< Yesaya 60 >
1 “Dzuka, wala, pakuti kuwala kwako kwafika, ndipo ulemerero wa Yehova wakuwalira.
Nouse, ole kirkas, sillä sinun valkeutesi tulee, ja Herran kunnia koittaa sinun ylitsesi.
2 Taona, mdima waphimba dziko lapansi ndipo mdima wandiweyani wagwa pa anthu a mitundu ina, koma Yehova adzakuwalira iwe, ndipo ulemerero wake udzaoneka pa iwe.
Sillä katso, pimeys peittää maan ja synkeys kansat, mutta sinun ylitsesi koittaa Herra, ja sinun ylläsi näkyy hänen kunniansa.
3 Mitundu ya anthu idzatsata kuwunika kwako ndipo mafumu adzalondola kunyezimira kwa mʼbandakucha wako.
Kansat vaeltavat sinun valkeuttasi kohti, kuninkaat sinun koitteesi kirkkautta kohti.
4 “Tukula maso ako, yangʼanayangʼana ndipo ona zimene zikuchitika. Onse akusonkhana ndipo akubwera kwa iwe; ana ako a amuna akubwera kuchokera kutali ndipo ana ako aakazi anyamulidwa mʼmanja.
Nosta silmäsi, katso ympärillesi: kaikki nämä ovat kokoontuneet, tulevat sinun tykösi; sinun poikasi tulevat kaukaa, sinun tyttäriäsi kainalossa kannetaan.
5 Ukadzaona zimenezi udzasangalala kwambiri, mtima wako udzalumpha ndi kudzaza ndi chimwemwe; chuma chakunyanja chidzabwera kwa iwe chuma cha mitundu ya anthu chidzabwera kwa iwe.
Silloin sinä saat sen nähdä, ja sinä loistat ilosta, sinun sydämesi sykkii ja avartuu, kun meren aarteet kääntyvät sinun tykösi, kansojen rikkaudet tulevat sinulle.
6 Gulu la ngamira lidzaphimba dziko lako, ngamira zingʼonozingʼono zidzachokera ku Midiyani ndi ku Efai. Ndipo onse a ku Seba adzabwera atanyamula golide ndi lubani uku akutamanda Yehova.
Kamelien paljous peittää sinut, Midianin ja Eefan varsat; kaikki tulevat Sabasta, kantavat kultaa ja suitsutusta ja Herran ylistystä ilmoittavat.
7 Ziweto zonse za ku Kedara adzazisonkhanitsa kwa inu, nkhosa zazimuna za ku Nabayoti zidzakutumikirani; zidzalandiridwa monga chopereka pa guwa langa la nsembe, ndipo ndidzakongoletsa Nyumba yanga.
Kaikki Keedarin laumat kokoontuvat sinun tykösi, Nebajotin oinaat palvelevat sinua; minulle otollisina ne nousevat minun alttarilleni, ja minä kirkastan kirkkauteni huoneen.
8 “Kodi ndi zayani izo zikuwuluka ngati mitambo, ngati kapena nkhunda zobwerera ku zisa zawo?
Keitä ovat nuo, jotka lentävät niinkuin pilvet ja niinkuin kyyhkyset lakkoihinsa?
9 Ndithu, izi ndi sitima za pa madzi zochokera ku mayiko akutali; patsogolo pali sitima zapamadzi za ku Tarisisi, zikubweretsa ana ako ochokera kutali, pamodzi ndi siliva wawo ndi golide wawo, kudzalemekeza Yehova Mulungu wako, Woyerayo wa Israeli, pakuti Iye wakuvekani inu ulemerero.
Merensaaret odottavat minua, ja etumaisina tulevat Tarsiin-laivat tuodakseen sinun lapsesi kaukaa; hopeansa ja kultansa heillä on mukanansa Herran, sinun Jumalasi, nimelle, Israelin Pyhälle, sillä hän kirkastaa sinut.
10 “Alendo adzamanganso malinga ako, ndipo mafumu awo adzakutumikira. Ngakhale ndinakukantha ndili wokwiya, koma tsopano ndidzakukomera mtima ndikukuchitira chifundo.
Ja muukalaiset rakentavat sinun muurisi, ja heidän kuninkaansa palvelevat sinua; sillä vihassani minä löin sinua, mutta mielisuosiossani minä sinua armahdan.
11 Zipata zako zidzakhala zotsekula nthawi zonse, sadzazitseka nthawi zonse, usana ndi usiku, kotero anthu adzabwera kwa iwe ndi chuma chawo, akuyenda pa mdipiti mafumu awo ali patsogolo.
Sinun porttisi pidetään aina auki, ei niitä suljeta päivällä eikä yöllä, että kansojen rikkaudet tuotaisiin ja heidän kuninkaansa saatettaisiin sinun tykösi.
12 Pakuti mtundu wa anthu ndi mafumu amene sakutumikira iwe; adzawonongeka kotheratu.
Sillä se kansa tai valtakunta, joka ei sinua palvele, hukkuu, ja ne kansat hävitetään perinjuurin.
13 “Adzabwera nayo kwa iwe mitengo ya payini, mkuyu ndi naphini imene ili mʼnkhalango ya Lebanoni kuti adzakongoletsere malo a nyumba yanga yopatulika; ndipo ndidzalemekeza malo amene Ine ndimapondapo.
Libanonin kunnia tulee sinun tykösi, kypressit, jalavat ynnä hopeakuuset, kaunistamaan minun pyhäkköni paikkaa, ja minä saatan jalkaini sijan kunniaan.
14 Ana aja amene anakuzunzani adzabwera ndipo adzakugwadirani; onse amene anakunyozani adzagwada pansi pa mapazi anu. Ndipo adzakutchani kuti Mzinda wa Yehova; Ziyoni mzinda wa Woyerayo wa Israeli.
Ja kumarassa käyden tulevat sinun tykösi sinun sortajaisi pojat, ja kaikki sinun pilkkaajasi heittäytyvät sinun jalkaisi juureen. He nimittävät sinut "Herran kaupungiksi", "Israelin Pyhän Siioniksi".
15 “Ngakhale anthu anakusiya nadana nawe, koma Ine ndidzakukuza mpaka muyaya, ndipo udzakhala malo a chimwemwe cha anthu amibado yonse.
Sen sijaan, että sinä olet ollut hyljätty ja vihattu, niin ettei ollut kauttasi kulkijaa, teen minä sinut korkeaksi iankaikkisesti, iloksi polvesta polveen.
16 Udzamwa mkaka wa mitundu ya anthu ndi kuleredwa pa maere aufumu, motero udzadziwa kuti Ine Yehova, ndine Mpulumutsi wako, Momboli wako ndiye Wamphamvu wa Yakobo.
Ja sinä saat imeä kansojen maidon, imeä kuningasten rintoja, saat tuntea, että minä, Herra, olen sinun auttajasi, että Jaakobin Väkevä on sinun lunastajasi.
17 Ndidzakupatsa golide mʼmalo mwa mkuwa, ndi siliva mʼmalo mwa chitsulo. Ndidzakupatsa mkuwa mʼmalo mwa thabwa ndi chitsulo mʼmalo mwa miyala. Olamulira ako adzakhala a mtendere. Ndidzasandutsa okulamulira kuti akhale achilungamo.
Minä tuon vasken sijaan kultaa, ja raudan sijaan minä tuon hopeata, puun sijaan vaskea ja kiven sijaan rautaa. Ja minä panen sinulle esivallaksi rauhan ja käskijäksi vanhurskauden.
18 Ziwawa sizidzamvekanso mʼdziko lako, bwinja kapena chiwonongeko sizidzapezeka mʼdziko lako, ndidzakhala malinga ako okuteteza ndipo udzanditamanda.
Ei kuulu enää väkivaltaa sinun maassasi, ei tuhoa, ei turmiota sinun rajaisi sisällä, ja sinä kutsut pelastuksen muuriksesi ja kiitoksen portiksesi.
19 Sipadzakhala dzuwa kuti likuwunikire, kapena mwezi kuti uwunikire usiku, pakuti Yehova ndiye adzakhale kuwunika kwako kwa muyaya, ndipo Mulungu wako adzakhala ulemerero wako.
Ei ole enää aurinko sinun valonasi päivällä, eikä valaise sinua kuun kumotus, vaan Herra on sinun iankaikkinen valkeutesi, ja sinun Jumalasi sinun kirkkautesi.
20 Dzuwa lako silidzalowanso, ndipo mwezi wako sudzazimiriranso; Yehova adzakhala kuwunika kwako kwamuyaya, ndipo masiku a mavuto ako adzatha.
Ei sinun aurinkosi enää laske, eikä sinun kuusi vajene, sillä Herra on sinun iankaikkinen valkeutesi, ja päättyneet ovat sinun murheesi päivät.
21 Ndipo anthu ako onse adzakhala olungama ndipo dzikolo lidzakhala lawo mpaka muyaya. Iwo ndi mphukira imene Ine ndayidzala, ntchito ya manja anga, kuti aonetse ulemerero wanga.
Sinun kansassasi ovat kaikki vanhurskaita, he saavat periä maan iankaikkisesti, he, minun istutukseni vesa, minun kätteni teko, minun kirkkauteni ilmoitukseksi.
22 Kabanja kakangʼono kadzasanduka fuko, kafuko kakangʼono kudzasanduka mtundu wamphamvu. Ine ndine Yehova, nthawi yake ikafika ndidzazichita zimenezi mofulumira.”
Pienimmästä kasvaa heimo, vähäisimmästä väkevä kansa. Minä, Herra, sen aikanansa nopeasti täytän.