< Yesaya 60 >

1 “Dzuka, wala, pakuti kuwala kwako kwafika, ndipo ulemerero wa Yehova wakuwalira.
興起,發光!因為你的光已經來到! 耶和華的榮耀發現照耀你。
2 Taona, mdima waphimba dziko lapansi ndipo mdima wandiweyani wagwa pa anthu a mitundu ina, koma Yehova adzakuwalira iwe, ndipo ulemerero wake udzaoneka pa iwe.
看哪,黑暗遮蓋大地, 幽暗遮蓋萬民, 耶和華卻要顯現照耀你; 他的榮耀要現在你身上。
3 Mitundu ya anthu idzatsata kuwunika kwako ndipo mafumu adzalondola kunyezimira kwa mʼbandakucha wako.
萬國要來就你的光; 君王要來就你發現的光輝。
4 “Tukula maso ako, yangʼanayangʼana ndipo ona zimene zikuchitika. Onse akusonkhana ndipo akubwera kwa iwe; ana ako a amuna akubwera kuchokera kutali ndipo ana ako aakazi anyamulidwa mʼmanja.
你舉目向四方觀看; 眾人都聚集來到你這裏。 你的眾子從遠方而來; 你的眾女也被懷抱而來。
5 Ukadzaona zimenezi udzasangalala kwambiri, mtima wako udzalumpha ndi kudzaza ndi chimwemwe; chuma chakunyanja chidzabwera kwa iwe chuma cha mitundu ya anthu chidzabwera kwa iwe.
那時,你看見就有光榮; 你心又跳動又寬暢; 因為大海豐盛的貨物必轉來歸你; 列國的財寶也必來歸你。
6 Gulu la ngamira lidzaphimba dziko lako, ngamira zingʼonozingʼono zidzachokera ku Midiyani ndi ku Efai. Ndipo onse a ku Seba adzabwera atanyamula golide ndi lubani uku akutamanda Yehova.
成群的駱駝, 並米甸和以法的獨峰駝必遮滿你; 示巴的眾人都必來到; 要奉上黃金乳香, 又要傳說耶和華的讚美。
7 Ziweto zonse za ku Kedara adzazisonkhanitsa kwa inu, nkhosa zazimuna za ku Nabayoti zidzakutumikirani; zidzalandiridwa monga chopereka pa guwa langa la nsembe, ndipo ndidzakongoletsa Nyumba yanga.
基達的羊群都必聚集到你這裏, 尼拜約的公羊要供你使用, 在我壇上必蒙悅納; 我必榮耀我榮耀的殿。
8 “Kodi ndi zayani izo zikuwuluka ngati mitambo, ngati kapena nkhunda zobwerera ku zisa zawo?
那些飛來如雲、 又如鴿子向窗戶飛回的是誰呢?
9 Ndithu, izi ndi sitima za pa madzi zochokera ku mayiko akutali; patsogolo pali sitima zapamadzi za ku Tarisisi, zikubweretsa ana ako ochokera kutali, pamodzi ndi siliva wawo ndi golide wawo, kudzalemekeza Yehova Mulungu wako, Woyerayo wa Israeli, pakuti Iye wakuvekani inu ulemerero.
眾海島必等候我, 首先是他施的船隻, 將你的眾子連他們的金銀從遠方一同帶來, 都為耶和華-你上帝的名, 又為以色列的聖者, 因為他已經榮耀了你。
10 “Alendo adzamanganso malinga ako, ndipo mafumu awo adzakutumikira. Ngakhale ndinakukantha ndili wokwiya, koma tsopano ndidzakukomera mtima ndikukuchitira chifundo.
外邦人必建築你的城牆; 他們的王必服事你。 我曾發怒擊打你, 現今卻施恩憐恤你。
11 Zipata zako zidzakhala zotsekula nthawi zonse, sadzazitseka nthawi zonse, usana ndi usiku, kotero anthu adzabwera kwa iwe ndi chuma chawo, akuyenda pa mdipiti mafumu awo ali patsogolo.
你的城門必時常開放, 晝夜不關; 使人把列國的財物帶來歸你, 並將他們的君王牽引而來。
12 Pakuti mtundu wa anthu ndi mafumu amene sakutumikira iwe; adzawonongeka kotheratu.
哪一邦哪一國不事奉你,就必滅亡, 也必全然荒廢。
13 “Adzabwera nayo kwa iwe mitengo ya payini, mkuyu ndi naphini imene ili mʼnkhalango ya Lebanoni kuti adzakongoletsere malo a nyumba yanga yopatulika; ndipo ndidzalemekeza malo amene Ine ndimapondapo.
黎巴嫩的榮耀, 就是松樹、杉樹、黃楊樹, 都必一同歸你, 為要修飾我聖所之地; 我也要使我腳踏之處得榮耀。
14 Ana aja amene anakuzunzani adzabwera ndipo adzakugwadirani; onse amene anakunyozani adzagwada pansi pa mapazi anu. Ndipo adzakutchani kuti Mzinda wa Yehova; Ziyoni mzinda wa Woyerayo wa Israeli.
素來苦待你的,他的子孫都必屈身來就你; 藐視你的,都要在你腳下跪拜。 他們要稱你為「耶和華的城」, 為「以色列聖者的錫安」。
15 “Ngakhale anthu anakusiya nadana nawe, koma Ine ndidzakukuza mpaka muyaya, ndipo udzakhala malo a chimwemwe cha anthu amibado yonse.
你雖然被撇棄被厭惡, 甚至無人經過, 我卻使你變為永遠的榮華, 成為累代的喜樂。
16 Udzamwa mkaka wa mitundu ya anthu ndi kuleredwa pa maere aufumu, motero udzadziwa kuti Ine Yehova, ndine Mpulumutsi wako, Momboli wako ndiye Wamphamvu wa Yakobo.
你也必吃萬國的奶, 又吃君王的奶。 你便知道我-耶和華是你的救主, 是你的救贖主,雅各的大能者。
17 Ndidzakupatsa golide mʼmalo mwa mkuwa, ndi siliva mʼmalo mwa chitsulo. Ndidzakupatsa mkuwa mʼmalo mwa thabwa ndi chitsulo mʼmalo mwa miyala. Olamulira ako adzakhala a mtendere. Ndidzasandutsa okulamulira kuti akhale achilungamo.
我要拿金子代替銅, 拿銀子代替鐵, 拿銅代替木頭, 拿鐵代替石頭; 並要以和平為你的官長, 以公義為你的監督。
18 Ziwawa sizidzamvekanso mʼdziko lako, bwinja kapena chiwonongeko sizidzapezeka mʼdziko lako, ndidzakhala malinga ako okuteteza ndipo udzanditamanda.
你地上不再聽見強暴的事, 境內不再聽見荒涼毀滅的事。 你必稱你的牆為「拯救」, 稱你的門為「讚美」。
19 Sipadzakhala dzuwa kuti likuwunikire, kapena mwezi kuti uwunikire usiku, pakuti Yehova ndiye adzakhale kuwunika kwako kwa muyaya, ndipo Mulungu wako adzakhala ulemerero wako.
日頭不再作你白晝的光; 月亮也不再發光照耀你。 耶和華卻要作你永遠的光; 你上帝要為你的榮耀。
20 Dzuwa lako silidzalowanso, ndipo mwezi wako sudzazimiriranso; Yehova adzakhala kuwunika kwako kwamuyaya, ndipo masiku a mavuto ako adzatha.
你的日頭不再下落; 你的月亮也不退縮; 因為耶和華必作你永遠的光。 你悲哀的日子也完畢了。
21 Ndipo anthu ako onse adzakhala olungama ndipo dzikolo lidzakhala lawo mpaka muyaya. Iwo ndi mphukira imene Ine ndayidzala, ntchito ya manja anga, kuti aonetse ulemerero wanga.
你的居民都成為義人, 永遠得地為業; 是我種的栽子,我手的工作, 使我得榮耀。
22 Kabanja kakangʼono kadzasanduka fuko, kafuko kakangʼono kudzasanduka mtundu wamphamvu. Ine ndine Yehova, nthawi yake ikafika ndidzazichita zimenezi mofulumira.”
至小的族要加增千倍; 微弱的國必成為強盛。 我-耶和華要按定期速成這事。

< Yesaya 60 >