< Yesaya 6 >
1 Chaka chimene mfumu Uziya anamwalira, ndinaona Ambuye atakhala pa mpando waufumu, wautali ndi wokwezedwa, ndipo mkanjo wawo unali wautali; kotero kuti unadzaza mʼNyumba ya Yehova.
V letu, ko je kralj Uzíjah umrl, sem videl tudi Gospoda sedeti na prestolu, visokega in dvignjenega in njegova vlečka je napolnila tempelj.
2 Pamwamba pawo panayimirira Aserafi, aliyense anali ndi mapiko asanu ndi limodzi: awiri anaphimba nkhope zawo, awiri anaphimba mapazi awo, ndipo awiri ankawulukira.
Nad njim so stali serafi. Vsak je imel šest peruti. Z dvema je pokril svoj obraz in z dvema je pokril svoja stopala in z dvema je letel.
3 Ndipo Aserafiwo amafuwulirana kuti “Woyera, woyera, woyera Yehova Wamphamvuzonse. Dziko lonse lapansi ladzaza ndi ulemerero wake.”
Eden je vzklikal drugemu in govoril: »Svet, svet, svet je Gospod nad bojevniki. Celotna zemlja je polna njegove slave.«
4 Chifukwa cha kufuwulako maziko a zitseko ndi ziwundo anagwedezeka ndipo mʼNyumba ya Yehova munadzaza utsi.
Podboji vrat so se premaknili ob glasu tistega, ki je vpil in hiša je bila napolnjena z dimom.
5 Tsono ine ndinafuwula kuti, “Tsoka langa ine! Ndatayika! Pakuti ndine munthu wapakamwa poyipa, ndipo ndimakhala pakati pa anthu a pakamwa poyipa, ndipo ndi maso anga ndaona mfumu Yehova Wamphamvuzonse.”
Potem sem rekel: »Gorje meni! Kajti onemel sem, ker sem človek nečistih ustnic in prebivam v sredi ljudstva nečistih ustnic, kajti moje oči so videle kralja, Gospoda nad bojevniki.«
6 Pomwepo mmodzi mwa Aserafi aja anawulukira kwa ine ali ndi khala lamoto mʼdzanja lake, khala limene analichotsa ndi mbaniro pa guwa lansembe.
Potem je priletel k meni eden izmed serafov, ki je imel v svoji roki žerjavico, ki jo je s kleščami vzel od oltarja.
7 Ndipo anandikhudza pakamwa panga ndi khala lamotolo nati, “Taona ndakhudza pa milomo yako ndi khalali; kulakwa kwako kwachotsedwa, machimo ako akhululukidwa.”
To je položil na moja usta in rekel: »Glej, to se je dotaknilo tvojih ustnic in tvoja krivičnost je odvzeta proč in tvoj greh je očiščen.«
8 Kenaka ndinamva mawu a Ambuye akuti, “Kodi ndidzatuma yani? Ndipo ndani adzapite mʼmalo mwathu?” Ndipo ine ndinati, “Ndilipo. Tumeni!”
Slišal sem tudi glas od Gospoda, rekoč: »Koga naj pošljem in kdo bo šel za nas?« Potem sem rekel: »Tukaj sem, pošlji mene.«
9 Yehova anati, “Pita ndipo ukawawuze anthu awa: “‘Kumva muzimva, koma osamvetsetsa; kupenya muzipenya koma osaona kanthu.’
Rekel je: »Pojdi in povej temu ljudstvu: ›Resnično, poslušajte, toda ne razumite in resnično glejte, pa ne zaznajte.
10 Tsono anthu amenewa uwaphe mtima; uwagonthetse makutu, ndipo uwatseke mʼmaso. Mwina angaone ndi maso awo, angamve ndi makutu awo, angamvetse ndi mitima yawo, kenaka ndi kutembenuka mtima ndi kuchiritsidwa.”
Naredi srce tega ljudstva debelo in njihova ušesa naredi težka in zapri njihove oči, da ne bi videli s svojimi očmi in [ne bi] slišali s svojimi ušesi in [ne bi] razumeli s svojim srcem in ne bi bili spreobrnjeni in ne bi bili ozdravljeni.‹«
11 Pamenepo ine ndinati, “Zimenezo ndi mpaka liti Inu Ambuye?” Ndipo Iyeyo anandiyankha kuti, “Mpaka mizinda itasanduka mabwinja nʼkusowa wokhalamo, mpaka nyumba zitasowa anthu okhalamo, mpaka dziko litasanduka chipululu ndithu,
Tedaj sem rekel: »Gospod, doklej?« Odgovoril je: »Dokler ne bodo mesta opustošena, brez prebivalca in hiše brez človeka in ne bo dežela popolnoma zapuščena
12 mpaka Yehova atasamutsira aliyense kutali, dziko nʼkusiyidwa kwathunthu.
in Gospod je ljudi odstranil daleč proč in tam bo veliko zapuščanja v sredi dežele.
13 Ndipo ngakhale chigawo chakhumi cha anthu chitatsala mʼdziko, nachonso chidzawonongedwa. Koma monga momwe mitengo ya muwanga ndi thundu imasiyira chitsa pamene ayidula, chonchonso mbewu yoyera idzatsalira ngati chitsa chotsala mʼdziko.”
Toda vendar bo v njej desetina in ta se bo vrnila in bo požrta; kakor terebinta in kakor hrast, katerega snov je v njiju, ko odvržeta svoje listje, tako bo sveto seme snov le-tega.«