu. Ine ndine Yehova, nthawi yake ikafika ndidzazichita zimenezi mofulumira.”
Le plus petit deviendra un millier, et le moindre, une nation puissante. Moi, l'Éternel, je hâterai ceci en son temps.

< Yesaya 60 >