< Yesaya 60 >
1 “Dzuka, wala, pakuti kuwala kwako kwafika, ndipo ulemerero wa Yehova wakuwalira.
Arise, be enlightened, O Jerusalem: for thy light is come, and the glory of the Lord is risen upon thee.
2 Taona, mdima waphimba dziko lapansi ndipo mdima wandiweyani wagwa pa anthu a mitundu ina, koma Yehova adzakuwalira iwe, ndipo ulemerero wake udzaoneka pa iwe.
For behold darkness shall cover the earth, and a mist the people: but the Lord shall arise upon thee, and his glory shall be seen upon thee.
3 Mitundu ya anthu idzatsata kuwunika kwako ndipo mafumu adzalondola kunyezimira kwa mʼbandakucha wako.
And the Gentiles shall walk in thy light, and kings in the brightness of thy rising.
4 “Tukula maso ako, yangʼanayangʼana ndipo ona zimene zikuchitika. Onse akusonkhana ndipo akubwera kwa iwe; ana ako a amuna akubwera kuchokera kutali ndipo ana ako aakazi anyamulidwa mʼmanja.
Lift up thy eyes round about, and see: all these are gathered together, they are come to thee: thy sons shall come from afar, and thy daughters shall rise up at thy side.
5 Ukadzaona zimenezi udzasangalala kwambiri, mtima wako udzalumpha ndi kudzaza ndi chimwemwe; chuma chakunyanja chidzabwera kwa iwe chuma cha mitundu ya anthu chidzabwera kwa iwe.
Then shalt thou see, and abound, and thy heart shall wonder and be enlarged, when the multitude of the sea shall be converted to thee, the. strength of the Gentiles shall come to thee.
6 Gulu la ngamira lidzaphimba dziko lako, ngamira zingʼonozingʼono zidzachokera ku Midiyani ndi ku Efai. Ndipo onse a ku Seba adzabwera atanyamula golide ndi lubani uku akutamanda Yehova.
The multitude of camels shall cover thee, the dromedaries of Madian and Epha: all they from Saba shall come, bringing gold and frankincense: and shewing forth praise to the Lord.
7 Ziweto zonse za ku Kedara adzazisonkhanitsa kwa inu, nkhosa zazimuna za ku Nabayoti zidzakutumikirani; zidzalandiridwa monga chopereka pa guwa langa la nsembe, ndipo ndidzakongoletsa Nyumba yanga.
All the flocks of Cedar shall be gathered together unto thee, the rams of Nabaioth shall minister to thee: they shall be offered upon my acceptable altar, and I will glorify the house of my majesty.
8 “Kodi ndi zayani izo zikuwuluka ngati mitambo, ngati kapena nkhunda zobwerera ku zisa zawo?
Who are these, that fly as clouds, and as doves to their windows?
9 Ndithu, izi ndi sitima za pa madzi zochokera ku mayiko akutali; patsogolo pali sitima zapamadzi za ku Tarisisi, zikubweretsa ana ako ochokera kutali, pamodzi ndi siliva wawo ndi golide wawo, kudzalemekeza Yehova Mulungu wako, Woyerayo wa Israeli, pakuti Iye wakuvekani inu ulemerero.
For, the islands wait for me, and the ships of the sea in the beginning: that I may bring thy sons from afar: their silver, and their gold with them, to the name of the Lord thy God, and to the Holy One of Israel, because he hath glorified thee.
10 “Alendo adzamanganso malinga ako, ndipo mafumu awo adzakutumikira. Ngakhale ndinakukantha ndili wokwiya, koma tsopano ndidzakukomera mtima ndikukuchitira chifundo.
And the children of strangers shall build up thy walls, and their kings shall minister to thee: for in my wrath have I struck thee, and in my reconciliation have I had mercy upon thee.
11 Zipata zako zidzakhala zotsekula nthawi zonse, sadzazitseka nthawi zonse, usana ndi usiku, kotero anthu adzabwera kwa iwe ndi chuma chawo, akuyenda pa mdipiti mafumu awo ali patsogolo.
And thy gates shall be open continually: they shall not be shut day nor night, that the strength of the Gentiles may be brought to thee, and their kings may be brought.
12 Pakuti mtundu wa anthu ndi mafumu amene sakutumikira iwe; adzawonongeka kotheratu.
For the nation and the kingdom that will not serve thee, shall perish: and the Gentiles shall be wasted with desolation.
13 “Adzabwera nayo kwa iwe mitengo ya payini, mkuyu ndi naphini imene ili mʼnkhalango ya Lebanoni kuti adzakongoletsere malo a nyumba yanga yopatulika; ndipo ndidzalemekeza malo amene Ine ndimapondapo.
The glory of Libanus shall come to thee, the Ar tree, and the box tree, and the pine tree together, to beautify the place of my sanctuary: and I will glorify the place of my feet.
14 Ana aja amene anakuzunzani adzabwera ndipo adzakugwadirani; onse amene anakunyozani adzagwada pansi pa mapazi anu. Ndipo adzakutchani kuti Mzinda wa Yehova; Ziyoni mzinda wa Woyerayo wa Israeli.
And the children of them that afflict thee, shall come bowing down to thee, and all that slandered thee shall worship the steps of thy feet, and shall call thee the city of the Lord, the Sion of the Holy One of Israel.
15 “Ngakhale anthu anakusiya nadana nawe, koma Ine ndidzakukuza mpaka muyaya, ndipo udzakhala malo a chimwemwe cha anthu amibado yonse.
Because thou wast forsaken, and hated, and there was none that passed through thee, I will make thee to be an everlasting glory, a joy unto generation and generation:
16 Udzamwa mkaka wa mitundu ya anthu ndi kuleredwa pa maere aufumu, motero udzadziwa kuti Ine Yehova, ndine Mpulumutsi wako, Momboli wako ndiye Wamphamvu wa Yakobo.
And thou shalt suck the milk of the Gentiles, and thou shalt be nursed with the breasts of kings: and thou shalt know that I am the Lord thy Saviour, and thy Redeemer, the Mighty One of Jacob.
17 Ndidzakupatsa golide mʼmalo mwa mkuwa, ndi siliva mʼmalo mwa chitsulo. Ndidzakupatsa mkuwa mʼmalo mwa thabwa ndi chitsulo mʼmalo mwa miyala. Olamulira ako adzakhala a mtendere. Ndidzasandutsa okulamulira kuti akhale achilungamo.
For brass I will bring gold, and for iron I will bring silver: and for wood brass, and for stones iron: and I will make thy visitation peace, and thy overseers justice.
18 Ziwawa sizidzamvekanso mʼdziko lako, bwinja kapena chiwonongeko sizidzapezeka mʼdziko lako, ndidzakhala malinga ako okuteteza ndipo udzanditamanda.
Iniquity shall no more be heard in thy land, wasting nor destruction in thy borders, and salvation shall possess thy walls, and praise thy gates.
19 Sipadzakhala dzuwa kuti likuwunikire, kapena mwezi kuti uwunikire usiku, pakuti Yehova ndiye adzakhale kuwunika kwako kwa muyaya, ndipo Mulungu wako adzakhala ulemerero wako.
Thou shalt no more have the sun for thy light by day, neither shall the brightness of the moon enlighten thee: but the Lord shall be unto thee for an everlasting light, and thy God for thy glory.
20 Dzuwa lako silidzalowanso, ndipo mwezi wako sudzazimiriranso; Yehova adzakhala kuwunika kwako kwamuyaya, ndipo masiku a mavuto ako adzatha.
Thy sun shall go down no more, and thy moon shall not decrease: for the Lord shall be unto thee for an everlasting light, and the days of thy mourning shall be ended.
21 Ndipo anthu ako onse adzakhala olungama ndipo dzikolo lidzakhala lawo mpaka muyaya. Iwo ndi mphukira imene Ine ndayidzala, ntchito ya manja anga, kuti aonetse ulemerero wanga.
And thy people shall be all just, they shall inherit the land for ever, the branch of my planting, the work of my hand to glorify me.
22 Kabanja kakangʼono kadzasanduka fuko, kafuko kakangʼono kudzasanduka mtundu wamphamvu. Ine ndine Yehova, nthawi yake ikafika ndidzazichita zimenezi mofulumira.”
The least shall become a thousand, and a little one a most strong nation: I the Lord will suddenly do this thing in its time.