< Yesaya 60 >

1 “Dzuka, wala, pakuti kuwala kwako kwafika, ndipo ulemerero wa Yehova wakuwalira.
« Lève-toi, brille, car ta lumière est venue, et la gloire de Yahvé s'est levée sur vous!
2 Taona, mdima waphimba dziko lapansi ndipo mdima wandiweyani wagwa pa anthu a mitundu ina, koma Yehova adzakuwalira iwe, ndipo ulemerero wake udzaoneka pa iwe.
Car voici, les ténèbres couvriront la terre, et d'épaisses ténèbres les peuples; mais Yahvé se lèvera sur vous, et sa gloire sera vue sur vous.
3 Mitundu ya anthu idzatsata kuwunika kwako ndipo mafumu adzalondola kunyezimira kwa mʼbandakucha wako.
Les nations viendront à ta lumière, et les rois à l'éclat de ton lever.
4 “Tukula maso ako, yangʼanayangʼana ndipo ona zimene zikuchitika. Onse akusonkhana ndipo akubwera kwa iwe; ana ako a amuna akubwera kuchokera kutali ndipo ana ako aakazi anyamulidwa mʼmanja.
« Lève tes yeux tout autour, et regarde: ils se rassemblent tous. Ils viennent à vous. Vos fils viendront de loin, et vos filles seront portées dans les bras.
5 Ukadzaona zimenezi udzasangalala kwambiri, mtima wako udzalumpha ndi kudzaza ndi chimwemwe; chuma chakunyanja chidzabwera kwa iwe chuma cha mitundu ya anthu chidzabwera kwa iwe.
Alors tu verras et tu seras rayonnant, et votre cœur palpitera et s'élargira; car l'abondance de la mer se tournera vers vous. La richesse des nations viendra à toi.
6 Gulu la ngamira lidzaphimba dziko lako, ngamira zingʼonozingʼono zidzachokera ku Midiyani ndi ku Efai. Ndipo onse a ku Seba adzabwera atanyamula golide ndi lubani uku akutamanda Yehova.
Une multitude de chameaux te couvriront, les dromadaires de Midian et d'Epha. Tous ceux de Saba viendront. Ils apporteront de l'or et de l'encens, et proclameront les louanges de Yahvé.
7 Ziweto zonse za ku Kedara adzazisonkhanitsa kwa inu, nkhosa zazimuna za ku Nabayoti zidzakutumikirani; zidzalandiridwa monga chopereka pa guwa langa la nsembe, ndipo ndidzakongoletsa Nyumba yanga.
Tous les troupeaux de Kédar seront rassemblés auprès de toi. Les béliers de Nebaioth te serviront. Ils seront acceptés comme offrandes sur mon autel; et j'embellirai ma glorieuse maison.
8 “Kodi ndi zayani izo zikuwuluka ngati mitambo, ngati kapena nkhunda zobwerera ku zisa zawo?
« Qui sont ceux qui volent comme une nuée? et comme les colombes à leurs fenêtres?
9 Ndithu, izi ndi sitima za pa madzi zochokera ku mayiko akutali; patsogolo pali sitima zapamadzi za ku Tarisisi, zikubweretsa ana ako ochokera kutali, pamodzi ndi siliva wawo ndi golide wawo, kudzalemekeza Yehova Mulungu wako, Woyerayo wa Israeli, pakuti Iye wakuvekani inu ulemerero.
Les îles m'attendent, et les navires de Tarsis en premier, pour faire venir vos fils de loin, leur argent et leur or avec eux, au nom de Yahvé ton Dieu, et pour le Saint d'Israël, parce qu'il vous a glorifié.
10 “Alendo adzamanganso malinga ako, ndipo mafumu awo adzakutumikira. Ngakhale ndinakukantha ndili wokwiya, koma tsopano ndidzakukomera mtima ndikukuchitira chifundo.
« Les étrangers bâtiront vos murs, et leurs rois te serviront; car dans ma colère, je t'ai frappé, mais en ma faveur, j'ai eu pitié de toi.
11 Zipata zako zidzakhala zotsekula nthawi zonse, sadzazitseka nthawi zonse, usana ndi usiku, kotero anthu adzabwera kwa iwe ndi chuma chawo, akuyenda pa mdipiti mafumu awo ali patsogolo.
Tes portes seront toujours ouvertes, elles ne se fermeront ni jour ni nuit, afin qu'on t'apporte les richesses des nations et qu'on emmène leurs rois en captivité.
12 Pakuti mtundu wa anthu ndi mafumu amene sakutumikira iwe; adzawonongeka kotheratu.
Car la nation et le royaume qui ne te serviront pas périront; oui, ces nations seront anéanties.
13 “Adzabwera nayo kwa iwe mitengo ya payini, mkuyu ndi naphini imene ili mʼnkhalango ya Lebanoni kuti adzakongoletsere malo a nyumba yanga yopatulika; ndipo ndidzalemekeza malo amene Ine ndimapondapo.
« La gloire du Liban viendra à toi, le cyprès, le pin et le buis réunis, pour embellir le lieu de mon sanctuaire, et je rendrai glorieux le lieu de mes pieds.
14 Ana aja amene anakuzunzani adzabwera ndipo adzakugwadirani; onse amene anakunyozani adzagwada pansi pa mapazi anu. Ndipo adzakutchani kuti Mzinda wa Yehova; Ziyoni mzinda wa Woyerayo wa Israeli.
Les fils de ceux qui t'ont affligé viendront se prosterner devant toi; et tous ceux qui te méprisaient se prosterneront sous la plante de tes pieds. Ils t'appelleront la Cité de Yahvé, la Sion du Saint d'Israël.
15 “Ngakhale anthu anakusiya nadana nawe, koma Ine ndidzakukuza mpaka muyaya, ndipo udzakhala malo a chimwemwe cha anthu amibado yonse.
« Alors que vous avez été abandonnés et haïs, pour que personne ne passe à travers toi, Je ferai de vous une excellence éternelle, une joie pour de nombreuses générations.
16 Udzamwa mkaka wa mitundu ya anthu ndi kuleredwa pa maere aufumu, motero udzadziwa kuti Ine Yehova, ndine Mpulumutsi wako, Momboli wako ndiye Wamphamvu wa Yakobo.
Vous boirez aussi le lait des nations, et nourrira des seins royaux. Alors vous saurez que moi, Yahvé, je suis votre Sauveur, votre Rédempteur, le Puissant de Jacob.
17 Ndidzakupatsa golide mʼmalo mwa mkuwa, ndi siliva mʼmalo mwa chitsulo. Ndidzakupatsa mkuwa mʼmalo mwa thabwa ndi chitsulo mʼmalo mwa miyala. Olamulira ako adzakhala a mtendere. Ndidzasandutsa okulamulira kuti akhale achilungamo.
Pour le bronze, j'apporterai de l'or; pour le fer, j'apporterai de l'argent; pour le bois, le bronze, et pour les pierres, du fer. Je ferai aussi de la paix votre gouverneur, et la droiture votre chef.
18 Ziwawa sizidzamvekanso mʼdziko lako, bwinja kapena chiwonongeko sizidzapezeka mʼdziko lako, ndidzakhala malinga ako okuteteza ndipo udzanditamanda.
On n'entendra plus parler de violence dans votre pays, ni désolation ni destruction dans tes frontières; mais vous appellerez vos murs le Salut, et tes portes Louanges.
19 Sipadzakhala dzuwa kuti likuwunikire, kapena mwezi kuti uwunikire usiku, pakuti Yehova ndiye adzakhale kuwunika kwako kwa muyaya, ndipo Mulungu wako adzakhala ulemerero wako.
Le soleil ne sera plus ta lumière le jour, et l'éclat de la lune ne vous éclairera pas non plus, mais Yahvé sera votre lumière éternelle, et ton Dieu sera ta gloire.
20 Dzuwa lako silidzalowanso, ndipo mwezi wako sudzazimiriranso; Yehova adzakhala kuwunika kwako kwamuyaya, ndipo masiku a mavuto ako adzatha.
Votre soleil ne se couchera plus, et votre lune ne se retirera pas non plus; car Yahvé sera votre lumière éternelle, et les jours de ton deuil prendront fin.
21 Ndipo anthu ako onse adzakhala olungama ndipo dzikolo lidzakhala lawo mpaka muyaya. Iwo ndi mphukira imene Ine ndayidzala, ntchito ya manja anga, kuti aonetse ulemerero wanga.
Alors ton peuple sera tout à fait juste. Ils hériteront de la terre pour toujours, la branche de ma plantation, le travail de mes mains, afin que je sois glorifié.
22 Kabanja kakangʼono kadzasanduka fuko, kafuko kakangʼono kudzasanduka mtundu wamphamvu. Ine ndine Yehova, nthawi yake ikafika ndidzazichita zimenezi mofulumira.”
Le petit deviendra un millier, et la petite, une nation forte. Moi, Yahvé, je ferai cela rapidement en son temps. »

< Yesaya 60 >